Ezekieli 15 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 15:1-8

Yerusalemu, Mtengo Wamphesa Wosabereka

1Yehova anayankhulanso nane kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse. 3Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo? 4Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse? 5Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?

6“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu. 7Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 8Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Ezequiel 15:1-8

Jerusalén, una vid inútil

1El Señor me habló diciendo: 2«Hijo de hombre, ¿en qué supera la madera de la vid a la madera de los árboles del bosque? 3Esa madera no sirve para hacer muebles, ¡y ni siquiera para hacer una percha! 4¡Escasamente sirve para alimentar el fuego! Pero ¿de qué sirve cuando sus extremos se consumen y ya se ha quemado por dentro? 5Si cuando estaba entera no servía para nada, ¡mucho menos cuando ya ha sido consumida por el fuego!

6»Por tanto, así dice el Señor omnipotente: Como el leño de la vid que eché al fuego, así haré con los habitantes de Jerusalén. 7Voy a enfrentarme a ellos; ¡se han librado de un fuego, pero serán consumidos por otro! Cuando me enfrente a ellos, vosotros sabréis que yo soy el Señor. 8Convertiré a este país en desolación, porque ha sido infiel. Lo afirma el Señor omnipotente».