Ezekieli 3 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 3:1-27

1Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.” 2Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.

3Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.

4Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga. 5Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli. 6Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera. 7Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma. 8Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo. 9Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”

10Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako. 11Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”

12Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!” 13Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu. 14Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu. 15Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.

Chenjezo kwa Israeli

16Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti, 17“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza. 18Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 19Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.

20“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 21Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”

22Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.” 23Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.

24Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako. 25Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu. 26Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu. 27Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 3:1-27

1„Spis nu den her bogrulle,” sagde han, „og forkynd derefter mit ord for Israels folk.” 2Så åbnede jeg munden, og han puttede bogrullen i munden på mig, 3idet han tilføjede: „Spis hele bogrullen. Lad den fuldstændigt fylde dit indre.” Så spiste jeg den, og den smagte sødt som honning.

4„Jeg sender dig til Israels folk med et budskab fra mig,” fortsatte han. 5„Jeg sender dig ikke til et fremmed folk, hvis sprog du ikke forstår. 6Hvis jeg gjorde det, ville de i det mindste lytte til dig. 7I stedet sender jeg dig til Israels folk, og de vil ikke lytte mere til dig, end de lytter til mig, for de er stivnakkede og egenrådige i bund og grund. 8Men se, jeg gør dig hård og ubøjelig som dem, så du kan holde stand imod dem. 9Jeg gør dig hårdhudet og stærk som en klippe, så du ikke bliver såret af deres vrede blikke. Husk på, at det er et oprørsk folk. 10Hør godt efter alt, hvad jeg siger til dig, og lad budskabet blive en del af dig selv. 11Gå derefter rundt til folket, der bor i eksil, og forkynd dem mit ord, uanset om de hører efter eller ej.”

12Så løftede Ånden mig op og førte mig bort. Bag mig hørte jeg en buldrende røst, som lovpriste Herrens herlighed, 13og jeg hørte lyden af de levende væseners vinger, der rørte ved hinanden, og en voldsom rumlen fra hjulene, der fulgtes med dem.

14Efter at Ånden havde løftet mig op og ført mig bort, vandrede jeg om med forpint sjæl og oprørt indre, og Herrens kraft var stadig over mig. 15Så kom jeg til judæerne, som boede i Tel-Abib ved Kebarfloden. Der satte jeg mig tavs ned og stirrede lamslået frem for mig i syv dage.

Ezekiel kaldes til at være en vagtpost for folket

16Da de syv dage var gået, sagde Herren til mig:

17„Jeg har udvalgt dig til at holde udkig og stå vagt for Israels folk. Når du får et budskab fra mig, skal du straks give advarslen videre. 18Hvis jeg siger om nogle, at de skal dø som straf for deres ondskab, så skal du advare dem, så de har en chance for at ændre deres liv og undgå straffen. Hvis du ikke advarer dem, og de derfor ikke ændrer deres liv, så skal de dø for deres ondskab, men du skal også dø, for jeg vil holde dig ansvarlig for deres død. 19Hvis du derimod advarer dem, og de bliver ved med at synde uden at omvende sig, så skal de dø for deres ondskab, men du redder livet.

20Hvis retskafne mennesker bliver onde, og jeg derfor må straffe dem, så er det deres egen ondskab, der er skyld i deres død. Alle deres tidligere gode gerninger kan ikke redde dem. Og hvis du undlader at advare dem, bliver du også straffet. 21Men advarer du dem, så de holder op med deres ondskab, redder du både dig selv og dem.”

22Da mærkede jeg Herrens kraft over mig igen, og han sagde til mig: „Rejs dig og gå ud i dalen. Der vil jeg tale til dig.” 23Så rejste jeg mig og gik derud, og jeg så Herrens herlighed, som jeg tidligere havde set ved Kebarfloden, og jeg kastede mig ned med ansigtet mod jorden.

24Åndens kraft kom over mig og rejste mig op. „Gå hjem og luk dig inde i dit hus,” sagde han. 25„Der vil du blive bundet, så du ikke kan gå uden for din dør. 26Og jeg vil lade din tunge klæbe til ganen, så du ikke af dig selv kan anklage mit oprørske folk. 27Men når du får et budskab fra mig, vil jeg løse din tunge og lade dig tale, så du kan advare dem. ‚Hør hvad Gud Herren siger til jer!’ skal du sige. Nogle vil lytte til dig, men andre nægter at høre efter, for det er et oprørsk folk.”