Ezekieli 12 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 12:1-28

Chifaniziro cha Otengedwa Ukapolo

1Yehova anayankhula nane kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.

3“Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu. 4Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo. 5Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako. 6Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”

7Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.

8Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati: 9“Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?

10“Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’ 11Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’

“Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”

12“Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita. 13Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko. 14Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.

15“Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena. 16Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”

17Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati, 18“Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako. 19Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo. 20Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

21Yehova anayankhulanso nane kuti, 22“Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’ 23Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi. 24Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli. 25Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’ ”

26Yehova anandiyankhula nati: 27“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’

28“Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’ ”

New International Version – UK

Ezekiel 12:1-28

The exile symbolised

1The word of the Lord came to me: 2‘Son of man, you are living among a rebellious people. They have eyes to see but do not see and ears to hear but do not hear, for they are a rebellious people.

3‘Therefore, son of man, pack your belongings for exile and in the daytime, as they watch, set out and go from where you are to another place. Perhaps they will understand, though they are a rebellious people. 4During the daytime, while they watch, bring out your belongings packed for exile. Then in the evening, while they are watching, go out like those who go into exile. 5While they watch, dig through the wall and take your belongings out through it. 6Put them on your shoulder as they are watching and carry them out at dusk. Cover your face so that you cannot see the land, for I have made you a sign to the Israelites.’

7So I did as I was commanded. During the day I brought out my things packed for exile. Then in the evening I dug through the wall with my hands. I took my belongings out at dusk, carrying them on my shoulders while they watched.

8In the morning the word of the Lord came to me: 9‘Son of man, did not the Israelites, that rebellious people, ask you, “What are you doing?”

10‘Say to them, “This is what the Sovereign Lord says: this prophecy concerns the prince in Jerusalem and all the Israelites who are there.” 11Say to them, “I am a sign to you.”

‘As I have done, so it will be done to them. They will go into exile as captives.

12‘The prince among them will put his things on his shoulder at dusk and leave, and a hole will be dug in the wall for him to go through. He will cover his face so that he cannot see the land. 13I will spread my net for him, and he will be caught in my snare; I will bring him to Babylonia, the land of the Chaldeans, but he will not see it, and there he will die. 14I will scatter to the winds all those around him – his staff and all his troops – and I will pursue them with drawn sword.

15‘They will know that I am the Lord, when I disperse them among the nations and scatter them through the countries. 16But I will spare a few of them from the sword, famine and plague, so that in the nations where they go they may acknowledge all their detestable practices. Then they will know that I am the Lord.’

17The word of the Lord came to me: 18‘Son of man, tremble as you eat your food, and shudder in fear as you drink your water. 19Say to the people of the land: “This is what the Sovereign Lord says about those living in Jerusalem and in the land of Israel: they will eat their food in anxiety and drink their water in despair, for their land will be stripped of everything in it because of the violence of all who live there. 20The inhabited towns will be laid waste and the land will be desolate. Then you will know that I am the Lord.” ’

There will be no delay

21The word of the Lord came to me: 22‘Son of man, what is this proverb you have in the land of Israel: “The days go by and every vision comes to nothing”? 23Say to them, “This is what the Sovereign Lord says: I am going to put an end to this proverb, and they will no longer quote it in Israel.” Say to them, “The days are near when every vision will be fulfilled. 24For there will be no more false visions or flattering divinations among the people of Israel. 25But I the Lord will speak what I will, and it shall be fulfilled without delay. For in your days, you rebellious people, I will fulfil whatever I say, declares the Sovereign Lord.” ’

26The word of the Lord came to me: 27‘Son of man, the Israelites are saying, “The vision he sees is for many years from now, and he prophesies about the distant future.”

28‘Therefore say to them, “This is what the Sovereign Lord says: none of my words will be delayed any longer; whatever I say will be fulfilled, declares the Sovereign Lord.” ’