Ezekieli 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 3:1-27

1Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.” 2Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.

3Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.

4Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga. 5Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli. 6Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera. 7Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma. 8Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo. 9Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”

10Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako. 11Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”

12Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!” 13Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu. 14Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu. 15Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.

Chenjezo kwa Israeli

16Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti, 17“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza. 18Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 19Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.

20“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 21Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”

22Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.” 23Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.

24Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako. 25Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu. 26Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu. 27Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 3:1-27

1祂對我說:「人子啊,你要把得到的吃下去,要吃下這書卷,然後去向以色列人傳講。」 2我張開口,祂就給我吃那書卷, 3對我說:「吃下我賜你的這書卷,讓它充滿你的肚腹。」我便吃了,書卷在我嘴裡甘甜如蜜。

4祂又對我說:「人子啊,現在你要到以色列人那裡,把我的話傳給他們。 5你不是奉命去語言不通的民族那裡,而是到以色列人當中。 6我不是派你到那些語言陌生、難懂、你聽不明白的民族中。我若果真派你到他們那裡,他們一定會聽你的話。 7然而以色列人卻不肯聽從你,因為他們頑固不化,不肯聽從我。 8不過,我要使你的臉像他們的臉一樣硬,使你的額像他們的額一樣硬。 9我要使你的額比火石更硬,如同金剛石。他們雖然是一群叛逆的人,你不要害怕,也不要因為他們的臉色而驚慌。」 10祂又說:「人子啊,你要留心聽我說的一切話,牢記在心。 11你要到你那些被擄的同胞那裡,不論他們聽不聽,你都要向他們宣告,『主耶和華這樣說。』」

12那時,靈把我舉起,我聽見後面有隆隆的聲音說:「耶和華的榮耀在祂的居所當受稱頌!」 13我聽見活物的翅膀相碰的聲音,以及他們旁邊的輪子發出的隆隆聲。 14靈把我舉起帶走了。我心裡苦悶,充滿憤怒,耶和華大能的手在我身上。 15我來到住在提勒·亞畢的被擄的人中,在迦巴魯河邊。我感到無比震驚,在他們中間坐了七天。

告誡以色列人

16過了七天,耶和華對我說: 17「人子啊,我立你做以色列人的守望者,你要把我告誡他們的話告訴他們。 18當我說某個惡人必滅亡時,如果你不告誡他,勸告他痛改前非,挽救他的性命,他必死在自己的罪中,而我要追究你的責任。 19如果你已經告誡他,他還是不肯離開自己的邪惡和罪行,他必死在罪惡之中,而你必免於罪責。 20如果一個義人偏離正道、犯罪作惡,我會使他跌倒,他必死亡。如果你不告誡他,他必死在罪惡之中,他以前的義行也不會被記念,而我要追究你的責任。 21如果你告誡他不要犯罪,他聽了你的告誡不再犯罪,他必保住性命,你也必免於罪責。」

22在那裡,耶和華的手按在我身上,對我說:「你起來前往平原,我要在那裡對你說話。」 23我到了平原,看見耶和華的榮耀停在那裡,那榮耀和我在迦巴魯河邊所見的一樣,我就俯伏在地。 24這時靈進入我裡面,使我站立起來。耶和華對我說:「你要把自己關在房子裡。 25人子啊,他們必把你捆綁起來,使你不能到百姓當中。 26同時,我要使你的舌頭緊貼上膛,使你不能開口責備他們,因為他們是一群叛逆的人。 27但當我對你說話的時候,我必開啟你的口,你要向他們宣告,『主耶和華這樣說。』肯聽的就讓他聽,不肯聽的就由他不聽,因為他們是一群叛逆的人。」