Ezekieli 23 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 23:1-49

Za Yerusalemu ndi Samariya

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi. 3Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja. 4Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.

5“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya. 6Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo. 7Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye. 8Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.

9“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka. 10Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.

11“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake. 12Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka. 13Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.

14“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira, 15atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya. 16Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana. 17Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo. 18Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake. 19Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto. 20Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo. 21Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.

22“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse. 23Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo. 24Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire. 25Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto. 26Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali. 27Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.

28“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo. 29Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako, 30zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo. 31Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.

32“Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“Udzamwera chikho cha mkulu wako,

chikho chachikulu ndi chakuya;

anthu adzakuseka ndi kukunyoza,

pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.

33Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni.

Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu,

chikho cha mkulu wako Samariya.

34Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza.

Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho

ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake.

Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.

35“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”

36Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa. 37Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo. 38Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga. 39Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.

40“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka. 41Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.

42“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu. 43Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’ 44Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama. 45Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.

46“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo. 47Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.

48“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo. 49Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 23:1-49

两个淫妇的比喻

1耶和华对我说: 2“人子啊,有一对同胞姊妹, 3她们在埃及做娼妓,年轻时就淫乱,任人抚摸她们的胸,玩弄她们的乳。 4姐姐名叫阿荷拉,妹妹名叫阿荷利巴。后来她们都归属了我,并且生儿育女。阿荷拉撒玛利亚阿荷利巴耶路撒冷

5阿荷拉归属我后仍然淫乱,贪恋她的情人——亚述人。 6他们都是身穿紫衣的省长和总督,都是英俊的年轻骑士。 7她便与这些亚述的精英放纵情欲,拜他们的偶像,玷污自己。 8她没有放弃在埃及的淫荡行为,她年轻的时候就任人玩弄、发泄情欲。 9因此,我把她交在她所恋慕的亚述人手里。 10他们扒光她的衣服,夺去她的儿女,用刀杀了她。她受了报应,成了妇女口中的笑柄。

11“她妹妹阿荷利巴看见这一切,不但没有引以为戒,反而更加放荡淫乱。 12她贪恋亚述的省长和总督,那些衣着华丽、英俊的年轻骑士。 13我看见她玷污了自己,与姐姐的行径如出一辙。 14她还变本加厉地放荡淫乱,看见墙上用朱砂画着迦勒底人的像, 15腰间束带,头巾飘扬,都像是来自迦勒底巴比伦人的将领, 16便恋上了他们,差遣使者到他们那里。 17巴比伦人便来上她的床,放纵情欲玷污了她。之后,她便厌弃他们。 18她继续公开地淫乱,在众人面前赤身露体,我厌弃她,像厌弃她姐姐一样。 19她却更加淫乱,怀念自己年轻时在埃及为娼的日子, 20怎样与那些体壮精足、如驴似马的情人纵淫, 21渴望重温早年的淫行,任埃及人摸胸弄乳。

22“因此,主耶和华对阿荷利巴这样说,‘我要使那些被你离弃的情人从四面八方来攻击你。 23他们是巴比伦人,还有从比割书亚哥亚来的迦勒底人以及亚述人,都是骑马的省长和总督及年轻英俊的有名将领。 24他们率领大队人马,带着兵器、战车和军需车来攻击你。他们顶盔贯甲,手拿盾牌从四面八方进攻你。我要让他们惩罚你,他们会按自己的律例来审判你。 25我要借着他们向你倾倒我的义愤,他们要在愤怒中对付你,割去你的鼻子和耳朵,掳去你的儿女,城中剩下的人都要死于刀下,被火吞噬。 26他们要剥下你的衣服,夺去你的珠宝。 27我要借此制止你从埃及染上的淫乱和放荡,使你不再向往埃及28我要把你交在你所厌恶的人手中, 29他们必满怀仇恨地对付你,夺去你努力得来的一切,留下你赤身露体,使你淫荡的丑恶公布于众。 30因为你与各国苟合,被他们的偶像玷污,这些事必临到你身上。 31你既然步你姐姐的后尘,我要让你喝她喝的那杯。’

32“主耶和华说,

“‘你必喝你姐姐那又大又深的杯,

成为人们耻笑和辱骂的对象。

33你姐姐撒玛利亚的杯盛满了恐惧和凄凉。

你喝了后必酩酊大醉,

满心忧愁。

34你必一滴不剩把它喝光,

然后把杯摔成碎片,

抓破自己的胸脯。

这是主耶和华说的。’

35“主耶和华说,‘你既忘记我,把我抛在脑后,就要受自己放荡淫乱的报应。’”

36耶和华又对我说:“人子啊,你要审判阿荷拉阿荷利巴,指出她们的丑行。 37她们淫荡,手上沾满血腥,与偶像淫乱,把为我所生的儿女烧死献给偶像。 38同时,她们还在同一天玷污我的圣所,亵渎我的安息日, 39她们焚烧自己的儿女献祭给偶像,并在当天进入我的圣所,亵渎圣所。这就是她们在我圣所里的恶行。

40“她们甚至派使者请来远方的人,并且沐浴洗身,描眉画眼,佩戴首饰, 41坐在华丽的床上,面前的桌子上摆设着我的香料和膏油。 42她们屋里传出众人的安乐声,从旷野来的酒徒和粗汉把镯子戴在这对姊妹的手腕上,把华冠戴在她们的头上。 43我说,‘她们纵欲无度、年老色衰,这些人还与她们淫乱。 44他们与这对淫妇阿荷拉阿荷利巴淫乱,好像与娼妓淫乱一样。 45她们是双手沾满血腥的淫妇,必有义人按她们应得的报应审判她们。’

46“主耶和华说,‘我要使许多人起来攻击、抢掠她们,叫她们胆战心惊。 47这些人要用石头打死她们,用刀杀戮她们和她们的儿女,用火烧毁她们的房屋。 48这样,我便制止了这地方的淫乱,所有的妇女都引以为戒,不敢效法她们。 49她们淫乱,必得报应;她们拜偶像,必受惩罚。这样,你们就知道我是主耶和华。’”