Ezekieli 32 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 32:1-32

Nyimbo ya Maliro a Farao

1Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti,

“Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu.

Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja.

Umakhuvula mʼmitsinje yako,

kuvundula madzi ndi mapazi ako

ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.

3“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri,

ndidzakuponyera khoka langa

ndi kukugwira mu ukonde wanga.

4Ndidzakuponya ku mtunda

ndi kukutayira pansi.

Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe,

ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.

5Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri

ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.

6Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako,

mpaka kumapiri komwe,

ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.

7Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba

ndikudetsa nyenyezi zake.

Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo,

ndipo mwezi sudzawala.

8Zowala zonse zamumlengalenga

ndidzazizimitsa;

ndidzachititsa mdima pa dziko lako,

akutero Ambuye Yehova.

9Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri

pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,

ku mayiko amene iwe sunawadziwe.

10Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe,

ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe

pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo.

Pa nthawi ya kugwa kwako,

aliyense wa iwo adzanjenjemera

moyo wake wonse.

11“ ‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti,

“ ‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni

lidzabwera kudzalimbana nawe.

12Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe

ndi lupanga la anthu amphamvu,

anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu.

Adzathetsa kunyada kwa Igupto,

ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.

13Ndidzawononga ziweto zake zonse

zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri.

Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu

kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.

14Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake

ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta,

akutero Ambuye Yehova.

15Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja;

ndikadzawononga dziko lonse

ndi kukantha onse okhala kumeneko,

adzadziwa kuti ndine Yehova.’

16“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”

17Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti: 18“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa. 19Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’ 20Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo. 21Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’

22“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo. 23Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.

24“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. 25Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.

26“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. 27Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo.

28“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.

29“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.

30“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.

31“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 32Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

Nueva Versión Internacional

Ezequiel 32:1-32

Lamento por el faraón

1El día primero del mes duodécimo del año duodécimo, el Señor me dirigió la palabra: 2«Hijo de hombre, entona este lamento dedicado al faraón, rey de Egipto:

»“Pareces un león entre las naciones;

eres semejante a un monstruo marino

chapoteando en el río;

con tus patas enturbias el agua

y revuelves sus corrientes.

3»”Así dice el Señor y Dios:

»” Aunque estés entre numerosos pueblos,

tenderé sobre ti mi red

y te atraparé con ella.

4Te arrastraré por tierra

y en pleno campo te dejaré tendido.

Dejaré que sobre ti se posen

todas las aves del cielo.

Dejaré que con tu carne

se sacien todas las bestias de la tierra.

5Desparramaré tu carne por los montes

y con tu carroña llenaré los valles.

6Con tu sangre empaparé la tierra

hasta la cima de las montañas;

con tu sangre llenaré los canales de los ríos.

7Cuando te hayas consumido,

haré que el cielo se oscurezca

y se apaguen las estrellas;

cubriré el sol con una nube,

y no brillará más la luna.

8Todos los astros brillantes de los cielos,

los oscureceré sobre ti;

traeré oscuridad sobre la tierra,

afirma el Señor y Dios.

9Yo turbaré el corazón de muchos pueblos

cuando provoque tu destrucción,

aún entre las naciones que no conocías.

10Haré que por ti muchos pueblos queden consternados.

Cuando yo esgrima mi espada delante de ellos,

sus reyes se estremecerán.

En el día de tu caída,

en todo momento temblarán de miedo

por temor a perder la vida.

11»”Así dice el Señor y Dios:

»”La espada del rey de Babilonia

vendrá contra ti.

12Haré que tus multitudes caigan a filo de espada,

empuñada por los guerreros

más crueles entre las naciones.

Ellos arrasarán la soberbia de Egipto

y toda su multitud será derrotada.

13Voy a destruir todo el ganado

que pasta junto a las aguas abundantes;

nunca más serán enturbiadas

por hombres ni animales.

14Entonces dejaré que las aguas se asienten

y que corran tranquilas, como el aceite,

afirma el Señor y Dios.

15Cuando deje en ruinas a Egipto,

la despoje de todo lo que hay en su tierra

y hiera a todos los que la habitan,

entonces sabrán que yo soy el Señor ”.

16»Este es el lamento que las ciudades de las naciones entonarán sobre Egipto y toda su multitud, afirma el Señor y Dios».

17En el día quince del mes duodécimo del año duodécimo, el Señor me dirigió la palabra: 18«Hijo de hombre, entona un lamento sobre las multitudes de Egipto y, junto con las ciudades de las naciones más poderosas, hazlas descender con los que bajan a la fosa, a las regiones más profundas. 19Pregúntales: “¿Se creen acaso más privilegiados que otros? ¡Pues bajen y tiéndanse entre los paganos!”.32:19 paganos. Lit. incircuncisos. 20Y caerán entre los que murieron a filo de espada. Ya tienen la espada en la mano: ¡que se arrastre a Egipto y a sus multitudes! 21Allí en los dominios de la muerte,32:21 los dominios de la muerte. Lit. el Seol. los guerreros más fuertes y valientes hablarán de Egipto y de sus aliados. Y dirán: “¡Ya han descendido! ¡Yacen tendidos entre los paganos que murieron a filo de espada!”.

22»Allí está Asiria, con toda su multitud en torno a su sepulcro. Todos ellos murieron a filo de espada. 23Todos los que sembraban el terror en la tierra de los vivientes yacen muertos, víctimas de la espada. Ahora están sepultados en lo más profundo de la fosa, tendidos alrededor de su tumba.

24»Allí está Elam, con toda su multitud en torno a su sepulcro. Todos ellos murieron a filo de espada. Todos los que sembraban el terror en la tierra de los vivientes bajaron como paganos a lo más profundo de la fosa. Yacen tendidos sin honor entre los que descendieron a la fosa. 25A Elam le han preparado una cama en medio de los muertos, entre los paganos que murieron a filo de espada y que ahora rodean su tumba. Ellos sembraron el terror en la tierra de los vivientes, pero ahora yacen tendidos sin honor entre los que descendieron a la fosa. Allí quedaron, entre gente que murió asesinada.

26»Allí están Mésec y Tubal, con toda su multitud en torno a su sepulcro. Todos ellos son paganos, muertos a filo de espada porque sembraron el terror en la tierra de los vivientes. 27No yacen con los héroes caídos de entre los paganos, que bajaron a los dominios de la muerte con sus armas de guerra y que tienen sus espadas bajo la cabeza. El castigo de sus pecados cayó sobre sus huesos, porque estos héroes sembraron el terror en la tierra de los vivientes.

28»Ahí estarás tú, faraón, en medio de los paganos, abatido y sepultado junto con los que murieron a filo de espada.

29»Allí está Edom, con sus reyes y príncipes. A pesar de todo su poder, también ellos yacen tendidos junto a los que murieron a filo de espada. Yacen entre los paganos, con los que descendieron a la fosa.

30»Allí están todos los príncipes del norte, y todos los de Sidón. A pesar del terror que sembraron con su poderío, también ellos bajaron, envueltos en deshonra, con los que murieron a filo de espada. Son paganos, y ahora yacen tendidos entre los que murieron a filo de espada, en medio de los que descendieron a la fosa.

31»El faraón los verá y se consolará de la muerte de toda su gente, pues él y todo su ejército morirán a filo de espada, afirma el Señor y Dios. 32Aunque yo hice que el faraón sembrara el terror en la tierra de los vivientes, él y todo su ejército serán sepultados entre los paganos, con los que murieron a filo de espada, afirma el Señor y Dios».