Ezekieli 13 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 13:1-23

Mawu Odzudzula Aneneri Onyenga

1Yehova anayankhulanso nane kuti, 2“Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’ 3Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’ 4Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja. 5Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova. 6Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi. 7Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.

8“Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova. 9Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

10“Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza, 11choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho. 12Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’

13“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu. 14Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 15Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza. 16Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’

17“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule. 18Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu? 19Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.

20“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame. 21Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 22Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo, 23choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 13:1-23

Dommen over de falske profeter

1Herren sagde til mig:

2-3„Du menneske, profetér imod de falske profeter i Israel, som kommer med deres egne idéer og hævder, at deres budskaber er fra mig. Ve de tåbelige profeter, som siger: ‚Hør, hvad Herren siger!’ uden at jeg har talt til dem.

4-5Åh, Israels folk, jeres falske profeter er som sjakaler, der går på rov mellem ruinerne. De har intet gjort for at opbygge mit folk eller udbedre manglerne, så folket kunne undgå at blive ramt af min dom. 6De har løjet ved at påstå, at deres budskab kom fra mig, selv om jeg aldrig har sendt dem, så de kan ikke forvente, at jeg skal opfylde deres profetier. 7-8Derfor siger jeg til dem: ‚Er det måske ikke falske profetier og syner, der kommer fra jer, når I hævder at have et budskab fra mig, selvom jeg ikke har givet jer noget budskab? Fordi I er kommet med falske profetier og syner, må jeg straffe jer.’ 9De får aldrig nogen lederposition, ja, jeg vil slette deres navne af listen over Israels folk, og de vil aldrig få deres land at se igen. Så vil I indse, at jeg er Gud Herren. 10De fører mit folk på afveje ved at profetere om fred, når der ikke er fred. Mit folk har bygget en mur af løse sten, og profeterne påstår, et lag kalk kan holde sammen på den.

11Ezekiel, du kan godt fortælle dem, at deres fine, hvidkalkede mure vil falde sammen. Synden kan ikke skjules bag en pæn facade. Der kommer snart en mægtig storm med hagl og styrtregn, som får murene til at falde sammen. 12Når katastrofen indtræder, vil folket anklage de falske profeter for at have slået det hele hen i stedet for at advare dem om deres synd.

13Derfor siger jeg, Herren, til de falske profeter: Min vrede skal hagle ned over jer, og min harme er som en voldsom orkan, mit raseri er som den piskende regn. 14Jeg vil smadre den hvidkalkede mur, så den bryder sammen og knuser jer i faldet. Så vil I indse, at jeg er Herren. 15Jeg vil lade min vrede få frit løb imod muren og dem, som kalkede den. Så forsvinder både muren og de mennesker, som kalkede den, 16de profeter, som forkyndte fred og ingen fare for Jerusalem, når der i virkeligheden ikke var udsigt til fred.

17-18Profetér også imod de kvindelige profeter, der profeterer deres egne fantasier. Sig til dem: ‚Ve jer, der forfører mit folk, unge såvel som gamle, ved at lave amuletter, magiske armbånd til deres håndled og magiske tørklæder i alle størrelser. I vil blive straffet for at bedrage mit folk. 19I tager nogle håndfulde byg eller et par stykker brød som betaling for at spå dem. Derved fører I uskyldige folk i døden og holder hånden over andre, som i virkeligheden fortjente at dø. I lyver for mit folk, og de lytter med glæde til jeres løgne.

20Derfor siger jeg, Herren: Jeg vil straffe jer, fordi I jagter mit folks sjæle med jeres magiske armbånd. Jeg vil rive armbåndene af og sætte mit folk i frihed, som fuglen der slippes ud af sit bur. 21Jeg befrier mit folk for jeres magiske tørklæder og river dem ud af jeres kløer, så de ikke længere skal være ofre for jer. Så vil I indse, at jeg er Herren. 22I har taget modet fra de retskafne, stik imod min vilje, og I har opmuntret de onde, så de ikke omvendte sig fra deres ondskab og blev reddet. 23Men nu skal det være slut med jeres løgne og spådomskunster. Jeg river mit folk ud af jeres kløer, og så vil I indse, at jeg er Herren.’ ”