Ezekieli 31 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 31:1-18

Mkungudza mu Lebanoni

1Pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu, chaka cha khumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, unene kwa Farao mfumu ya Igupto ndi gulu lake lankhondo. Awawuze kuti,

“ ‘Kodi mu ukulu wanu ndani angafanane ndi inu?

3Taonani, ndidzakufanizirani ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni,

wa nthambi zokongola zochititsa mthunzi mʼnkhalango.

Unali wautali,

msonga zake zooneka pamwamba pa nkhalango.

4Madzi ndiwo ankawukulitsa mkungudzawo,

akasupe ozama ankawutalikitsa.

Mitsinje yake inkayenda

mozungulira malo amene unaliwo

ndipo ngalande zake zinkafika

ku mitengo yonse ya mʼmunda.

5Choncho unatalika kwambiri

kupambana mitengo yonse ya mʼmunda.

Nthambi zake zinachuluka

ndi kutalika kwambiri,

chifukwa inkalandira madzi ambiri.

6Mbalame zonse zamlengalenga

zinkamanga zisa zake mʼnthambi za mtengowo.

Nyama zakuthengo zonse

zinkaswanirana mʼmunsi mwa nthambi zake.

Mitundu yotchuka ya anthu

inkakhala mu mthunzi wake.

7Unali wokongola kwambiri,

wa nthambi zake zotambalala,

chifukwa mizu yake inazama pansi

kumene kunali madzi ochuluka.

8Mʼmunda wa Mulungu munalibe

mkungudza wofanana nawo,

kapena mitengo ya payini

ya nthambi zofanafana ndi nthambi zake.

Munalibenso mtengo wa mkuyu

nthambi zofanafana ndi zake.

Mʼmunda wa Mulungu munalibe mtengo wina uliwonse

wofanana ndi iwo kukongola kwake.

9Ine ndinawupanga wokongola

wa nthambi zochuluka.

Mitengo yonse ya mu Edeni, mʼmunda wa

Mulungu inawuchitira nsanje.

10“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Chifukwa kuti mtengowo unatalika kwambiri, unatulutsa songa zake mpaka ku thambo, ndipo unadzikweza chifukwa cha msinkhu wake, 11ndinawupereka mʼdzanja la mfumu ya mitundu ya anthu kuti awulange molingana ndi kuyipa kwake. 12Anthu ankhanza kwambiri amitundu ya anthu achilendo adzawudula ndi kuwusiya. Nthambi zake zidzagwera pa mapiri ndi mu zigwa zonse. Nthambi zake zidzathyokera mʼmitsinje ya mʼdzikomo. Motero mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi amene ankasangalala mu mthunzi wake idzawusiya. 13Mbalame zonse zamlengalenga zidzakhala pa mtengo wakugwawo, ndipo nyama zakuthengo zonse zidzakhala pa nthambi zake. 14Zidzakutero kuti pasakhalenso mitengo inanso ya mʼmbali mwa madzi yotalika kwambiri, imene idzatalike kwambiri ndi songa zake kufika mpaka ku mitambo. Komanso kuti pasadzakhalenso mitengo yolandira bwino madzi, imene idzatalika motero. Paja yonseyo kutha kwake ndi kufa, kupita ku dziko lapansi kukhala ndi anthu akufa amene analowa mʼmanda kale.

15“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. 16Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. 17Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu.

18“ ‘Ndi mitengo iti ya mu Edeni imene ingafanane ndi kukongola kwako ndi ulemerero wako? Komabe iwenso, udzatsikira ku dziko la anthu akufa pamodzi ndi mitengo ya mu Edeni. Udzagona pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, anthu amene anaphedwa pa nkhondo.

“ ‘Mtengowo ndi Farao ndi gulu lake lankhondo, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 31:1-18

香柏樹的比喻

1第十一年三月一日,耶和華對我說: 2「人子啊,你要對埃及王法老和他的百姓說,

『誰能比你強大呢?

3看啊,亞述曾是黎巴嫩的一棵香柏樹,

枝繁葉茂,遮天蔽日,

高聳入雲。

4它在河流和深泉的滋潤下茁壯成長,

溪流四圍環繞它,

澆灌著林間的樹木。

5充足的水源使它高過田間所有的樹木,

枝子長得又粗又長。

6空中的飛鳥都在它的枝頭上搭窩,

田間的野獸都在它的樹蔭下生產,

所有的大國都住在它的蔭下。

7它高大美麗,枝幹修長,

因為樹根深入水源,

8連上帝園中的香柏樹也不能與它相比。

松樹不能與它的枝幹相比,

楓樹不能與它的枝條相比,

主耶和華園中的樹木沒有一棵能與它媲美。

9我使它枝繁葉茂,美麗無比,

以致上帝伊甸園裡的樹木都羡慕它。』

10「因此,主耶和華說,『因為它樹幹高大,樹梢高聳入雲,心高氣傲, 11我要把它交在列國的首領手裡,他必按照它的邪惡懲治它。我丟棄了它。 12外族人,就是列邦中最殘暴的人要把它砍倒,丟棄在那裡,它折斷的枝幹散落在山間和河谷中。世上各族都離開它的蔭下, 13天上的飛禽要棲身在那折斷的樹幹上,地上的走獸要躺臥在它的枝條中。 14故此,水邊的樹木都不再傲然矗立,高聳入雲,水源充足的大樹也不再如此高大,因為它們都註定要與下墳墓的人一同死亡,落到陰間的深處。』

15「主耶和華說,『它下到陰間的那天,我要使哀聲響起,使深淵閉塞,江河止息,洪水停滯。我要使黎巴嫩為它哀哭,田野的樹木因它而枯萎。 16我將它與下墳墓的人一同拋到陰間時,列國聽見它墜落的響聲,都恐懼戰抖。伊甸園中的樹木和黎巴嫩水源充足、上好的樹木都在陰間得到安慰。 17在它蔭庇下做它爪牙的盟友都與它一同落到陰間,到被殺的人那裡。

18「『伊甸園的樹木中,誰能與你的威榮相比呢?然而你卻要與伊甸園的樹木一同下到陰間,躺臥在未受割禮的人當中,與被殺的人在一起。

「『這就是法老和他百姓的結局。這是主耶和華說的。』」