Ezekieli 20 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 20:1-49

Kuwukira kwa Israeli

1Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.

2Tsono Yehova anandiyankhula nati: 3“Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’

4“Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti, 5‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu. 6Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena. 7Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’

8“ ‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo. 9Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto. 10Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu. 11Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. 12Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.

13“ ‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu. 14Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto. 15Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse. 16Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano. 17Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu. 18Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo. 19Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga. 20Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’

21“ ‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo. 22Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo. 23Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali, 24chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo. 25Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo. 26Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’

27“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika. 28Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa. 29Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’

Chiweruzo ndi Kubwezeretsa

30“Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa? 31Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.

32“ ‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika. 33Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani. 34Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri. 35Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu. 36Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova. 37Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa. 38Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

39“ ‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano. 40Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika. 41Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona. 42Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu. 43Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita. 44Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Uneneri Wotsutsa Kummwera

45Yehova anandiyankhula nati: 46“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera. 47Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo. 48Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’ ”

49Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’ ”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Езекиил 20:1-49

Мятежный Исроил

1В седьмом году, в десятый день пятого месяца (14 августа 591 г. до н. э.), некоторые из старейшин Исроила пришли спросить Вечного и сели передо мной.

2И было ко мне слово Вечного:

3– Смертный, говори со старейшинами Исроила и скажи им: Так говорит Владыка Вечный: «Вы пришли вопрошать Меня? Верно, как и то, что Я живу, – Я не позволю вам вопрошать Меня», – возвещает Владыка Вечный.

4Будешь ли судить их? Будешь ли судить их, смертный? Тогда укажи им на омерзительные обычаи их предков 5и скажи им: Так говорит Владыка Вечный: «В день, когда Я избрал Исроил, Я с поднятой рукой поклялся потомкам Якуба и открылся им в Египте. С поднятой рукой Я сказал им: „Я – Вечный, ваш Бог“. 6В тот день Я поклялся им, что выведу их из Египта в землю, которую Я для них усмотрел, в землю, где течёт молоко и мёд, прекраснейшую из земель, 7и сказал им: „Пусть каждый отвергнет гнусные истуканы, которыми вы любуетесь, и идолами Египта не оскверняется. Я – Вечный, ваш Бог“.

8Но они восстали против Меня и не стали Меня слушать; они не отвергли гнусные истуканы, которыми любовались, и не отвергли идолов Египта. Тогда Я сказал, что изолью на них Свою ярость и обращу на них Свой гнев в земле Египта. 9Но ради Моего имени Я поступил так, чтобы оно не осквернилось у народов, среди которых они жили и на глазах у которых Я открылся исроильтянам, выведя их из Египта. 10Поэтому Я вывел их из Египта и привёл в пустыню. 11Я дал им Мои установления и объявил Мои законы, потому что тот, кто исполняет их, будет жив ими. 12Ещё Я дал им Мои субботы20:12 Суббота – седьмой день недели у иудеев, день, посвящённый Вечному. В этот день, согласно повелению Вечного, исроильский народ должен был отдыхать и совершать ритуальные приношения (см. Исх. 31:12-17; Чис. 28:9-10). как знак между нами, чтобы они знали, что Я, Вечный, их освящаю.

13Но народ Исроила восстал против Меня в пустыне. Они не соблюдали Моих установлений и отвергли Мои законы – хотя тот, кто исполняет их, будет жив ими – и полностью осквернили Мои субботы. Тогда Я сказал, что изолью на них Свою ярость и погублю их в пустыне. 14Но ради Моего имени Я поступил так, чтобы оно не осквернилось у народов, на глазах у которых Я вывел их. 15И с поднятой рукой Я поклялся им в пустыне, что не приведу их в землю, которую им отдал, в землю, где течёт молоко и мёд, прекраснейшую из земель, 16потому что они отвергли Мои законы, не соблюдали Моих установлений и оскверняли Мои субботы. Ведь их сердца были преданы идолам. 17Но Я взглянул на них с жалостью и не погубил, не уничтожил их в пустыне. 18В пустыне Я сказал их детям: „Не исполняйте установлений и законов ваших отцов и не оскверняйте себя их идолами. 19Я – Вечный, ваш Бог; следуйте Моим установлениям и прилежно исполняйте Мои законы. 20Храните Мои субботы святыми, чтобы они были знаком соглашения между нами. Тогда вы узнаете, что Я – Вечный, ваш Бог“.

21Но их дети восстали против Меня: они не исполняли Моих установлений, не старались исполнять Мои законы – хотя тот, кто исполняет их, будет жив ими – и оскверняли Мои субботы. Тогда Я сказал, что изолью на них в пустыне Свою ярость и обращу на них Свой гнев. 22Но Я удержал Свою руку и ради Моего имени поступил так, чтобы оно не осквернилось у народов, на глазах у которых Я их вывел. 23И с поднятой рукой Я поклялся им в пустыне, что рассею их среди народов и разбросаю по странам 24за то, что они не исполняли Моих законов, отвергли Мои установления и оскверняли Мои субботы, а глаза их были обращены к идолам их отцов. 25Поэтому Я позволил им следовать установлениям, которые не были хороши, и законам, по которым нельзя жить. 26Я разрешил им оскверняться их дарами – принесением в огненную жертву каждого первенца, – чтобы ужаснуть их, чтобы они узнали, что Я – Вечный».

27Поэтому, смертный, говори с народом Исроила и скажи им: Так говорит Владыка Вечный: «Этим ваши предки тоже оскорбляли Меня, поступая со Мной вероломно. 28Я привёл их в землю, которую клялся им дать, а они, завидев высокий холм или тенистое дерево, приносили там жертвы, совершали приношения, которые возбуждали Мой гнев, возносили благовония и воздавали жертвенные возлияния. 29Я спросил их: „Что это за возвышенность, на которую вы ходите?“»

(Поэтому такие капища называются «возвышенностями»20:29 На языке оригинала: «Бама». и до сегодняшнего дня.)

Наказание и возрождение

30– Поэтому скажи исроильтянам: Так говорит Владыка Вечный: «Вы хотите осквернять себя по примеру отцов и блудить с их гнусными истуканами? 31Когда вы приносите дары и сжигаете детей, принося их в жертву, вы по-прежнему оскверняете себя своими идолами. Неужели Я позволю вам вопрошать Меня, о народ Исроила? Верно, как и то, что Я живу, – возвещает Владыка Вечный, – Я не позволю вам вопрошать Меня.

32Вы говорите: „Мы хотим быть как все народы, племена земли, которые служат дереву и камню“, но вовеки не бывать тому, что у вас на уме. 33Верно, как и то, что Я живу, – возвещает Владыка Вечный, – Я буду править вами могучей и простёртой рукой и великой яростью. 34Я выведу вас из народов и соберу из стран, где вы были рассеяны, могучей и простёртой рукой и великой яростью. 35Я изгоню вас в пустыню народов20:35 Пустыня народов – так названа, как полагают, сирийская пустыня, простиравшаяся между Палестиной и Вавилоном и принадлежавшая территориально многим народам. и там буду судиться с вами лицом к лицу. 36Подобно тому, как Я судился с вашими предками в пустыне земли Египта, так Я буду судиться и с вами, – возвещает Владыка Вечный. – 37Я проведу вас под пастушеским посохом, чтобы посчитать и осмотреть вас, и введу в узы соглашения. 38Я очищу вас от тех, кто взбунтовался и восстал против Меня. Хотя Я и выведу их из земли, где они живут как пришельцы, но в землю Исроила они не войдут. Тогда вы узнаете, что Я – Вечный».

39А о вас, исроильтяне, так говорит Владыка Вечный: «Ступайте, служите каждый своим идолам, если не будете слушать Меня! Но вам больше не осквернять Моего святого имени своими дарами и идолами. 40Ведь на Моей святой горе, на горной вершине Исроила, – возвещает Владыка Вечный, – там, в той земле, весь народ Исроила будет служить Мне, и там Я приму их с благоволением. Там Я потребую ваших приношений и лучших даров20:40 Или: «первых плодов». со всеми священными жертвами. 41Я приму вас, как приятный запах благовоний, когда выведу из народов и соберу из стран, где вы были рассеяны, и явлю среди вас Свою святость на глазах у народов. 42Тогда вы узнаете, что Я – Вечный, когда Я приведу вас в землю Исроила, в землю, которую Я с поднятой рукой клялся отдать вашим предкам. 43Там вы вспомните свои пути и дела, которыми оскверняли себя, и будете гнушаться себя из-за зла, которое сделали. 44Вы узнаете, что Я – Вечный, когда Я поступлю с вами ради Моего имени, а не по вашим злым путям и скверным делам, о народ Исроила», – возвещает Владыка Вечный.

Огонь и меч против Иерусалима

45Было ко мне слово Вечного:

46– Смертный, обрати лицо на юг; проповедуй против южных земель и пророчествуй о лесах южного края. 47Скажи лесу южного края: Слушай слово Вечного. Так говорит Владыка Вечный: «Гляди, Я зажигаю среди тебя огонь, и он уничтожит все твои деревья, и зелёные, и засохшие. Не погаснет пылающее пламя, и вся земля с юга до севера будет опалена им. 48Всякая плоть увидит, что Я, Вечный, зажёг его; оно не погаснет».

49Тогда я сказал:

– О Владыка Вечный! Они говорят мне: «Разве он говорит не притчами?»