Ezekieli 22 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 22:1-31

Machimo a Yerusalemu

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa 3ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano, 4wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke. 5Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.

6“ ‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu. 7Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye. 8Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga. 9Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa. 10Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo. 11Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo. 12Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.

13“ ‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu. 14Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi. 15Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako. 16Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

17Yehova anandiyankhula nati: 18“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva. 19Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu. 20Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani. 21Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo. 22Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’ ”

23Yehova anandiyankhulanso nati, 24“Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’ 25Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye. 26Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo. 27Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa. 28Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule. 29Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.

30“Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze. 31Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 22:1-31

耶路撒冷的罪惡

1耶和華對我說: 2「人子啊,你要審判耶路撒冷這殺人流血的城。你要審判她,使她知道自己一切可憎的行為。 3你要向她宣告主耶和華的話,說,『唉,你這殺人流血、製造偶像玷污自己的城啊,你的末日到了。 4你既犯罪殺人、製造偶像玷污自己、自招審判,我要使你成為列國列邦侮辱和譏諷的對象。 5你這聲名狼藉、混亂不堪的城將要受到遠近各國的恥笑。

6「『看啊,在你城中的以色列首領各逞權勢,殺人流血。 7他們輕慢父母,壓迫寄居者,欺負孤兒寡婦。 8他們藐視我的聖物,褻瀆我的安息日。 9在你這城中,有人好誹謗、殺人流血,有人在山上吃祭物,有人淫亂, 10有人與繼母通姦,羞辱父親,有人姦污經期不潔的婦女, 11有人與鄰居的妻子幹出可憎之事,有人玷污自己的兒媳婦,有人姦污自己的同父姊妹。 12在你這城中,他們受賄殺人,放債取利,壓榨鄰居,早把我忘了。這是主耶和華說的。

13「『我見你謀財害命,就擊掌歎息。 14在我懲罰你的日子,你還有勇氣和力量嗎?我耶和華言出必行, 15我要把你驅散到列國,分散到列邦,我要除掉你的污穢。 16你必在列國面前受凌辱,你便知道我是耶和華。』」

17耶和華對我說: 18「人子啊,在我看來,以色列人已經變成了渣滓。他們是爐中的銅、錫、鐵、鉛,都是銀渣滓。 19所以主耶和華說,『你們既是渣滓,我要把你們聚集在耶路撒冷城。 20我要在烈怒中把你們聚集在城裡熔化,就像人把銀、銅、鐵、鉛、錫聚在高溫的爐中熔化一樣。 21我要聚集你們,把我的怒火倒在你們身上,熔化你們。 22你們要在城中熔化,就像銀在煉爐中熔化。你們就知道我耶和華已將我的烈怒傾倒在你們身上。』」

23耶和華對我說: 24「人子啊,你要對以色列說,『在我發怒的日子,將沒有雨水滋潤你這不潔之地。 25你的首領圖謀惡事,好像咆哮著撕碎獵物的獅子,他們草菅人命,搶奪財寶,使多人變成寡婦。 26你的祭司強解我的律法,褻瀆我的聖物。他們聖俗不分,也不教導人分辨潔淨的和污穢的。他們藐視我的安息日,褻瀆我。 27你的首領好像撕碎獵物的豺狼,殺人流血,謀取不義之財。 28你的先知對他們說虛假的異象和占卜,像用白灰刷牆一樣掩蓋他們的罪惡,說,耶和華這樣說,其實耶和華沒有說。 29你的居民強取豪奪,欺壓貧困的,虐待寄居的,無法無天。 30我想在他們中間尋找一位重修城牆的人,站在我面前為這地方堵住缺口,免得我毀滅這裡。可是,我一個也找不到。 31因此,我要向他們傾倒我的烈怒,用怒火滅盡他們,照他們的所作所為報應他們。這是主耶和華說的。』」