Ezekieli 21 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 21:1-32

Babuloni, Lupanga la Mulungu

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu. 3Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe. 4Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto. 5Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’

6“Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu. 7Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”

8Yehova anandiyankhulanso kuti, 9“Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti,

“Izi ndi zimene Yehova akunena:

Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.

10Lanoledwa kuti likaphe,

lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi!

“ ‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.

11“ ‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe,

ndi kuti linyamulidwe,

lanoledwa ndi kupukutidwa,

kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.

12Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu,

pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga;

zidzagweranso akalonga onse a Israeli.

Adzaphedwa ndi lupanga

pamodzi ndi anthu anga.

Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.

13“ ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’

14“Tsono mwana wa munthu, nenera

ndipo uwombe mʼmanja.

Lupanga likanthe kawiri

ngakhale katatu.

Limenelo ndilo lupanga lophera anthu.

Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa

limene likuwazungulira.

15Ndawayikira pa zipata zawo zonse

lupanga laphuliphuli

kuti ataye mtima

ndiponso kuti anthu ambiri agwe.

Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi

ndi kuti azilisolola kuphera anthu.

16Iwe lupanga, ipha anthu kumanja,

kenaka kumanzere,

kulikonse kumene msonga yako yaloza.

17Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga,

ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga

Ine Yehova ndayankhula.”

18Yehova anandiyankhulanso kuti, 19“Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda. 20Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa. 21Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe. 22Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo. 23Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.

24“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.

25“ ‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni, 26Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa. 27Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’

28“Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Lupanga, lupanga,

alisolola kuti liphe anthu,

alipukuta kuti liwononge

ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.

29Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza.

Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso.

Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa

amene tsiku lawo lafika,

ndiye kuti nthawi

ya kulangidwa kwawo komaliza.

30“ ‘Bwezerani lupanga mʼchimake.

Ku malo kumene inu munabadwira,

mʼdziko la makolo anu,

ndidzakuweruzani.

31Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu,

ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani.

Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza;

anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.

32Mudzakhala ngati nkhuni pa moto.

Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe.

Simudzakumbukiridwanso

pakuti Ine Yehova ndayankhula.’ ”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Езекиил 21:1-32

1Было ко мне слово Вечного:

2– Смертный, обрати лицо к Иерусалиму и пророчествуй против святилища. Пророчествуй о земле Исраила 3и скажи ей: Так говорит Вечный: «Я твой противник. Я вытащу меч из ножен и истреблю и твоих праведников, и твоих злодеев. 4Так как Я стану истреблять и праведников, и злодеев, Мой меч обнажится на всякую плоть с юга до севера. 5И всякая плоть узнает, что Я, Вечный, извлёк меч из ножен; больше он в них не вернётся».

6Итак, стони, смертный! Стони перед ними с разбитым сердцем и в тоске. 7Когда они спросят тебя: «Почему ты стонешь?» – отвечай: «Из-за вестей, что идут. Все сердца изнемогут, все руки потеряют силу; всякий дух ослабнет и всякое колено задрожит, как вода». Это придёт и непременно сбудется, – возвещает Владыка Вечный.

Вавилон – меч правосудия Аллаха

8Было ко мне слово Вечного:

9– Смертный, пророчествуй и скажи: Так говорит Вечный:

«Меч, меч

наточен и очищен –

10наточен для резни,

очищен, чтобы сверкать, как молния!»

– Как нам радоваться жезлу царя, если меч сильнее любой подобной деревяшки?

11– Меч дан, чтобы его очистили,

чтобы в руке зажали;

и наточен он, и очищен,

чтобы лечь губителю в руку.

12Смертный, кричи и плачь,

ведь он обратится на Мой народ;

на вождей Исраила он обратится.

Под меч они будут брошены

вместе с Моим народом.

Так бей себя в грудь от горя.

13Ведь испытание непременно придёт: и что, если жезл царя, который будет уничтожен мечом, прекратит своё существование? – возвещает Владыка Вечный.

14– Так пророчествуй, смертный,

бей о ладонь ладонью.

Пусть меч ударит дважды, трижды –

это меч для резни,

меч для великой бойни;

меч идёт к ним со всех сторон,

15чтобы сердцам изнемочь,

и умножиться павшим.

Лезвие меча

Я приставил ко всем их вратам.

Увы! Он сделан, чтобы сверкать,

он очищен для бойни.

16Бей направо, рази налево,

куда бы ни обратилось лезвие!

17Я тоже ударю о ладонь ладонью

и утолю Свой гнев.

Я, Вечный, сказал это.

18Было ко мне слово Вечного:

19– А ты, смертный, начерти две дороги, по которым пойдёт меч царя Вавилона; обе они пусть начинаются в одной земле. А там, где дорога поворачивает к городу, поставь путевой знак. 20Проведи одну дорогу, по которой пойдёт меч царя Вавилона, в аммонитскую столицу Раббу, а другую – в Иудею и укреплённый Иерусалим. 21Ведь царь Вавилона остановится у развилки, на распутье двух дорог, чтобы поворожить: он будет трясти стрелы, спрашивать своих домашних божков и разглядывать печень. 22В его правую руку попадётся жребий «на Иерусалим», чтобы поставить там стенобитные орудия, дать приказ убивать, издать боевой клич, приставить к воротам тараны, сделать насыпь и возвести осадные валы. 23Тем, кто поклялся ему в верности, это покажется ложным знамением, но он напомнит им об их вине и возьмёт их в плен.

24Поэтому так говорит Владыка Вечный:

– Вы напомнили о своей вине, ваш мятеж и ваши грехи стали явными во всём, что вы делаете. За это вас уведут в плен.

25А тебе, недостойный, преступный исраильский вождь, чей день настал, чей час наказания пробил, 26так говорит Владыка Вечный:

– Сними головной убор, сложи венец. Как было, так больше не будет: те, кто внизу, будут возвышены, а те, кто наверху, будут унижены. 27Гибель, гибель, гибель! Я наведу её! Не возродится эта земля, пока не придёт Тот, Кому она по праву принадлежит; Ему Я отдам её.

28– А ты, смертный, пророчествуй и скажи: Так говорит Владыка Вечный об аммонитянах и их оскорблениях:

«Меч, меч

обнажён для бойни,

начищен пожирать

и сверкать, словно молния!

29Несмотря на пустые видения о тебе

и лживые гадания,

он обрушится на шеи

обречённых на смерть злодеев,

чей день настал,

чей час наказания пробил.

30Верни его в ножны!

Там, где был сотворён ты,

в земле твоего рождения,

Я буду тебя судить.

31Я изолью на тебя Свою ярость,

пылающим гневом повею на тебя.

Я отдам тебя людям жестоким,

людям, приученным убивать.

32Будешь ты топливом для костра,

будет кровь твоя литься на землю,

вспоминать о тебе не будут;

ведь Я, Вечный, так сказал».