Ezekieli 23 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 23:1-49

Za Yerusalemu ndi Samariya

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi. 3Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja. 4Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.

5“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya. 6Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo. 7Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye. 8Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.

9“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka. 10Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.

11“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake. 12Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka. 13Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.

14“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira, 15atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya. 16Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana. 17Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo. 18Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake. 19Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto. 20Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo. 21Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.

22“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse. 23Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo. 24Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire. 25Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto. 26Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali. 27Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.

28“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo. 29Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako, 30zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo. 31Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.

32“Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“Udzamwera chikho cha mkulu wako,

chikho chachikulu ndi chakuya;

anthu adzakuseka ndi kukunyoza,

pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.

33Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni.

Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu,

chikho cha mkulu wako Samariya.

34Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza.

Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho

ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake.

Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.

35“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”

36Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa. 37Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo. 38Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga. 39Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.

40“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka. 41Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.

42“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu. 43Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’ 44Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama. 45Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.

46“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo. 47Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.

48“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo. 49Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 23:1-49

Billedtale om Samarias og Jerusalems utroskab

1Herren sagde til mig: 2-3„Du menneske, der var engang to søstre, der fra deres tidligste ungdom levede som prostituerede i Egypten. Dér krammede og knugede man deres jomfruelige bryster. 4Storesøsteren hed Ohola og lillesøsteren Oholiba. De symboliserer Samaria og Jerusalem.23,4 De to navne, der betyder „hendes telt” og „mit telt er i hende”, hentyder til, at Jerusalem havde Herrens helligdom/telt, mens Samaria havde sin egen helligdom. Hovedstæderne står symbolsk for Nordriget og Sydriget.

Jeg giftede mig med dem begge, og de fødte mig sønner og døtre. 5Men Ohola var mig utro og blev forgabt i assyrerne, 6for deres officerer og stormænd var utrolig flotte med purpurfarvede klæder og prægtige heste. 7Hun horede med Assyriens fornemste mænd og dyrkede uhæmmet deres afguder. 8Allerede da hun var i Egypten, var hun utro imod mig og gav sig hen til afguderne der. Desværre holdt hun fast ved sin utroskab, selv efter at hun havde forladt Egypten.

9Derfor lagde jeg hendes skæbne i assyrernes hænder. Hendes elskere kunne nu gøre med hende, hvad de ville. 10Som straf ydmygede de hende ved at rive tøjet af hende og gøre hendes børn til slaver. Derpå blev hun slået ned med sværdet, og de andre kvinder hånede hende for den skændsel, hun blev udsat for.

11Men selv om hendes søster Oholiba så, hvad der skete med hende, tog hun ikke ved lære. Hendes afgudsliderlighed var forfærdelig, og hun syndede endnu mere end søsteren. 12Hun flirtede med de assyriske officerer og stormænd, der havde så flotte uniformer og prægtige heste. 13Hun var lige så troløs som sin søster, 14-15ja, hun var faktisk værre end søsteren, for hun forelskede sig endog i de babyloniske officerer, hun havde set malerier af på murene med røde uniformer, bælte om livet og turban på hovedet. 16Hun blev så forelsket i dem, at hun sendte bud til Babylon om, at de skulle komme til hende. 17De kom så og horede med hende, men bagefter følte hun afsky for dem.

18Fordi hun blottede sig for dem og gav sig selv hen til dem, blev jeg led ved hende, som jeg var blevet led ved hendes storesøster. 19-20Men det generede hende ikke. Hun huskede sin fortid som prostitueret i Egypten og gav sig nu hen til de liderlige egyptere, der var brunstige som æsler og gejle som hingste. 21Hun gik tilbage til sin ungdoms lyster, dengang man krammede hendes bryster i Egypten.

22Men hør nu Herrens ord, Oholiba: Alle dine elskere, som du vendte dig fra i afsky, hidser jeg op imod dig. 23Babylonierne kommer imod dig sammen med alle kaldæerne fra Pekod, Shoa og Koa. Også assyrerne sender jeg mod dig, alle de flotte officerer og stormænd, klædt i purpur og ridende på prægtige heste. 24Fra nord kommer stridsvogne og forsyningsvogne rumlende imod dig, og deres fodfolk kommer vrimlende fra alle kanter, bevæbnet til tænderne. Fjenden omringer dig fra alle sider, og jeg overlader det til dem at udføre straffen over dig. 25I jalousi vil jeg hævne mig på dig. Jeg lader dem skære næsen og ørerne af dig og bortføre dine børn som slaver. De, der overlever, vil falde for sværdet eller brændes i ilden. 26De vil flå tøjet af dig og rive dine juveler til sig. 27Sådan vil jeg gøre en ende på dine uhæmmede lidenskaber, den skamløse livsstil du tog med dig fra Egypten. Du skal ikke mere tilbede falske guder eller tænke på Egypten. 28Jeg giver dig i dine fjenders vold, dem du afskyr og har taget afstand fra. 29I deres raseri vil de frarøve dig alt, hvad du har, og slænge dig bort, nøgen og forladt, så din skandaløse livsstil afsløres. 30Al den elendighed er du selv skyld i, fordi du dyrkede fremmede folkeslags guder og gjorde dig selv uren ved at tilbede deres afgudsbilleder. 31Du fulgte i din søsters fodspor, og derfor skal du få en straf, der svarer til hendes. 32Det er en hård straf, og du bliver genstand for alverdens hån. Du må tømme straffens fyldte bæger til bunds. 33Du vil blive fuldstændig omtåget og stønne af gru og rædsel. 34Men du skal tømme det til sidste dråbe og derefter smadre det i tusind stykker og rive dig selv til blods i fortvivlelse. Jeg, Herren, har talt. 35Fordi du glemte mig og vendte mig ryggen, må du tage konsekvensen af din forfærdelige utroskab.”

36Herren fortsatte: „Du menneske, udtal min dom over Ohola og Oholiba. Fortæl om deres frygtelige synder. 37De var mig utro og har blod på hænderne, for de dyrkede afguderne og myrdede de børn, som de fødte mig, ved at brænde dem på afgudsaltrene. 38Desuden vanærede de mit tempel og overholdt ikke sabbatsbudet. 39Tænk, lige efter at have slagtet og brændt deres børn til ære for afguderne kom de til mit tempel for at tilbede mig! Hvilken afskyelig handlemåde!

40I to søstre sendte bud til fjerne lande efter flotte mænd. I badede jer, lagde sminke på øjnene og tog jeres fineste smykker på. 41I satte jer til bords på elegante puder og stillede min hellige røgelse og olie frem på bordet. 42Der var fest og ballade. De mange indbudte mænd fra ørkenen drak sig fulde og satte armringe på jeres arme og en fornem krone på jeres hoved. 43Jeg sagde til mig selv: De utro gamle skøger! 44Derpå gik mændene ind til Ohola og Oholiba som til prostituerede. Åh, de skamløse kvinder. 45Men retskafne mænd skal efter lovens ord idømme dem straffen for ægteskabsbrud og mord, for de har været utro imod mig, og de har blod på hænderne.

46Gud Herren siger: Før en hær imod dem, så de bliver terroriseret og udplyndret. 47Lad fjenden kaste sten imod dem og hugge dem ned med sværdet, slagte deres børn og brænde deres huse ned til grunden. 48For jeg vil sætte en stopper for den afgudsliderlighed, der hersker i landet. I skal være et eksempel til skræk og advarsel for andre til alle tider. 49I vil blive straffet hårdt for jeres uanstændige afguderi, og I skal forstå, at jeg er Herren.”