Ezekieli 18 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 18:1-32

Munthu Wochimwa Adzafa

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti:

“ ‘Nkhuyu zodya akulu zimapota

ndi ana omwe?’ ”

3“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli. 4Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.

5“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama

amene amachita zolungama ndi zolondola.

6Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo

kapena kupembedza mafano a Aisraeli.

Iye sayipitsa mkazi wa mnzake

kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.

7Iye sapondereza munthu wina aliyense,

koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake.

Iye salanda zinthu za osauka,

koma amapereka chakudya kwa anthu anjala,

ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.

8Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira,

kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu.

Amadziletsa kuchita zoyipa

ndipo sakondera poweruza milandu.

9Iye amatsatira malangizo anga,

ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika.

Munthu ameneyo ndi wolungama;

iye adzakhala ndithu ndi moyo,

akutero Ambuye Yehova.

10“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere. 11Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo.

“Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo.

Amayipitsa mkazi wa mnzake.

12Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa.

Amalanda zinthu za osauka.

Sabweza chikole cha munthu wa ngongole.

Iye amatembenukira ku mafano

nachita zonyansa.

13Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu.

Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.

14“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.

15“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo.

Sapembedza mafano a ku Israeli.

Sayipitsa mkazi wa mnzake.

16Sapondereza munthu wina aliyense.

Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka.

Salanda zinthu za munthu.

Amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.

17Amadziletsa kuchita zoyipa.

Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja.

Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga.

Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu. 18Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.

19“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse. 20Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.

21“ ‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi. 22Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo. 23Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.

24“ ‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.

25“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama? 26Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo. 27Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake. 28Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa. 29Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?

30“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo. 31Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli? 32Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 18:1-32

犯罪者必滅亡

1耶和華對我說: 2「你們以色列人為什麼說『父親吃了酸葡萄,兒子的牙酸倒了』這句俗語呢? 3主耶和華說,我憑我的永恆起誓,你們在以色列必不再用這句話。 4因為所有的生命都屬於我,父和子都屬於我。誰犯罪,誰死亡。

5「倘若有義人秉公行義, 6不在山上的廟宇裡吃祭物,不拜以色列的偶像,不玷污別人的妻子,不親近經期中的婦女; 7不欺壓人,反而退還債戶的抵押品;不搶奪財物,反而給饑餓的人食物吃,給赤身露體的人衣服穿; 8不放債取利,不犯罪作惡,反而公平待人, 9遵守我的律例,順從我的典章——這樣的義人必能活著。這是主耶和華說的。

10「倘若這人生了一個不肖子,兇殘暴戾,殺人搶劫,無惡不作, 11常在廟宇吃祭偶像之物,玷污別人的妻子, 12欺壓貧窮困苦的人,搶奪財物,扣留債戶的抵押品,祭拜偶像,犯罪作惡, 13放債取利,這樣的人還能活著嗎?他必不能活。他作惡多端,必自取滅亡,抵償自己的血債。

14「倘若這不肖子有一個好兒子,他看見父親的所作所為,不願步父親的後塵。 15他不肯在山上吃祭偶像之物,不拜以色列人的偶像,不玷污別人的妻子, 16不欺壓他人,不扣留抵押品,不搶奪財物,反而給饑餓的人食物吃,給赤身露體的人衣服穿, 17不壓榨貧窮的人,不放債取利,反而遵守我的典章,順從我的律例,這人必不因父親的罪惡而死亡,他必活著。 18他父親因肆意欺詐,掠奪同胞,多行不義,必自招滅亡。

19「你們會問,『兒子為什麼不用承擔父親的罪惡呢?』這是因為兒子秉公行義,謹遵我的律例,所以他必活著。 20誰犯罪,誰死亡,兒子不用承擔父親的罪惡,父親也不用承擔兒子的罪惡。義人必有善報,惡人必有惡報。

21「惡人若肯痛改前非,遵守我的律例,秉公行義,就必活著,不致死亡。 22我必不追究他以前所犯的一切罪行,他必因行事正直而活著。 23主耶和華說,我難道喜歡惡人死亡嗎?我豈不是更願他們痛改前非並活著嗎? 24義人若棄善行惡,與惡人同流合污,這人豈能活著?他從前的義行不會被記念,他必因自己的背信和罪惡而滅亡。

25「你們說,主這樣做不公平。以色列人啊,你們聽著,是我的做法不公平呢?還是你們的做法不公平呢? 26倘若義人離義行惡,他必因犯罪而死。 27倘若惡人離惡行義,他必救回自己的性命。 28因為他醒悟過來,痛改前非,必能活著,不致死亡。 29以色列人卻說,『主這樣做不公平!』以色列人啊,是我的做法不公平呢?還是你們的做法不公平呢?

30「所以主耶和華說,『以色列人啊,我必按你們各人的行為審判你們。你們要悔改,痛改前非,使你們不致死在罪惡中。 31你們要離棄從前所有的罪惡,洗心革面。以色列人啊!你們何必走向滅亡呢?』 32主耶和華說,『我斷不喜歡任何人死亡,你們要悔改,以便存活。』」