Ezekieli 30 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 30:1-26

Za Kulangidwa kwa Igupto

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,

‘Kalanga, tsiku lafika!’

3Pakuti tsiku layandikira,

tsiku la Yehova lili pafupi,

tsiku la mitambo yakuda,

tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.

4Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto

ndipo mavuto adzafika pa Kusi.

Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,

chuma chake chidzatengedwa

ndipo maziko ake adzagumuka.

5Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

6“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa

ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.

Adzaphedwa ndi lupanga

kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”

ndikutero Ine Ambuye Yehova.

7“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja

kupambana mabwinja ena onse opasuka,

ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka

kupambana mizinda ina yonse.

8Nditatha kutentha Igupto

ndi kupha onse omuthandiza,

pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni

kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.

11Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja

adzabwera kudzawononga dzikolo.

Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto

ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.

12Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo

ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.

Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.

Ine Yehova ndayankhula.

13“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzawononga mafano

ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.

Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,

ndipo ndidzaopseza dziko lonse.

14Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,

ndi kutentha mzinda wa Zowani.

Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.

15Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,

linga lolimba la Igupto,

ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.

16Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;

Peluziumu adzazunzika ndi ululu.

Malinga a Thebesi adzagumuka,

ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.

17Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti

adzaphedwa ndi lupanga

ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.

18Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima

pamene ndidzathyola goli la Igupto;

motero kunyada kwake kudzatha.

Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,

ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.

19Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,

ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Farao Watha Mphamvu

20Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Езекиил 30:1-26

Плач о Египте

1Было ко мне слово Вечного:

2– Смертный, пророчествуй и скажи: Так говорит Владыка Вечный:

«Плачьте: „О скорбный день!“

3День близок,

день Вечного близок –

сумрачный день,

время беды для народов.

4На Египет нагрянет меч,

Эфиопию охватит ужас,

когда в Египте станут падать поражённые,

когда будет отнято его богатство,

а его основания разрушены.

5Эфиопия, Ливия, Лидия30:5 Букв.: «Пут, Луд»., вся Аравия, Кув и народ страны священного соглашения30:5 Народ страны священного соглашения – скорее всего, иудеи, жившие в Египте. падут от меча вместе с египтянами».

6Так говорит Вечный:

«Падут сторонники Египта,

его гордая мощь сгинет.

От Мигдола на севере до Сиены на юге

его жители будут падать от меча, –

возвещает Владыка Вечный. –

7Разорены они будут

среди разорённых земель,

города их будут стоять

среди городов опустевших.

8Тогда узнают, что Я – Вечный,

когда Я предам Египет огню,

и будут разбиты его помощники.

9В тот день Мои вестники выйдут на кораблях, чтобы напугать беспечную Эфиопию. В день гибели Египта их охватит ужас, ведь он уже наступает!»

10Так говорит Владыка Вечный:

«Я уничтожу орды Египта

рукой Навуходоносора, царя Вавилона.

11Он и его народ – ужаснейший из народов –

будут приведены, чтобы погубить страну.

Они обнажат на Египет мечи

и наполнят страну поражёнными.

12Я осушу рукава Нила

и продам страну злодеям;

рукой чужеземцев

Я опустошу землю и всё, что её наполняет.

Я, Вечный, так сказал».

13Так говорит Владыка Вечный:

«Я уничтожу идолов

и истреблю истуканы в Мемфисе30:13 Букв.: «в Нофе»; также в ст. 16..

В Египте больше не будет правителя;

Я наведу на Египет страх.

14Я предам разорению Верхний Египет,

подожгу Цоан

и покараю Фивы30:14 Букв.: «Но»; также в ст. 15-16..

15Ярость Свою изолью на Син,

египетскую крепость,

и погублю фиванские орды.

16Я подожгу Египет,

скорчится в муках Син.

Враг возьмёт приступом Фивы

и средь бела дня обрушится на Мемфис.

17Юноши Гелиополя и Бубаста30:17 Букв.: «Она и Пи-Бешета».

падут от меча,

а девушки отправятся в плен.

18В Тахпанхесе померкнет день,

когда Я сокрушу там ярмо Египта,

и падёт его гордая мощь.

Этот город покроет туча,

и отправятся в плен жители его селений.

19Я покараю Египет,

и тогда узнают, что Я – Вечный».

Сокрушение мощи царя Египта

20В одиннадцатом году, в седьмой день первого месяца (29 апреля 587 г. до н. э.), было ко мне слово Вечного:

21– Смертный, Я разгромил мощную руку фараона, царя Египта, и её не перевязали, чтобы исцелить, и не наложили повязку, чтобы она окрепла и могла вновь владеть мечом.

22Поэтому так говорит Владыка Вечный:

– Я – враг фараону, царю Египта. Я сломаю ему обе руки – и здоровую, и уже сломанную, так что он уронит свой меч. 23Я рассею египтян среди других народов и развею их по чужим землям. 24Я укреплю мышцы вавилонского царя и вложу Мой меч в его руку, а мышцы фараона разорву, и он будет стонать перед царём Вавилона, словно смертельно раненый. 25Я укреплю мышцы вавилонского царя, а мышцы фараона ослабнут. Они узнают, что Я – Вечный, когда Я вложу Мой меч в руку царя Вавилона, и он занесёт его над Египтом. 26Я рассею египтян среди других народов и развею их по чужим землям. Тогда они узнают, что Я – Вечный.