Ezekieli 15 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 15:1-8

Yerusalemu, Mtengo Wamphesa Wosabereka

1Yehova anayankhulanso nane kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse. 3Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo? 4Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse? 5Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?

6“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu. 7Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 8Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’ ”

New Russian Translation

Иезекииль 15:1-8

Иерусалим – бесполезное дерево

1Было ко мне слово Господа:

2– Сын человеческий, чем древесина виноградной лозы лучше древесины ветвей всех деревьев леса? 3Разве берут древесину виноградной лозы, чтобы сделать что-нибудь нужное? Разве делают из нее хотя бы колышки, чтобы развешивать вещи? 4А когда ее бросают в огонь как топливо, и огонь сжигает оба ее конца и обугливает середину, то годится ли она на что-нибудь? 5Если она ни на что не годилась, когда была целой, то на что же она сгодится после того, как ее поглотил огонь, и она обуглилась?

6Поэтому так говорит Владыка Господь:

– Как Я отдал древесину виноградной лозы среди деревьев леса на пожирание огню, так поступлю Я и с жителями Иерусалима. 7Я обращу лицо Мое против них. Даже если они выберутся из огня, огонь все равно поглотит их. И когда Я обращу против них лицо, вы узнаете, что Я – Господь. 8Я предам землю опустошению за то, что они нарушили верность, – возвещает Владыка Господь.