Ezekieli 21 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 21:1-32

Babuloni, Lupanga la Mulungu

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu. 3Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe. 4Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto. 5Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’

6“Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu. 7Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”

8Yehova anandiyankhulanso kuti, 9“Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti,

“Izi ndi zimene Yehova akunena:

Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.

10Lanoledwa kuti likaphe,

lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi!

“ ‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.

11“ ‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe,

ndi kuti linyamulidwe,

lanoledwa ndi kupukutidwa,

kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.

12Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu,

pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga;

zidzagweranso akalonga onse a Israeli.

Adzaphedwa ndi lupanga

pamodzi ndi anthu anga.

Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.

13“ ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’

14“Tsono mwana wa munthu, nenera

ndipo uwombe mʼmanja.

Lupanga likanthe kawiri

ngakhale katatu.

Limenelo ndilo lupanga lophera anthu.

Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa

limene likuwazungulira.

15Ndawayikira pa zipata zawo zonse

lupanga laphuliphuli

kuti ataye mtima

ndiponso kuti anthu ambiri agwe.

Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi

ndi kuti azilisolola kuphera anthu.

16Iwe lupanga, ipha anthu kumanja,

kenaka kumanzere,

kulikonse kumene msonga yako yaloza.

17Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga,

ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga

Ine Yehova ndayankhula.”

18Yehova anandiyankhulanso kuti, 19“Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda. 20Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa. 21Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe. 22Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo. 23Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.

24“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.

25“ ‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni, 26Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa. 27Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’

28“Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Lupanga, lupanga,

alisolola kuti liphe anthu,

alipukuta kuti liwononge

ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.

29Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza.

Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso.

Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa

amene tsiku lawo lafika,

ndiye kuti nthawi

ya kulangidwa kwawo komaliza.

30“ ‘Bwezerani lupanga mʼchimake.

Ku malo kumene inu munabadwira,

mʼdziko la makolo anu,

ndidzakuweruzani.

31Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu,

ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani.

Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza;

anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.

32Mudzakhala ngati nkhuni pa moto.

Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe.

Simudzakumbukiridwanso

pakuti Ine Yehova ndayankhula.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 21:1-32

耶和華審判的刀

1耶和華對我說: 2「人子啊,你要面向耶路撒冷,說預言斥責以色列和聖所, 3告訴以色列,耶和華這樣說,『我要與你為敵,我要拔刀將你那裡的義人和惡人一同消滅, 4從南到北不留一人, 5使世人都知道我耶和華已拔刀出鞘,不再收回。』 6人子啊,你要在他們面前哀歎,要傷心欲絕地哀歎。 7如果有人問你為什麼哀歎,你就說有噩耗傳來,聽見的人都膽戰心驚、兩手發軟、精神萎靡、膝弱如水。災難必很快發生。這是主耶和華說的。」

8耶和華對我說: 9「人子啊,你要說預言,告訴他們,耶和華這樣說,

『有一把刀,

有一把刀磨快擦亮了,

10磨得鋒利,為要殺戮,

擦得亮如閃電。

我們豈能因我兒的權杖而快樂?這刀鄙視一切權杖。 11這刀已交給人去擦亮,好握在手中,這刀已磨快擦亮,預備交給屠殺的人。 12人子啊,號啕大哭吧,因為這刀要攻擊我的子民和所有以色列的首領,他們都要死於刀下。所以你要捶胸頓足。 13這刀必試驗他們,這刀所鄙視的權杖若不復存在,怎麼辦呢?這是主耶和華說的。』

14「人子啊,你要拍掌對他們說預言,你要拿刀揮舞兩三次,預示這刀要從四面八方大肆殺戮, 15使他們嚇得肝膽俱裂,許多人倒在家門口。我已賜下這亮如閃電的刀,用來殺戮。 16刀啊,你要左砍右劈,大肆殺戮。 17我要拍掌,我的烈怒要平息。這是我耶和華說的。」

18耶和華對我說: 19「人子啊,你要為巴比倫王的刀畫出兩條進攻之路,兩條路要從一個地方出發,要在通往城邑的路口設路標。 20一條路通往亞捫拉巴城,一條路通往猶大的堅城耶路撒冷21巴比倫王將站在兩路的岔口,搖籤求問他的神像,察看祭牲的肝。 22他右手拿到的是攻打耶路撒冷的籤,於是,他用撞城錘來攻耶路撒冷的城門,廝殺吶喊,建壘築臺圍攻城池。 23猶大人必認為這是虛假的徵兆。他們曾向巴比倫王發誓效忠,但巴比倫王要使他們想起自己的罪,並擄走他們。

24「主耶和華說,『因為你們的過犯昭然若揭,你們的罪惡表露無遺,因此,你們必遭擄掠。 25你這邪惡敗壞的以色列首領啊!你的結局到了,審判你的日子來了。』 26主耶和華說,『取下你的頭巾,摘下你的冠冕吧,時局轉變了。要提拔卑微的,貶抑高貴的。 27毀滅,毀滅,我要毀滅這國,使它蕩然無存,直到那應得的人來到後,這國才能得到重建,我要把這國交給他。』

28「人子啊,你要說有關亞捫人及其恥辱的預言,告訴他們,主耶和華說,『有刀,有刀已出鞘,為要殺戮;它亮如閃電,要行毀滅。 29有關你們的異象和占卜是虛假的,你們將與其他惡人一同被殺,因為你們的結局到了,審判你們的日子來了。 30你們要收刀入鞘,我要在你們的家鄉,在你們的出生之地審判你們, 31我要把烈怒倒在你們身上,將我的怒火噴在你們身上,把你們交在嗜殺成性的惡徒手中, 32你們必被當作柴焚燒,你們的血必流在自己的土地上,無人再記得你們。因為這是我耶和華說的。』」