Ezekieli 35 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 35:1-15

Za Chilango cha Edomu

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo 3awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu. 4Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

5“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake. 6Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola. 7Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko. 8Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse. 9Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

10“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo. 11Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo. 12Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’ 13Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva. 14Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja. 15Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Езекиил 35:1-15

Пророчество об Эдоме

1Было ко мне слово Вечного:

2– Смертный, обрати лицо к горе Сеир35:2 Сеир – горная страна, также известна как Эдом, земля потомков Эсова, брата Якуба.; пророчествуй против неё 3и скажи: Так говорит Владыка Вечный: «Я твой противник, гора Сеир. Я подниму на тебя руку и предам тебя полному опустошению. 4Я превращу твои города в руины, и ты станешь необитаемой. Тогда ты узнаешь, что Я – Вечный.

5За то, что ты питала вечную вражду и предавала исроильтян мечу во время их беды, когда пробил час их наказания, 6за это, верно, как и то, что Я живу, – возвещает Владыка Вечный, – Я предам тебя кровопролитию, и оно будет преследовать тебя. Так как ты не возненавидела кровопролитие, оно будет тебя преследовать. 7Я предам гору Сеир полному опустошению и погублю на ней всех, кто уходит и возвращается. 8Я покрою твои вершины павшими; сражённые мечом будут падать на твоих холмах, в долинах и во всех ущельях. 9Я предам тебя вечному опустошению; твои города больше не будут заселены. Тогда ты узнаешь, что Я – Вечный.

10За то, что ты сказала: „Оба этих народа и обе эти страны будут моими; я завладею ими“, хотя с ними был Вечный, 11за это, верно, как и то, что Я живу, – возвещает Владыка Вечный, – Я поступлю с тобой по злобе и зависти, которые ты выказала, враждуя с ними, и явлю Себя им, когда стану тебя судить. 12Тогда ты узнаешь, что Я, Вечный, услышал все оскорбления, которые ты слала горам Исроила. Ты говорила: „Они опустошены и отданы мне на съедение!“ 13Ты хвасталась предо Мной и говорила против Меня, не сдерживаясь, и Я это услышал. 14Так говорит Владыка Вечный: Когда вся земля будет радоваться, Я предам тебя опустошению. 15За то, что ты радовалась опустошению наследия Исроила, Я поступлю с тобой точно так же. Ты будешь опустошена, гора Сеир, и с тобой – весь Эдом. Тогда узнают, что Я – Вечный».