Ezekieli 29 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 29:1-21

Za Chilango cha Igupto

1Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake. 3Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto,

iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako.

Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga;

ndinadzipangira ndekha.’

4Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako

ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako.

Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo

pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.

5Ndidzakutaya ku chipululu,

iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako.

Udzagwera pamtetete kuthengo

popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako.

Ndidzakusandutsa chakudya

cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.

6Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

“ ‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli. 7Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.

8“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe. 9Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

“ ‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’ 10nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi. 11Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi. 12Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.

13“ ‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako. 14Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika. 15Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu. 16Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’ ”

Mphotho ya Nebukadinezara

17Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti: 18“Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo. 19Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo. 20Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.

21“Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Thai New Contemporary Bible

เอเสเคียล 29:1-21

คำพยากรณ์กล่าวโทษอียิปต์

1ในวันที่สิบสองเดือนที่สิบปีที่สิบ พระดำรัสขององค์พระผู้เป็นเจ้ามาถึงข้าพเจ้าว่า 2“บุตรมนุษย์เอ๋ย จงหันหน้าไปทางฟาโรห์กษัตริย์แห่งอียิปต์ และพยากรณ์กล่าวโทษเขาและอียิปต์ทั้งปวงว่า 3‘พระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตตรัสดังนี้ว่า

“ ‘ฟาโรห์กษัตริย์แห่งอียิปต์ เราเป็นศัตรูกับเจ้า

เจ้าผู้เป็นสัตว์ร้ายมหึมาซึ่งกบดานอยู่ในสายน้ำของเจ้า

เจ้ากล่าวว่า “แม่น้ำไนล์เป็นของข้า

ข้าสร้างมันขึ้นมาเพื่อตัวข้าเอง”

4แต่เราจะเอาเบ็ดเกี่ยวขากรรไกรของเจ้า

และทำให้ปลาในลำน้ำของเจ้าติดกับเกล็ดของเจ้า

เราจะดึงเจ้าขึ้นจากสายน้ำ

พร้อมกับปลาทั้งปวงซึ่งติดอยู่ที่เกล็ดของเจ้า

5เราจะทิ้งเจ้าไว้ในถิ่นกันดาร

ทั้งตัวเจ้าและปลาทั้งปวงจากลำน้ำของเจ้า

เจ้าจะตกอยู่กลางทุ่ง

ไม่มีใครหอบหรือเก็บเจ้าขึ้นมา

เราจะยกเจ้าให้เป็นอาหาร

ของสัตว์บกและนกในอากาศ

6เมื่อนั้นทุกคนที่อยู่ในอียิปต์จะรู้ว่าเราคือพระยาห์เวห์

“ ‘เจ้าเป็นไม้อ้อสำหรับพงศ์พันธุ์อิสราเอล 7เมื่อเขาฉวยเจ้าไว้ในมือ เจ้าก็ปริแตกและบาดไหล่ของเขา เมื่อเขาพิงเจ้า เจ้าก็หักและทำให้หลังของเขาเคล็ด

8“ ‘ฉะนั้นพระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตตรัสดังนี้ว่า เราจะนำดาบมาห้ำหั่นเจ้า และฆ่าผู้คนและสัตว์ของเจ้า 9อียิปต์จะกลายเป็นแดนร้าง เมื่อนั้นพวกเขาจะรู้ว่าเราคือพระยาห์เวห์

“ ‘เนื่องจากเจ้ากล่าวว่า “แม่น้ำไนล์เป็นของข้า ข้าสร้างมันขึ้นมา” 10ฉะนั้นเราจึงเป็นศัตรูกับเจ้าและกับสายน้ำต่างๆ ของเจ้า เราจะทำให้ดินแดนอียิปต์กลายเป็นซากปรักหักพังและถูกทิ้งร้างตั้งแต่มิกดลจนถึงอัสวานไปจดพรมแดนของคูช29:10 คือ ตอนบนของลุ่มแม่น้ำไนล์ 11จะไม่มีรอยเท้าทั้งของคนและของสัตว์เหยียบผ่าน จะไม่มีใครอาศัยที่นั่นตลอดสี่สิบปี 12เราจะทำให้อียิปต์เริศร้างท่ามกลางดินแดนต่างๆ ซึ่งถูกทำลาย และเมืองต่างๆ ของอียิปต์จะถูกทิ้งร้างอยู่ท่ามกลางนครที่เป็นซากปรักหักพังตลอดสี่สิบปี เราจะทำให้ชาวอียิปต์กระจัดกระจายไปตามชนชาติต่างๆ และไปยังนานาประเทศ

13“ ‘ถึงอย่างนั้นพระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตตรัสดังนี้ว่า เมื่อครบสี่สิบปี เราจะรวบรวมชาวอียิปต์กลับมาจากชาติต่างๆ ที่พวกเขาถูกทำให้กระจัดกระจายไปนั้น 14เราจะนำพวกเขากลับมาจากการเป็นเชลยสู่ดินแดนอียิปต์ตอนบน29:14 ภาษาฮีบรูว่าสู่ปัทโรสอันเป็นดินแดนของบรรพบุรุษของพวกเขา พวกเขาจะเป็นอาณาจักรต่ำต้อยในที่แห่งนั้น 15จะต่ำต้อยที่สุดและจะไม่มีวันเผยอตัวขึ้นเหนือชนชาติอื่นๆ ได้อีกเลย เราจะทำให้อียิปต์อ่อนแอจนไม่ได้ขึ้นปกครองชนชาติต่างๆ อีกเลย 16อียิปต์จะไม่ได้เป็นแหล่งพักพิงให้ชนชาติอิสราเอลอีกต่อไป แต่จะเป็นเครื่องเตือนใจพวกเขาให้สำนึกถึงบาปที่ได้หันไปพึ่งพาอียิปต์ เมื่อนั้นพวกเขาจะรู้ว่าเราคือพระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิต’ ”

17ในวันที่หนึ่งเดือนที่หนึ่งปีที่ยี่สิบเจ็ด พระดำรัสขององค์พระผู้เป็นเจ้ามาถึงข้าพเจ้าว่า 18“บุตรมนุษย์เอ๋ย กษัตริย์เนบูคัดเนสซาร์แห่งบาบิโลนยกทัพมาสู้รบขับเคี่ยวกับไทระอย่างหนัก ทุกศีรษะถูกเสียดสีจนล้านเลี่ยน และทุกไหล่ถลอก ถึงอย่างนั้นเขากับกองทัพก็ไม่ได้อะไรจากการรบกับไทระ 19ฉะนั้นพระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตตรัสดังนี้ว่าเราจะมอบอียิปต์แก่กษัตริย์เนบูคัดเนสซาร์แห่งบาบิโลน และเขาจะริบทรัพย์สมบัติไป เขาจะปล้นชิงข้าวของในแดนนั้นไปเป็นค่าจ้างให้กองทัพของเขา 20เรายกอียิปต์ให้เป็นรางวัลจากการบากบั่นลงแรงของเขา เพราะเขากับกองทัพกระทำการเพื่อเรา พระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตประกาศดังนั้น

21“ในวันนั้นเราจะทำให้มีเขาสัตว์เขาหนึ่ง29:21เขาสัตว์ซึ่งเป็นสัญลักษณ์ของกำลังงอกขึ้นมาเพื่อพงศ์พันธุ์อิสราเอล และเราจะเปิดปากของเจ้าท่ามกลางพวกเขา เมื่อนั้นพวกเขาจะรู้ว่าเราคือพระยาห์เวห์”