Ezekieli 10 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 10:1-22

Ulemerero Uchoka ku mʼNyumba ya Mulungu

1Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro. 2Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.

3Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati. 4Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo. 5Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.

6Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi. 7Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka. 8Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.

9Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti. 10Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake. 11Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka. 12Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija. 13Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.” 14Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.

15Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. 16Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo. 17Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.

18Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi. 19Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.

20Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi. 21Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu. 22Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.

La Bible du Semeur

Ezéchiel 10:1-22

La gloire de l’Eternel quitte le Temple

1Je regardai et je vis dans l’étendue céleste qui s’étendait au-dessus de la tête des chérubins comme une pierre de saphir ; au-dessus de cette pierre, on apercevait quelque chose qui paraissait ressembler à un trône10.1 Voir 1.26.. 2Il dit à l’individu vêtu de lin : Passe entre les roues qui sont sous les chérubins et remplis tes mains des braises incandescentes qui se trouvent entre les chérubins, et répands-les sur la ville.

Il s’exécuta sous mes yeux10.2 Voir 1.13-21 ; cf. 2 R 25.8-9.. 3Or, les chérubins se tenaient à droite du Temple au moment où l’individu se rendit vers eux, et la nuée remplit le parvis intérieur. 4La gloire de l’Eternel s’était élevée de dessus le chérubin pour se diriger vers le seuil de la maison ; alors le Temple fut rempli par la nuée, et le parvis resplendit de l’éclat de la gloire de l’Eternel. 5Le bruissement des ailes des chérubins se fit entendre jusque dans le parvis extérieur. C’était comme la voix du Dieu tout-puissant quand il parle.

6Quand il avait ordonné à l’individu vêtu de lin : « Prends du feu entre les roues et entre les chérubins », l’individu y était allé et il se tenait à côté d’une roue. 7L’un des chérubins avança la main vers le feu qui était entre les chérubins. Il en retira des braises et les mit dans les mains de l’individu vêtu de lin. Celui-ci les prit et se retira. 8Alors apparut, sous les ailes des chérubins, une forme de main humaine.

9Je regardai et je vis quatre roues à côté des chérubins, une roue à côté de chacun d’eux. Elles avaient l’éclat de la chrysolithe. 10Toutes les quatre étaient pareilles et paraissaient imbriquées au milieu l’une de l’autre. 11Elles pouvaient donc se déplacer dans les quatre directions sans se tourner ; en effet, elles allaient du côté vers lequel se tournait la tête, sans pivoter dans leur mouvement. 12Tout le corps des chérubins, leurs dos et leurs mains, leurs ailes et les roues, étaient couverts d’yeux tout autour. Chacun des quatre avait sa roue. 13J’entendis qu’on donnait à ces roues le nom de tourbillon. 14Chacun des êtres vivants avait quatre faces. Les premières faces étaient des faces de chérubin, les deuxièmes des faces d’homme, les troisièmes des faces de lion et les quatrièmes des faces d’aigle.

15Les chérubins s’élevèrent : c’étaient les êtres vivants que j’avais vus sur les bords du canal du Kebar10.15 Voir 1.5 et note.. 16Quand les chérubins se déplaçaient, les roues se déplaçaient à côté d’eux, et quand ils déployaient leurs ailes pour s’élever au-dessus de la terre, les roues ne se détournaient pas d’eux, mais restaient à leurs côtés. 17Quand ils s’arrêtaient, elles s’arrêtaient, quand ils s’élevaient, elles s’élevaient avec eux, car l’Esprit qui animait les êtres vivants était aussi dans les roues.

18La gloire de l’Eternel quitta le seuil du Temple et vint se placer sur les chérubins. 19Ceux-ci déployèrent leurs ailes et s’élevèrent de terre sous mes yeux ; ils sortirent, et les roues sortirent avec eux. Ils s’arrêtèrent à l’entrée de la porte orientale du temple de l’Eternel et la gloire du Dieu d’Israël reposait sur eux tout au-dessus10.19 Voir 8.4 et note.. 20C’étaient les êtres vivants que j’avais vus au-dessous du Dieu d’Israël près du canal du Kebar, et je reconnus que c’étaient des chérubins. 21Chacun d’eux avait quatre faces et quatre ailes, sous lesquelles apparaissaient ce qui était comme des mains humaines. 22Leurs faces avaient la même apparence que celles que j’avais vues près du canal du Kebar, elles avaient le même aspect ; c’étaient bien eux. Chacun des êtres avançait droit devant lui.