Ezekieli 24 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 24:1-27

Mʼphika Wophikira

1Pa tsiku lakhumi la mwezi wakhumi chaka chachisanu ndi chinayi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu lemba dzina la tsiku lalero, lero lomwe lino, chifukwa mfumu ya Babuloni yazungulira Yerusalemu lero lino. 3Uwaphere mwambi anthu owukirawa ndi kuwawuza kuti: ‘Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Ikani mʼphika pa moto,

ndipo mu mʼphikamo muthiremo madzi.

4Mu mʼphikamo muyikemo nthuli za nyama,

nthuli zonse zabwino kwambiri za mwendo wathako ndi mwendo wamwamba.

Mudzadzemo mafupa abwino kwambiri.

5Pa gulu la nkhosa musankhepo nkhosa yabwino kwambiri.

Muyike nkhuni pansi pa mʼphikawo.

Madzi awire.

Kenaka muphike nyamayo pamodzi ndi mafupa omwe.’

6“ ‘Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi,

tsoka kwa mʼphika wadzimbiri;

dzimbiri lake losachoka!

Mutulutsemo nthuli imodzimodzi

osasankhulapo.

7“ ‘Paja magazi amene anakhetsa akanali pakati pake mu mzindamo.

Iye awakhuthulira pa thanthwe losalala.

Sanawakhutulire pa dothi

kuopa kuti fumbi lingawafotsere.

8Ndinasiya magaziwo pa mwala wosalala

kuti asafotseredwe ndi fumbi

chifukwa ndinafuna kuonetsa mkwiyo wanga ndi kulipsira.

9“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi!

Inenso, ndidzawunjika mulu waukulu wa nkhuni.

10Choncho wonjeza nkhuni

ndipo muyatse moto.

Phikani nyamayo bwinobwino,

muthiremo zokometsera,

mutsanule msuzi, ndipo mupsereze mafupawo.

11Tsono muyike pa makala mʼphika wopanda kanthuwo

mpaka utenthe kuchita kuti psuu

kuti zonyansa zake zisungunuke

ndi kuti dzimbiri lake lichoke.

12Koma mʼphikawo walephereka kuyeretsedwa.

Dzimbiri lake linalowerera silingatheke kuchoka

ngakhale ndi moto womwe.

13“ ‘Tsono dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako. Pakuti ine ndinayesa kukutsuka koma iwe sunayere, ndipo sudzayeranso mpaka ukali wanga utakwaniratu pa iwe.

14“ ‘Ine Yehova ndayankhula. Zimenezi zikubwera ndipo ndidzazichitadi. Sindidzabwerera mʼmbuyo. Sindidzakulekerera kapena kukuchitira chifundo. Ndidzakulanga molingana ndi makhalidwe ndi machitidwe ako, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Imfa ya Mkazi wa Ezekieli

15Yehova anandiyankhula kuti: 16“Iwe mwana wa munthu, Ine ndikulanda mwadzidzidzi mkazi amene amakukomera mʼmaso kwambiri. Koma usadandaule, usalire kapena kukhetsa misozi. 17Ubuwule koma mwakachetechete. Usamulire wakufayo. Uvale nduwira yako ndithu, nsapato zakonso usavule. Usaphimbe nkhope kapena kudya chakudya cha anamfedwa.”

18Choncho ndinayankhula ndi anthu mmawa, ndipo madzulo mkazi wanga anamwalira. Mmawa mwake ndinachita monga momwe anandilamulira.

19Ndipo anthu anandifunsa kuti, “Kodi sutifotokozera tanthauzo la zimene ukuchitazi?”

20Ndinawayankha kuti, “Yehova anandipatsa uthenga wakuti, 21‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga. 22Ndipo mudzachita monga ndachitira inemu. Inu simudzaphimba nkhope zanu kapena kudya chakudya cha anamfedwa. 23Mudzavala nduwira zanu kumutu ndi nsapato zanu ku mapazi anu. Simudzabuma maliro kapena kukhetsa misozi koma mudzavutika kwambiri chifukwa cha machimo anu ndipo mudzabuwula pakati panu. 24Ine Ezekieli ndidzakhala chitsanzo chanu. Mudzachita monga momwe ndachitira. Izi zikadzachitika, akutero Yehova, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Wamphamvuzonse.’

25“Ndipo Yehova anandiyankhula nati: Iwe mwana wa munthu, tsiku lina ndidzawachotsera anthuwa linga lawo limene ankakondwerera kukongola kwake, limene linkawakomera mʼmaso mwawo, limenenso anayikapo mtima wawo kwambiri. Ndidzawachotsera ana awo aamuna ndi aakazi. 26Pa tsiku limenelo wothawa nkhondo adzabwera kudzakuwuzani zimenezo. 27Pa tsiku limenelo pakamwa pako padzatsekuka. Udzatha kuyankhula naye ndipo sudzakhalanso chete. Motero udzakhala chizindikiro kwa iwo, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”