Ezekieli 20 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 20:1-49

Kuwukira kwa Israeli

1Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.

2Tsono Yehova anandiyankhula nati: 3“Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’

4“Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti, 5‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu. 6Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena. 7Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’

8“ ‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo. 9Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto. 10Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu. 11Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. 12Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.

13“ ‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu. 14Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto. 15Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse. 16Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano. 17Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu. 18Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo. 19Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga. 20Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’

21“ ‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo. 22Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo. 23Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali, 24chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo. 25Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo. 26Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’

27“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika. 28Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa. 29Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’

Chiweruzo ndi Kubwezeretsa

30“Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa? 31Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.

32“ ‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika. 33Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani. 34Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri. 35Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu. 36Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova. 37Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa. 38Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

39“ ‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano. 40Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika. 41Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona. 42Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu. 43Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita. 44Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Uneneri Wotsutsa Kummwera

45Yehova anandiyankhula nati: 46“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera. 47Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo. 48Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’ ”

49Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’ ”

O Livro

Ezequiel 20:1-49

Israel é rebelde

1Aconteceu no dia 10 do quinto mês20.1 Mês de Abe. Entre a lua nova do mês de julho e o mês de agosto., no sétimo ano do nosso exílio que alguns anciãos de Israel vieram ter comigo, pedindo-me instruções do Senhor, e sentaram-se diante de mim à espera de resposta.

2Então o Senhor transmitiu-me esta mensagem: 3“Homem mortal, diz aos anciãos de Israel, assim diz o Senhor Deus: Como ousam vir consultar-me? Garanto-vos que não direi nada daquilo que esperam!

4Julga-os tu, homem mortal, condena-os. Lembra-lhes todos os pecados desta nação, desde o tempo dos seus pais até agora. 5Diz-lhes estas palavras do Senhor Deus: Quando escolhi Israel e me revelei à nação, no Egito, jurei-lhes com a mão erguida, ao povo e aos seus descendentes: Eu sou o Senhor, vosso Deus! 6Naquele dia jurei solenemente que os tiraria dali e os levaria para uma terra que escolhi especialmente para eles, uma esplêndida terra onde jorra leite e mel, uma terra ótima entre todas as outras.

7Disse-lhes: ‘Desfaçam-se de toda a espécie de abominações; não se contaminem com os deuses do Egito, porque sou eu o Senhor, vosso Deus!’

8Mas eles rebelaram-se contra mim e não quiseram ouvir-me. Não abandonaram os abomináveis ídolos, nem puseram de parte os deuses do Egito. Pensei derramar a minha ira e fazê-los sentir a minha cólera, mesmo ainda quando estavam no Egito.

9No entanto, não o fiz, porque preferi preservar a honra do meu nome, visto que os egípcios haveriam de rir-se e dizer que o Deus de Israel não tinha sido capaz de os preservar do mal. 10Foi assim que acabei por tirar de lá o meu povo, mesmo na cara dos egípcios, levando-os para o deserto. 11Dei-lhes as minhas leis, com as quais, se as cumprissem, poderiam viver. 12Dei-lhes igualmente os meus sábados como sinal da relação que estabeleci com eles, para que se lembrassem de que sou eu, o Senhor, quem os santifica.

13Apesar disso, Israel tornou a virar-me as costas. Ali no deserto rejeitaram os meus mandamentos; não quiseram guardá-los, ainda que tal significasse para eles a vida, e desrespeitaram os meus sábados. Por isso, pensei derramar sobre eles a minha cólera e consumi-los totalmente ali mesmo no deserto.

14Mas novamente me detive, para manter a honra do meu nome, pois não queria que os povos que me viram trazê-los para fora do Egito dissessem que foi por não poder cuidar deles que os destruía. 15Jurei-lhes, no entanto, que não os levaria para a terra que lhes prometera, essa rica terra onde jorravam leite e mel, o melhor lugar da Terra. 16Porque se tinham rido das minhas leis, ignorando a minha vontade, abusando dos meus sábados; os seus corações continuavam a correr atrás dos ídolos. 17Porém, poupei-os e não acabei com eles ali no deserto.

18Dirigi-me depois aos seus filhos no deserto: ‘Não sigam as leis que os vossos antepassados fizeram, nem sigam as pisadas dos vossos pais; não se contaminem com os ídolos deles. 19Porque eu sou o Senhor, vosso Deus, sigam as minhas leis e cumpram fielmente os meus mandamentos. 20Santifiquem os meus sábados, que são um sinal da aliança estabelecida convosco, para vos recordar que eu sou o Senhor, vosso Deus.’

21Mas também os filhos deles se revoltaram contra mim e recusaram obedecer às minhas leis, leis que significavam a vida para quem as guardasse, e profanaram os meus sábados. Então disse: ‘Agora sim, é que vou castigar-vos com toda a severidade, aqui no deserto.’

22O certo é que novamente desisti da minha sentença contra eles, a fim de proteger o meu nome entre as nações que tinham sido testemunhas do meu poder ao tirá-los do Egito. 23Em todo o caso, fiz um juramento solene contra eles, enquanto estavam no deserto, que os dispersaria até aos confins da Terra, 24por não terem obedecido às minhas leis, por as terem desprezado, violado os meus sábados e corrido atrás dos ídolos dos seus pais. 25Deixei-os adotar costumes e princípios indignos e com essas coisas o destino deles nunca poderia ser a vida! 26Na esperança de que arrepiassem caminho, horrorizados com as coisas que faziam e que viessem a dar-se conta, enfim, que só eu sou o Senhor, permiti que se poluíssem até com os dons que lhes dera. Chegaram ao ponto de imolar pelo fogo os seus próprios filhos, como sacrifícios aos seus deuses!

27Homem mortal, dá-lhes a conhecer que o Senhor Deus lhes diz o seguinte: Os vossos pais continuaram a blasfemar de mim e a trair-me, 28mesmo depois de os ter trazido para a terra que lhes prometera, pois ofereceram sacrifícios e incenso sobre todas as colinas e debaixo das árvores, e suscitaram a minha ira, oferecendo sacrifícios a esses tais deuses. Trouxeram perfumes e incenso e derramaram perante eles as suas ofertas de vinho! 29Perguntei-lhes: ‘Que lugar de sacrifício é esse onde vão?’ E a partir daí começou a chamar-se lugares altos20.29 O termo implica altar idólatra de sacrifício em lugar elevado. aos santuários pagãos.

Juízo e restauração

30Portanto, declara aos israelitas: O Senhor Deus quer saber se vão continuar a contaminar-se, como o fizeram os vossos antepassados, se vão continuar a prostituir-se, entregando-vos a esses ídolos abomináveis? 31Porque quando lhes trazem ofertas e lhes oferecem em sacrifício as vossas crianças, para serem reduzidas a cinzas, como fazem ainda hoje, haveria eu de ouvir e ajudar-vos, ó Israel? Tão certo como eu viver, diz o Senhor Deus, não hão de receber qualquer outro tipo de mensagem, quando me procurarem.

32Aquilo que no íntimo desejam, isso não há de acontecer, que é serem como os outros povos à vossa volta e andarem a prestar culto a deuses de madeira e de pedra. 33Tão certo como eu viver, diz o Senhor Deus, dirigir-vos-ei com pulso de ferro no meio de grande rigor e poder. 34Com dominação e grande severidade vos trarei das terras para onde foram espalhados. 35Vou trazer-vos ao deserto do meu tribunal e ali vos julgarei face a face, 36tal como fiz nos primeiros tempos, também no deserto, após vos ter tirado do Egito, diz o Senhor Deus. 37Examinar-vos-ei cuidadosamente debaixo da minha vara e vos farei cumprir as obrigações da minha aliança. 38Os outros, os rebeldes, que pecaram contra mim, expurgá-los-ei do vosso meio. Hei de expusá-los, sim, das terras onde estiverem exilados, mas em Israel não hão de entrar. Quando tal acontecer vocês saberão que eu sou o Senhor!

39Ó Israel, o Senhor Deus diz: Se insistem em adorar ídolos, continuem. Contudo, mais tarde acabarão por me ouvir e não mais profanarão o meu santo nome com as vossas ofertas e com os vossos ídolos. 40Porque no meu santo monte, no alto monte de Israel, diz o Senhor Deus, que todo o Israel deverá adorar-me. É lá que aceito e peço que me tragam as vossas oferendas e o melhor dos vossos dons. 41Vocês mesmos serão para mim como uma oferta de incenso perfumado, quando vos trouxer do exílio, e os outros povos hão de ver a grande mudança do vosso coração. 42Nessa altura, quando vos tiver trazido para casa, para a terra que já prometera aos vossos antepassados, saberão que eu sou o Senhor. 43Então, ao considerarem o vosso passado e todos os vossos pecados, terão nojo de vós mesmos, por causa do mal que fizeram. 44Saberão que eu sou o Senhor, quando eu agir convosco por amor ao meu santo nome, abençoando-vos, a despeito da vossa maldade e atos corruptos, ó Israel, diz o Senhor Deus!”

Profecia contra o sul

45Chegou até mim esta mensagem do Senhor: 46“Homem mortal, olha em direção ao sul, a Jerusalém, e dirige estas palavras contra ela e contra as terras arborizadas do Negueve. 47Diz à floresta que fica a sul: Ouve a palavra do Senhor! Acenderei em ti um fogo, ó floresta, que consumirá todas as árvores, tanto as verdes como as que já estão a secar. As chamas ardentes que se levantarem não se extinguirão e estender-se-ão desde o Negueve até às fronteiras do norte. 48O mundo inteiro se dará conta de que fui eu, o Senhor, que ateei esse fogo, o qual não se apagará.”

49Então eu disse: “Ó Senhor Deus, eles dizem de mim que não passo de um contador de parábolas!”