Ezekieli 24 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 24:1-27

Mʼphika Wophikira

1Pa tsiku lakhumi la mwezi wakhumi chaka chachisanu ndi chinayi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu lemba dzina la tsiku lalero, lero lomwe lino, chifukwa mfumu ya Babuloni yazungulira Yerusalemu lero lino. 3Uwaphere mwambi anthu owukirawa ndi kuwawuza kuti: ‘Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Ikani mʼphika pa moto,

ndipo mu mʼphikamo muthiremo madzi.

4Mu mʼphikamo muyikemo nthuli za nyama,

nthuli zonse zabwino kwambiri za mwendo wathako ndi mwendo wamwamba.

Mudzadzemo mafupa abwino kwambiri.

5Pa gulu la nkhosa musankhepo nkhosa yabwino kwambiri.

Muyike nkhuni pansi pa mʼphikawo.

Madzi awire.

Kenaka muphike nyamayo pamodzi ndi mafupa omwe.’

6“ ‘Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi,

tsoka kwa mʼphika wadzimbiri;

dzimbiri lake losachoka!

Mutulutsemo nthuli imodzimodzi

osasankhulapo.

7“ ‘Paja magazi amene anakhetsa akanali pakati pake mu mzindamo.

Iye awakhuthulira pa thanthwe losalala.

Sanawakhutulire pa dothi

kuopa kuti fumbi lingawafotsere.

8Ndinasiya magaziwo pa mwala wosalala

kuti asafotseredwe ndi fumbi

chifukwa ndinafuna kuonetsa mkwiyo wanga ndi kulipsira.

9“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi!

Inenso, ndidzawunjika mulu waukulu wa nkhuni.

10Choncho wonjeza nkhuni

ndipo muyatse moto.

Phikani nyamayo bwinobwino,

muthiremo zokometsera,

mutsanule msuzi, ndipo mupsereze mafupawo.

11Tsono muyike pa makala mʼphika wopanda kanthuwo

mpaka utenthe kuchita kuti psuu

kuti zonyansa zake zisungunuke

ndi kuti dzimbiri lake lichoke.

12Koma mʼphikawo walephereka kuyeretsedwa.

Dzimbiri lake linalowerera silingatheke kuchoka

ngakhale ndi moto womwe.

13“ ‘Tsono dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako. Pakuti ine ndinayesa kukutsuka koma iwe sunayere, ndipo sudzayeranso mpaka ukali wanga utakwaniratu pa iwe.

14“ ‘Ine Yehova ndayankhula. Zimenezi zikubwera ndipo ndidzazichitadi. Sindidzabwerera mʼmbuyo. Sindidzakulekerera kapena kukuchitira chifundo. Ndidzakulanga molingana ndi makhalidwe ndi machitidwe ako, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Imfa ya Mkazi wa Ezekieli

15Yehova anandiyankhula kuti: 16“Iwe mwana wa munthu, Ine ndikulanda mwadzidzidzi mkazi amene amakukomera mʼmaso kwambiri. Koma usadandaule, usalire kapena kukhetsa misozi. 17Ubuwule koma mwakachetechete. Usamulire wakufayo. Uvale nduwira yako ndithu, nsapato zakonso usavule. Usaphimbe nkhope kapena kudya chakudya cha anamfedwa.”

18Choncho ndinayankhula ndi anthu mmawa, ndipo madzulo mkazi wanga anamwalira. Mmawa mwake ndinachita monga momwe anandilamulira.

19Ndipo anthu anandifunsa kuti, “Kodi sutifotokozera tanthauzo la zimene ukuchitazi?”

20Ndinawayankha kuti, “Yehova anandipatsa uthenga wakuti, 21‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga. 22Ndipo mudzachita monga ndachitira inemu. Inu simudzaphimba nkhope zanu kapena kudya chakudya cha anamfedwa. 23Mudzavala nduwira zanu kumutu ndi nsapato zanu ku mapazi anu. Simudzabuma maliro kapena kukhetsa misozi koma mudzavutika kwambiri chifukwa cha machimo anu ndipo mudzabuwula pakati panu. 24Ine Ezekieli ndidzakhala chitsanzo chanu. Mudzachita monga momwe ndachitira. Izi zikadzachitika, akutero Yehova, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Wamphamvuzonse.’

25“Ndipo Yehova anandiyankhula nati: Iwe mwana wa munthu, tsiku lina ndidzawachotsera anthuwa linga lawo limene ankakondwerera kukongola kwake, limene linkawakomera mʼmaso mwawo, limenenso anayikapo mtima wawo kwambiri. Ndidzawachotsera ana awo aamuna ndi aakazi. 26Pa tsiku limenelo wothawa nkhondo adzabwera kudzakuwuzani zimenezo. 27Pa tsiku limenelo pakamwa pako padzatsekuka. Udzatha kuyankhula naye ndipo sudzakhalanso chete. Motero udzakhala chizindikiro kwa iwo, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Korean Living Bible

에스겔 24:1-27

녹슨 가마

1우리가 포로 되어 온 지 9년째가 되는 해 10월 10일에 여호와께서 나 에게 말씀하셨다.

2“사람의 아들아, 너는 오늘 날짜를 기록하라. 오늘은 바빌로니아 왕이 예루살렘을 포위한 날이다.

3너는 거역하는 이 백성들에게 비유를 들어 나 주 여호와가 이렇게 말한다고 전하라. ‘너희는 가마 하나를 걸고 거기에 물을 붓고

4-5양떼 중에서 제일 좋은 것을 잡아 고기 의 제일 좋은 부분인 넓적다리와 어깻죽지를 가마에 넣고 뼈 중에서 제일 좋은 것을 골라 그 가마에 가득 채워라. 그리고 가마 밑에 나무를 쌓고 물을 펄펄 끓여 뼈가 물렁물렁할 때까지 삶아라.

6“ ‘나 주 여호와가 말한다. 살인자들의 도시 예루살렘아, 너는 녹이 슬었으나 그 녹을 제거하지 않은 가마와 같구나. 너에게 화가 있을 것이니 너는 24:6 또는 ‘제비 뽑을 것도 없이’순서를 가리지 말고 그 속에 있는 것을 하나하나 끄집어내어라.

7“ ‘성 안에 살인이 있었으나 그 피가 땅에 떨어져 티끌로 덮이지 않고 아무것도 덮여 있지 않은 바위 위에 떨어졌다.

8내가 그 피를 바위 위에 그대로 두어 덮이지 않게 한 것은 내가 분노하여 보복하기 위해서이다.

9“ ‘그러므로 나 주 여호와가 말한다. 살인자들의 도시 예루살렘에 화가 있을 것이다. 내가 그 장작더미를 더 높이 쌓고

10불을 피워 그 고기를 삶고 국물을 졸이고 뼈를 태운 다음

11빈 가마를 숯불 위에 얹어 놓고 쇠를 달구어 그 속의 불순물이 녹게 하며 찌꺼기가 다 타서 없어지게 하겠다.

12내가 이 성의 불순물을 제거하려고 애썼으나 그 속에 있는 녹이 벗겨지지 않고 불에서도 제거되지 않았다.

13“ ‘예루살렘아, 너의 음란한 행위가 너를 더럽혔다. 내가 너를 깨끗하게 하려고 하였으나 네가 깨끗해지지 않았다. 내가 너에게 분풀이를 하기 전에는 네 더러움이 깨끗해지지 않을 것이다.

14“ ‘나 주 여호와가 말하였으니 이제 내가 행할 때가 되었다. 내가 마음을 돌이키지 않고 너를 불쌍히 여기지 않으며 뉘우치지도 않을 것이니 네가 행한 대로 심판을 받을 것이다. 이것은 나 주 여호와의 말이다.’ ”

에스겔의 아내가 죽다

15여호와께서 또 나에게 말씀하셨다.

16“사람의 아들아, 네가 가장 사랑하는 사람을 내가 단번에 쳐서 빼앗아 가겠다. 너는 슬퍼하거나 울거나 눈물을 흘리지 말고

17말없이 탄식하여라. 죽은 사람을 위해 슬퍼하지 말고 두건을 머리에 꼭 붙들어 매고 신발을 신고 입술을 가리지 말며 조객들이 먹는 음식을 먹지 말아라.”

18그래서 내가 아침에 그런 이야기를 사람들에게 말해 주었는데 그 날 저녁에 내 아내가 죽었다. 그 다음날 아침에 내가 명령을 받은 대로 하자

19사람들이 나에게 물었다. “당신은 어째서 이렇게 하시오? 당신이 우리에게 말하려고 하는 것이 무엇이오?”

20-21그때 내가 그들에게 대답하였다. “여 호와께서는 이스라엘 백성에게 이렇게 전하라고 나에게 말씀하셨습니다. ‘내가 너희 힘의 자랑이요 너희 눈의 기쁨이며 너희 마음에 사랑의 대상인 내 성전을 더럽힐 것이니 예루살렘에 남아 있는 너희 자녀들이 전쟁에서 죽음을 당할 것이다.

22너희는 에스겔이 행한 대로 입술을 가리지 않고 초상집 음식을 먹지 않으며

23두건으로 머리를 싸매고 신발을 신은 채 슬퍼하지도 않고 울지도 않을 것이다. 그러나 너희는 너희 죄 때문에 쇠잔할 것이며 서로 바라보고 탄식할 것이다.

24이와 같이 에스겔이 너희에게 하나의 표징이 될 것이며 너희는 그가 행하는 대로 할 것이다. 이런 일이 일어나면 너희는 내가 주 여호와임을 알게 될 것이다.’ ”

25여호와께서 나에게 말씀하셨다. “사람의 아들아, 내가 그들의 힘과 자랑과 마음의 기쁨인 성전과 그들의 자녀를 없애는 그 날에

26도망쳐 나온 자가 너에게 와서 그 소식을 전할 것이다.

27그때 네 입이 열려 그와 말하게 될 것이며 다시는 네가 침묵을 지키지 않을 것이다. 이처럼 너는 그들에게 표징이 될 것이며 그들은 내가 여호와임을 알게 될 것이다.”