Ezekieli 30 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 30:1-26

Za Kulangidwa kwa Igupto

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,

‘Kalanga, tsiku lafika!’

3Pakuti tsiku layandikira,

tsiku la Yehova lili pafupi,

tsiku la mitambo yakuda,

tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.

4Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto

ndipo mavuto adzafika pa Kusi.

Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,

chuma chake chidzatengedwa

ndipo maziko ake adzagumuka.

5Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

6“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa

ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.

Adzaphedwa ndi lupanga

kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”

ndikutero Ine Ambuye Yehova.

7“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja

kupambana mabwinja ena onse opasuka,

ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka

kupambana mizinda ina yonse.

8Nditatha kutentha Igupto

ndi kupha onse omuthandiza,

pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni

kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.

11Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja

adzabwera kudzawononga dzikolo.

Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto

ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.

12Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo

ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.

Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.

Ine Yehova ndayankhula.

13“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzawononga mafano

ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.

Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,

ndipo ndidzaopseza dziko lonse.

14Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,

ndi kutentha mzinda wa Zowani.

Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.

15Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,

linga lolimba la Igupto,

ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.

16Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;

Peluziumu adzazunzika ndi ululu.

Malinga a Thebesi adzagumuka,

ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.

17Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti

adzaphedwa ndi lupanga

ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.

18Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima

pamene ndidzathyola goli la Igupto;

motero kunyada kwake kudzatha.

Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,

ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.

19Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,

ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Farao Watha Mphamvu

20Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

New International Version

Ezekiel 30:1-26

A Lament Over Egypt

1The word of the Lord came to me: 2“Son of man, prophesy and say: ‘This is what the Sovereign Lord says:

“ ‘Wail and say,

“Alas for that day!”

3For the day is near,

the day of the Lord is near—

a day of clouds,

a time of doom for the nations.

4A sword will come against Egypt,

and anguish will come upon Cush.30:4 That is, the upper Nile region; also in verses 5 and 9

When the slain fall in Egypt,

her wealth will be carried away

and her foundations torn down.

5Cush and Libya, Lydia and all Arabia, Kub and the people of the covenant land will fall by the sword along with Egypt.

6“ ‘This is what the Lord says:

“ ‘The allies of Egypt will fall

and her proud strength will fail.

From Migdol to Aswan

they will fall by the sword within her,

declares the Sovereign Lord.

7“ ‘They will be desolate

among desolate lands,

and their cities will lie

among ruined cities.

8Then they will know that I am the Lord,

when I set fire to Egypt

and all her helpers are crushed.

9“ ‘On that day messengers will go out from me in ships to frighten Cush out of her complacency. Anguish will take hold of them on the day of Egypt’s doom, for it is sure to come.

10“ ‘This is what the Sovereign Lord says:

“ ‘I will put an end to the hordes of Egypt

by the hand of Nebuchadnezzar king of Babylon.

11He and his army—the most ruthless of nations—

will be brought in to destroy the land.

They will draw their swords against Egypt

and fill the land with the slain.

12I will dry up the waters of the Nile

and sell the land to an evil nation;

by the hand of foreigners

I will lay waste the land and everything in it.

I the Lord have spoken.

13“ ‘This is what the Sovereign Lord says:

“ ‘I will destroy the idols

and put an end to the images in Memphis.

No longer will there be a prince in Egypt,

and I will spread fear throughout the land.

14I will lay waste Upper Egypt,

set fire to Zoan

and inflict punishment on Thebes.

15I will pour out my wrath on Pelusium,

the stronghold of Egypt,

and wipe out the hordes of Thebes.

16I will set fire to Egypt;

Pelusium will writhe in agony.

Thebes will be taken by storm;

Memphis will be in constant distress.

17The young men of Heliopolis and Bubastis

will fall by the sword,

and the cities themselves will go into captivity.

18Dark will be the day at Tahpanhes

when I break the yoke of Egypt;

there her proud strength will come to an end.

She will be covered with clouds,

and her villages will go into captivity.

19So I will inflict punishment on Egypt,

and they will know that I am the Lord.’ ”

Pharaoh’s Arms Are Broken

20In the eleventh year, in the first month on the seventh day, the word of the Lord came to me: 21“Son of man, I have broken the arm of Pharaoh king of Egypt. It has not been bound up to be healed or put in a splint so that it may become strong enough to hold a sword. 22Therefore this is what the Sovereign Lord says: I am against Pharaoh king of Egypt. I will break both his arms, the good arm as well as the broken one, and make the sword fall from his hand. 23I will disperse the Egyptians among the nations and scatter them through the countries. 24I will strengthen the arms of the king of Babylon and put my sword in his hand, but I will break the arms of Pharaoh, and he will groan before him like a mortally wounded man. 25I will strengthen the arms of the king of Babylon, but the arms of Pharaoh will fall limp. Then they will know that I am the Lord, when I put my sword into the hand of the king of Babylon and he brandishes it against Egypt. 26I will disperse the Egyptians among the nations and scatter them through the countries. Then they will know that I am the Lord.”