Ezekieli 38 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 38:1-23

Za Chilango cha Gogi

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu. 3Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala. 4Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola. 5Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo. 6Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.

7“ ‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo. 8Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere. 9Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.

10“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa. 11Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo. 12Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’ 13Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’ ”

14“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka. 15Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu. 16Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.

17“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli. 18Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. 19Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli. 20Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi. 21Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga. 22Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye. 23Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’ ”

La Bible du Semeur

Ezéchiel 38:1-23

Le futur ennemi du peuple de Dieu et sa fin

Comme un ouragan

1L’Eternel m’adressa la parole en ces termes :

2Fils d’homme, tourne tes regards vers Gog au pays de Magog, prince suprême38.2 suprême: certains traduisent : de Rosh. De même au verset 3 et en 39.1. de Méshek et de Toubal38.2 Méshek et Toubal, déjà cités en 27.13, sont des pays situés aux environs du Caucase, sur les bords de la mer Noire, en Asie Mineure. Gog et Magog: voir Gn 10.2-3 ; Ap 20.8. ! Prophétise contre lui 3et dis : « Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Je m’en prends à toi, Gog, prince suprême de Méshek ainsi que de Toubal. 4Je te ferai faire demi-tour, je te mettrai des crochets aux mâchoires, je te ferai sortir, toi et toute ton armée, tes chevaux et tes équipages, tous superbement revêtus et formant une troupe nombreuse, portant le grand et le petit bouclier, maniant l’épée. 5Perses, Ethiopiens et ceux de Pouth38.5 Voir Gn 10.6 et note. les rejoindront, tous équipés de casques et de boucliers. 6Gomer et toutes ses légions, et le peuple de Togarma38.6 Tous ces peuples viennent du nord. Selon Gn 10.3 et 1 Ch 1.6, Togarma était un fils de Gomer. aux confins du septentrion et toutes ses légions, des peuples innombrables, seront tes auxiliaires.

7Prends tes dispositions et tiens-toi prêt, toi et toutes tes troupes groupées autour de toi. Tu seras leur commandant. 8Au bout de bien des jours, tu seras appelé au combat ; dans la suite des temps, tu iras envahir un pays dont les habitants auront échappé à l’épée et auront été rassemblés d’entre beaucoup de peuples sur les montagnes d’Israël qui étaient si longtemps en ruine. Cette population qu’on aura fait sortir du milieu d’autres peuples habitera entièrement dans la sécurité. 9Tu montes, tu arrives comme un ouragan qui s’abat, comme un nuage qui va couvrir la terre, toi et tous tes bataillons et les peuples nombreux qui marchent avec toi.

10Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : En ce jour-là, des projets naîtront dans ton cœur, tu concevras un dessein criminel, 11et tu diras : “Je vais attaquer un pays ouvert, et j’arriverai chez des gens qui vivent tranquilles dans la sécurité, habitant dans des villes sans remparts, sans verrous, et qui n’ont pas de portes.” 12Tu iras pour piller et faire du butin, et pour porter la main sur des lieux auparavant désolés, maintenant habités, contre ce peuple rassemblé d’entre les autres peuples, ayant des troupeaux et des biens, qui habitera à présent au centre de ce monde38.12 C’est-à-dire en Israël, à Jérusalem (voir 5.5).. 13Ceux de Séba et de Dedân38.13 Peuples commerçants d’Arabie., les marchands de Tarsis et tous ses princes38.13 Le texte hébreu a : ses lionceaux, terme qui désigne les rois en 19.1-9. L’ancienne version grecque a : les villages qui en dépendent. te diront alors : “Est-ce donc pour piller, pour faire du butin, que tu as rassemblé tout cet amas de troupes et que tu es venu ? Est-ce pour enlever l’argent et pour emporter l’or, pour prendre les troupeaux et t’emparer des biens, pour faire un grand pillage ?” »

14C’est pourquoi, toi, fils d’homme, prophétise et va dire à Gog : « Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Assurément, en ce temps-là où mon peuple Israël habitera là-bas dans la sécurité, tu en auras connaissance38.14 Au lieu de tu en auras connaissance, l’ancienne version grecque porte : tu te mettras en branle.. 15Tu quitteras le lieu où tu seras alors aux confins du septentrion, toi et les nombreux peuples qui seront tes alliés, tous montés à cheval, grande coalition et armée innombrable, 16et tu viendras attaquer mon peuple Israël comme un nuage qui vient couvrir la terre. Je te ferai venir attaquer mon pays dans les temps de la fin afin que les autres peuples apprennent à connaître qui je suis, quand par mes actes envers toi je démontrerai à leurs yeux ma sainteté, ô Gog.

Appelé par Dieu – détruit par lui

17Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : N’est-ce pas toi dont j’ai parlé il y a bien longtemps par les prophètes d’Israël, mes serviteurs, qui ont prophétisé, déjà en ce temps-là et pendant des années, que je te ferais venir pour combattre mon peuple ?

18En ce jour-là, au jour où Gog pénétrera sur le sol d’Israël, c’est là ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : La colère me montera jusqu’au visage. 19Dans ma passion et dans ma colère ardente, je le déclare, un grand tremblement de terre surviendra, en ce jour-là, au pays d’Israël. 20Devant moi trembleront les poissons de la mer, les oiseaux, les bêtes sauvages, tous les animaux qui rampent sur le sol, les insectes, et tout homme qui vit sur la surface de la terre. Les montagnes s’écrouleront, les falaises s’affaisseront, et toutes les murailles s’effondreront à terre. 21Je susciterai alors la guerre contre Gog sur toutes mes montagnes, c’est là ce que déclare le Seigneur, l’Eternel, et ils s’entretueront, chacun tirant l’épée contre son camarade. 22J’exercerai mon jugement contre lui par la peste et le sang, et je ferai tomber une forte pluie, des grêlons, du feu et du soufre, sur lui, sur ses légions et sur les peuples nombreux qui seront avec lui. 23Je manifesterai ma grandeur et ma sainteté, je me ferai connaître à de nombreux peuples et ils reconnaîtront que je suis l’Eternel. »