Ezekieli 13 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 13:1-23

Mawu Odzudzula Aneneri Onyenga

1Yehova anayankhulanso nane kuti, 2“Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’ 3Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’ 4Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja. 5Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova. 6Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi. 7Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.

8“Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova. 9Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

10“Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza, 11choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho. 12Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’

13“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu. 14Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 15Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza. 16Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’

17“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule. 18Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu? 19Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.

20“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame. 21Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 22Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo, 23choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 13:1-23

斥責假先知

1耶和華對我說: 2「人子啊,你要說預言斥責以色列那些說預言的先知,告訴那些私自發預言的人,『你們要聽耶和華的話。 3主耶和華說,愚頑的先知有禍了!他們沒有看到異象,卻私自發預言。 4以色列人啊,你們的先知像廢墟中的狐狸, 5沒有上去堵住缺口,也沒有重建以色列的圍牆,使以色列在耶和華的日子來臨時的爭戰中堅立。 6他們的異象虛假不實,他們的預言謊話連篇。他們口口聲聲說是傳達耶和華的話,其實耶和華並沒有差遣他們。他們竟然指望自己的謊言能夠應驗。 7難道你們不是見了虛假的異象,說了虛謊的預言嗎?你們說這是耶和華說的,其實我並沒有說。』」

8所以主耶和華說:「因為你們的假異象和謊言,我要攻擊你們。這是主耶和華說的。 9我必動手攻擊那些見假異象、說假預言的先知。他們必從我的子民當中被剔除,不被收錄在以色列人的名冊上,也不能進入以色列的土地。這樣,你們就知道我是主耶和華。 10因為他們欺騙我的子民說,『平安!』其實並沒有平安,就像有人築了一道薄牆,用白灰加以粉飾。 11所以,你要警告那些粉刷白灰的人,說,『牆必倒塌,暴雨要來臨,冰雹勢必降下,狂風也必大作。』 12牆倒塌之後,一定會有人問,『你們粉飾的白灰在哪裡呢?』 13主耶和華說,『我必在烈怒中用狂風暴雨和冰雹來摧毀這牆, 14我必把你們粉飾的牆夷為平地,使其露出根基。牆倒塌的時候,你們必葬身其中。這樣,你們就知道我是耶和華。 15我要向這牆和粉飾這牆的人發怒,懲罰他們。我告訴你們,這牆完了!粉飾這牆的人也完了!』 16他們就是那些向耶路撒冷說假預言,在沒有平安的時候宣稱看到了平安異象的以色列先知。這是主耶和華說的。」

17「人子啊,你要說預言斥責你同胞中私自發預言的女子, 18告訴她們主耶和華這樣說,『你們這些婦女有禍了!你們為了獵取人命,給人縫製戴在手腕上的符咒和各種尺寸的頭巾。你們獵取我子民的性命,還想保住自己的性命嗎? 19你們為了幾把大麥和幾塊餅,在我的子民中褻瀆我,向那些肯聽謊言的說謊,殺死那些不該死的,救活那些不該活的。』

20「所以主耶和華說,『你們用符咒獵取人命如同捕鳥,我要除去你們的符咒,從你們手臂上扯掉它們,釋放你們所獵取的人。 21我還要撕去你們的頭巾,把我的子民從你們手中拯救出來,使他們不再做你們手中的獵物。這樣,你們就知道我是耶和華。 22我沒有使義人憂傷,你們卻以謊言叫他們灰心。你們慫恿惡人不要改邪歸正,以致他們喪命。 23因此,你們必不再見假異象,也不再占卜。我必從你們手中拯救我的子民。這樣,你們就知道我是耶和華。』」