Ezekieli 18 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 18:1-32

Munthu Wochimwa Adzafa

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti:

“ ‘Nkhuyu zodya akulu zimapota

ndi ana omwe?’ ”

3“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli. 4Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.

5“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama

amene amachita zolungama ndi zolondola.

6Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo

kapena kupembedza mafano a Aisraeli.

Iye sayipitsa mkazi wa mnzake

kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.

7Iye sapondereza munthu wina aliyense,

koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake.

Iye salanda zinthu za osauka,

koma amapereka chakudya kwa anthu anjala,

ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.

8Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira,

kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu.

Amadziletsa kuchita zoyipa

ndipo sakondera poweruza milandu.

9Iye amatsatira malangizo anga,

ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika.

Munthu ameneyo ndi wolungama;

iye adzakhala ndithu ndi moyo,

akutero Ambuye Yehova.

10“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere. 11Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo.

“Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo.

Amayipitsa mkazi wa mnzake.

12Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa.

Amalanda zinthu za osauka.

Sabweza chikole cha munthu wa ngongole.

Iye amatembenukira ku mafano

nachita zonyansa.

13Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu.

Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.

14“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.

15“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo.

Sapembedza mafano a ku Israeli.

Sayipitsa mkazi wa mnzake.

16Sapondereza munthu wina aliyense.

Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka.

Salanda zinthu za munthu.

Amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.

17Amadziletsa kuchita zoyipa.

Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja.

Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga.

Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu. 18Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.

19“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse. 20Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.

21“ ‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi. 22Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo. 23Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.

24“ ‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.

25“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama? 26Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo. 27Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake. 28Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa. 29Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?

30“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo. 31Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli? 32Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

La Bible du Semeur

Ezéchiel 18:1-32

La responsabilité individuelle

1L’Eternel m’adressa la parole et me dit18.1 Pour les v. 1-20, voir 14.12-20 ; Jr 31.29-30 et Dt 7.10 ; 24.16. :

2Qu’avez-vous à répéter ce proverbe dans le pays d’Israël : « Les pères ont mangé des raisins verts, mais ce sont les dents des enfants qui en sont agacées » ? 3Aussi vrai que je suis vivant, le Seigneur, l’Eternel, le déclare, vous n’aurez plus lieu de répéter ce proverbe en Israël. 4Voici : toute personne m’appartient, les fils comme les pères m’appartiennent. Eh bien, c’est la personne qui pèche qui mourra.

5Soit un homme qui est juste et qui agit avec droiture et selon la justice. 6Il ne participe pas aux repas de sacrifice sur les montagnes et ne tourne pas les regards vers les idoles de la communauté d’Israël, il ne déshonore pas la femme d’autrui et n’a pas de relations avec une femme quand elle est indisposée18.6 Voir Lv 18.19.. 7Il n’exploite personne, il restitue son gage à celui qui lui a emprunté de l’argent, il ne commet pas de vol, il donne son pain à celui qui a faim et des vêtements à celui qui n’en a pas. 8Il ne prête pas à un taux usuraire et ne retient pas d’intérêts18.8 Voir Lv 25.36-37., il évite de commettre l’injustice et, s’il doit arbitrer entre un homme et un autre, il rend un jugement selon la vérité. 9Il vit en accord avec mes lois et obéit à mes commandements pour agir loyalement. Un tel homme est juste et il vivra, le Seigneur, l’Eternel, le déclare.

10Mais si cet homme a un fils qui est un brigand, un criminel, et qui est coupable de l’un de ces actes, 11alors que son père n’en a commis aucun : il participe aux repas sacrificiels sur les montagnes, ou il déshonore la femme d’autrui, 12ou il exploite les pauvres et les démunis, il commet des vols, ne rend pas les gages reçus, ou il porte les regards sur les idoles et prend part à des rites abominables. 13Ou encore, il prête à un taux usuraire et retient des intérêts. Ce fils-là vivrait-il ? Non, vous dis-je, il ne vivra pas. Puisqu’il a commis toutes ces choses abominables, il mourra et il sera seul responsable de sa mort.

14Si maintenant cet homme a un fils qui est témoin de toutes les fautes commises par son père. Bien qu’il ait vu ces fautes, ce fils ne les a pas imitées. 15Il ne participe pas aux repas de sacrifice sur les montagnes, il ne porte pas ses regards sur les idoles de la communauté d’Israël, il ne déshonore pas la femme d’autrui. 16Il n’exploite personne, ne retient pas de gage, ne commet pas de vol, mais il donne son pain à celui qui a faim et des vêtements à celui qui n’en a pas. 17Il ne fait pas de tort au pauvre18.17 D’après le texte hébreu traditionnel. L’ancienne version grecque a : il ne commet pas d’injustice., ne prête pas à un taux usuraire, ni ne retient des intérêts. Il applique mes lois et vit selon mes commandements. Eh bien, ce fils-là ne mourra pas pour les fautes de son père : il vivra. 18C’est son père, qui a opprimé autrui, qui a volé son prochain et n’a pas bien agi au milieu de son peuple, c’est lui qui mourra pour ses propres fautes.

19Vous demandez : Pourquoi le fils ne paie-t-il pas pour les fautes de son père ? Eh bien : Parce que le fils a agi avec droiture et selon la justice, parce qu’il a obéi à tous mes commandements et les a appliqués, il vivra. 20C’est la personne qui pèche qui mourra et le fils ne sera pas tenu pour responsable de la faute de son père, ni le père tenu pour responsable de la faute de son fils. A celui qui est juste, sa droiture sera portée à son compte, et l’on portera au compte du méchant sa méchanceté.

21Si le méchant se détourne de toutes les fautes qu’il a commises, s’il obéit à tous mes commandements et agit avec droiture et selon la justice, il ne mourra pas, il vivra. 22Parce qu’il mène à présent une vie juste, on ne tiendra plus compte de tous les péchés qu’il a commis, et il vivra. 23Pensez-vous que je prenne le moindre plaisir à voir mourir le méchant ? demande le Seigneur, l’Eternel. Mon désir n’est-il pas plutôt qu’il abandonne sa mauvaise conduite et qu’il vive ? 24Mais si le juste abandonne sa droiture et se met à faire le mal, en imitant toutes les pratiques abominables du méchant, pensez-vous qu’il vivra ? On ne tiendra plus compte de tous les actes justes qu’il a accomplis par le passé et il mourra à cause de ses transgressions et de ses fautes.

25Vous prétendez : « La manière d’agir du Seigneur n’est pas équitable. » Ecoutez donc, gens d’Israël, est-ce ma manière d’agir qui n’est pas équitable ? N’est-ce pas plutôt la vôtre ? 26Si le juste abandonne la droiture et se met à faire le mal et s’il meurt pour cela, c’est bien à cause du mal qu’il a commis qu’il perd la vie. 27Et si le méchant renonce à la méchanceté avec laquelle il a agi pour vivre désormais dans la droiture et selon la justice, il sauvera sa vie. 28S’il considère tous les péchés qu’il a commis et s’en détourne, il vivra, il ne mourra pas. 29Et pourtant, les gens d’Israël prétendent que la manière d’agir du Seigneur n’est pas équitable. Est-ce vraiment ma manière d’agir qui n’est pas équitable, gens d’Israël ? N’est-ce pas plutôt la vôtre ?

30Ainsi donc, je jugerai chacun de vous, gens d’Israël, selon sa conduite, le Seigneur, l’Eternel, le déclare. Changez donc d’attitude et détournez-vous de tous vos péchés, pour que vos fautes ne causent pas votre perte. 31Rejetez loin de vous tous les péchés que vous avez commis contre moi. Faites-vous un cœur nouveau et un état d’esprit nouveau, car pourquoi faudrait-il que vous mouriez, gens d’Israël ? 32Vraiment, moi, je ne prends aucun plaisir à voir mourir qui que ce soit, le Seigneur, l’Eternel, le déclare. Convertissez-vous et vivez !