Ezekieli 37 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 37:1-28

Chigwa cha Mafupa Owuma

1Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa. 2Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri. 3Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?”

Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”

4Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova! 5Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo. 6Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

7Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake. 8Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.

9Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’ 10Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”

11Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’ 12Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli. 13Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo. 14Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’ ”

Dziko Limodzi Kutsogoleredwa ndi Mfumu Imodzi

15Yehova anandiyankhula kuti: 16“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’ 17Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.

18“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi 19iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’ 20Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse, 21udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo. 22Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri. 23Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.

24“ ‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga. 25Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya. 26Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya. 27Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga. 28Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’ ”

New Russian Translation

Иезекииль 37:1-28

Долина сухих костей

1Рука Господа была на мне. Он вывел меня Духом Господа и поставил посреди долины; она была полна костей. 2Он повел меня посреди них, и я увидел великое множество костей, лежавших в долине, и они были очень сухими. 3Он спросил меня:

– Сын человеческий, могут ли эти кости ожить?

Я ответил:

– Владыка Господи, это знаешь Ты один.

4Тогда Он сказал мне:

– Пророчествуй этим костям и скажи им: «Сухие кости, слушайте слово Господа! 5Так говорит этим костям Владыка Господь: Я пошлю в вас дыхание37:5 Или: «дух»; или: «ветер»; также в ст. 6–14., и вы оживете. 6Я прилажу к вам сухожилия, наращу на вас плоть и покрою кожей; Я вложу в вас дыхание, и вы оживете. Тогда вы узнаете, что Я – Господь».

7Я стал пророчествовать, как мне было велено. Когда я пророчествовал, раздался шум, постукивание, и кости начали сходиться – кость с костью. 8Я видел, как на них появились сухожилия и плоть, и как их покрыла кожа, но в них не было дыхания. 9Тогда Он сказал мне:

– Пророчествуй дыханию. Пророчествуй, сын человеческий, и скажи ему: «Так говорит Владыка Господь: Приди с четырех ветров, о дыхание, и вдохни в этих убитых, чтобы они ожили».

10Я начал пророчествовать, как Он повелел мне, и в них вошло дыхание. Они ожили и встали на ноги, это несметное войско. 11Тогда Он сказал мне:

– Сын человеческий, эти кости – весь дом Израиля. Они говорят: «Наши кости высохли, и надежда исчезла. С нами покончено». 12Поэтому пророчествуй и скажи им: «Так говорит Владыка Господь: Мой народ, Я открою ваши могилы и подниму вас из них. Я приведу вас в землю Израиля. 13И вы, Мой народ, узнаете, что Я – Господь, когда Я открою ваши могилы и выведу вас из них. 14Я вложу в вас Моего Духа37:14 Или: «Мое дыхание». и вы будете жить, а Я поселю вас в вашей земле. Тогда вы узнаете, что Я, Господь, сказал это и исполнил», – возвещает Господь.

Один народ и один царь

15Было ко мне слово Господне:

16– Сын человеческий, возьми деревянный брусок и напиши на нем: «Иудея и израильтяне, что с ней в союзе». Потом возьми другой брусок и напиши на нем: «Брусок Ефрема, что принадлежит Иосифу и всему дому Израиля, что с ним в союзе». 17Приложи их один к другому, чтобы у тебя в руке они стали единым целым.

18Когда твои соплеменники спросят тебя: «Не объяснишь ли нам, что это значит?» – 19скажи им: Так говорит Владыка Господь: «Я возьму брусок Иосифа и израильских родов, что с ним в союзе (он в руке Ефрема), и приложу к бруску Иудеи, сделав из них один брусок, и в Моей руке они станут единым целым». 20Держи перед глазами бруски, на которых ты сделал надпись, 21и скажи им: «Так говорит Владыка Господь: Я выведу израильтян из народов, к которым они ушли, соберу их отовсюду и приведу в их землю. 22В этой земле, на горах Израиля, Я сделаю их одним народом. У них будет один Царь, и они не будут больше двумя народами и не разделятся больше на два царства. 23Впредь они не станут оскверняться ни идолами, ни гнусными истуканами, ни другими своими преступлениями. Я спасу их из всех жилищ, где они грешили37:23 Во многих рукописях еврейского текста и в одном из древних переводов: «Я спасу их от их отступничества, в которое они впали»., и очищу их. Они будут Моим народом, а Я буду их Богом.

24Их царем станет Мой слуга Давид, и у всех у них будет один пастух. Они будут следовать Моим законам и бережно исполнять Мои установления. 25Они будут жить в земле, которую Я отдал Моему слуге Иакову, в земле, где жили их предки. Они сами, их дети и дети детей будут жить там вечно, и Мой слуга Давид навеки будет их правителем. 26Я заключу с ними завет мира; этот завет будет вечным. Я утвержу их на их земле и умножу их число. Я поставлю Мое святилище среди них навеки. 27У них будет Мое жилище. Я буду их Богом, а они будут Моим народом. 28И народы узнают, что Я, Господь, освящаю Израиль, когда Мое святилище встанет среди них навеки».