Ezekieli 16 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 16:1-63

Kusakhulupirika kwa Yerusalemu

1Yehova anayankhula nane kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa. 3Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti. 4Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu. 5Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.

6“ ‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’ 7ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.

8“ ‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.

9“ ‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta. 10Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta. 11Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako, 12ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako. 13Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi. 14Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.

15“ ‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake. 16Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso. 17Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama. 18Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo. 19Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

20“ ‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire 21kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo? 22Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.

23“ ‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse, 24wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse. 25Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo. 26Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako. 27Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa. 28Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe. 29Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.

30“ ‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi. 31Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.

32“ ‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako! 33Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe. 34Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.

35“ ‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova! 36Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano, 37nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse. 38Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri. 39Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa. 40Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo. 41Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako. 42Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.

43“ ‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.

44“ ‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’ 45Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori. 46Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi. 47Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo. 48Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.

49“ ‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi. 50Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu. 51Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye. 52Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.

53“ ‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu. 54Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa. 55Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja. 56Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu 57kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza. 58Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.

59“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa. 60Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe. 61Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe. 62Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 63Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 16:1-63

耶路撒冷的不忠

1耶和华对我说: 2“人子啊,你要使耶路撒冷知道她的可憎行径。 3你要告诉她,主耶和华这样对她说,‘你祖居迦南,生于迦南。你的父亲是亚摩利人,母亲是人。 4你出生时没人剪断你的脐带,没人用水洗你的身体,用盐擦净你,用布包裹你。 5没有人可怜你,同情你,为你做以上的事。你生下来便遭人厌恶,被扔在野外。

6“‘我从你旁边经过,见你在血泊中挣扎,便对血泊中的你说,活下去! 7我使你像田间的植物一样茁壮生长。你渐渐发育成熟,长得亭亭玉立,双乳丰满,秀发垂肩,但仍然赤身露体。

8“‘后来我又从你旁边经过,见你正值少女怀春,我便用衣襟遮盖你的身体,向你起誓,与你定下婚约,你便属于我。这是主耶和华说的。 9我用水洗净你身上的血污,给你涂上馨香的油, 10穿上锦绣的衣裳和海狗皮的鞋,披上细麻衣和丝绸外袍。 11我用首饰来装扮你,给你戴上手镯、项链、 12鼻环、耳环和华冠。 13这样,你戴的是金银首饰,穿的是绫罗绸缎,吃的是细面粉、蜂蜜和油。你变得美艳绝伦,晋升为王后。 14你的美貌名扬四方,因为我给你的华贵使你美貌无比。这是主耶和华说的。

15“‘你却仗着自己的美貌和名声纵情淫乱,与所有过路的人苟合。 16你用自己的衣服在拜偶像的地方结彩,在那里行淫。这样的事真是空前绝后! 17你用我给你的金银首饰为自己制造男人的像,与他们苟合。 18你给他们穿上锦绣衣服,把我给你的膏油和香料供奉他们。 19你把我赐你吃的细面粉、油和蜂蜜作为馨香的供物奉献在他们面前。这是主耶和华说的。 20你还把你给我生的儿女烧作燔祭献给偶像。难道你淫乱还不够吗? 21你竟屠杀我的儿女,把他们焚烧献给偶像。 22你做这一切可憎、淫乱的事,忘记了你幼年赤身露体,在血泊中挣扎的日子。

23“‘主耶和华说,你有祸了!你有祸了!你不但做了这些恶事, 24还为自己筑祭坛,在各广场建高高的神庙。 25你在街头巷尾建高高的神庙,糟蹋自己的美貌。你向每一个过路的人投怀送抱,纵情淫乱, 26甚至与放纵情欲的邻邦埃及人苟合,激起我的愤怒。 27看吧,我要伸手攻击你,削减你的口粮,把你交给憎恨你的非利士人,任他们宰割。他们会为你的淫荡行为感到羞耻。 28你欲海难填,又跟亚述人行淫,但仍不满足, 29于是又跟那商贾之地的迦勒底人行淫,但仍不满足。

30“‘主耶和华说,你的心败坏至极,简直就像不知羞耻的娼妓, 31因为你在街头巷尾筑祭坛,在广场建高高的神庙,甚至不收淫资,实在连妓女都不如。 32你这荡妇,宁愿跟外人淫乱,也不爱自己的丈夫。 33妓女接受淫资,你却送礼物给所有的情人,引诱他们从四方前来跟你淫乱。 34你卖淫不同于别的妓女,没有人给你淫资,你倒贴钱给人,你真是与众不同。

主对耶路撒冷的审判和应许

35“‘你这淫妇,要听耶和华的话。 36主耶和华说,你放纵情欲,赤身露体地与众情人苟合。你祭拜一切可憎的偶像,把自己儿女的血献给它们。 37因此,我要把你所爱和所恨的情人都聚集起来,从四方攻击你,让你赤裸裸地显露在他们面前,让他们看到你赤身露体。 38我要惩罚你,像惩罚淫乱和杀人的妇女一样。我要把烈怒和义愤倒在你身上,报应你杀人流血的罪。 39我要把你交在你的情人手里。他们必拆毁你的祭坛,夷平你高高的神庙,剥去你的衣裳,夺走你的珠宝,留下你赤身露体。 40他们要聚众攻击你,用石头打你,用刀剑砍碎你, 41烧毁你的房屋,在众妇女面前审判你。我要阻止你的淫乱行为,使你不再倒贴钱给情人。 42这样,我的烈怒才会平息,我的义愤才会消除,我才会平静下来,不再发怒。 43因为你忘记了幼年的日子,做这些事来惹我发怒,我要照你的所作所为报应你。因为你不仅行一切可憎的事,还放荡淫乱。这是主耶和华说的。

44“‘好说俗语的人都会讥讽你说,有其母必有其女。 45你和你母亲及姊妹如出一辙,都厌弃自己的丈夫和儿女。你母亲是人,你父亲是亚摩利人。 46你姐姐是撒玛利亚,她和她的女儿们住在你的北面。你妹妹是所多玛,她和她的女儿们住在你的南面。 47你不仅追随她们可憎的行径,还很快超过了她们。 48我凭我的永恒起誓,与你妹妹所多玛和她女儿们相比,你和你女儿们的行径有过之而无不及。这是主耶和华说的。 49看啊,你妹妹所多玛和她的女儿们傲慢狂妄,安逸饱足,对穷困的人漠不关心。 50她们心骄气傲,在我面前做可憎的事,我看见后便除掉了她们。 51撒玛利亚的罪还不及你的一半,你做的事比她们做的更可憎,以致与你相比,你的姊妹倒显得公义了。 52既然你帮了你的姊妹,使她们显得公义,你就蒙受羞辱吧!因为你犯的罪比你姊妹犯的罪更可憎,以致她们显得比你更公义。因此,你就自取其辱,抱愧蒙羞吧!

53“‘然而,我要使所多玛撒玛利亚及她们的女儿们复兴,并使你一同复兴, 54让你自取其辱,深感羞愧,因为你的一切恶行使她们反得安慰。 55你姊妹所多玛撒玛利亚和她们的众女儿,以及你和你的众女儿必恢复起初的光景。 56-57在你骄傲的日子,你的恶行还没有被揭露的时候,你觉得妹妹所多玛不屑一提。但现在,你却成为以东的众女儿和她四邻非利士的众女儿的笑柄。你周围的人都鄙视你。 58你要承担淫荡和可憎行径带来的惩罚。这是耶和华说的。

59“‘主耶和华说,你背誓毁约,我必照你的所作所为报应你。 60然而,我顾念在你幼年时与你所立的约,我要与你立一个永远的约。 61你接纳你姊妹的时候,会想起自己的所作所为并自觉羞愧。我要将你姊妹赐给你作女儿,我这样做并不是出于我与你所立的约。 62我要和你立约,使你知道我是耶和华。 63我要赦免你所有的罪,那时你想起这事会羞愧难当,不敢再开口。这是主耶和华说的。’”