Ezekieli 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 1:1-28

Zolengedwa za Moyo ndi Ulemerero wa Yehova

1Tsiku lachisanu la mwezi wachinayi, chaka cha makumi atatu, ine ndinali pakati pa amʼndende mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara. Tsono kumwamba kunatsekuka ndipo ndinaona maonekedwe a Mulungu mʼmasomphenya.

2Pa tsiku lachisanu la mwezi, chaka chachisanu Yehoyakini ali mʼndende, 3Yehova anayankhula ndi wansembe Ezekieli, mwana wa Buzi, mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara mʼdziko la Ababuloni. Dzanja la Yehova linali pa iye kumeneko.

4Ndinayangʼana ndipo ndinangoona mphepo yamkuntho ikubwera kuchokera kumpoto. Panali mtambo waukulu wozunguliridwa ndi kuwala ndipo moto unali lawilawi kuchokera mu mtambowo. Pakati pa motowo pankaoneka ngati mkuwa wonyezimira. 5Mʼkatikati mwa motowo munali zinthu zinayi zamaonekedwe a nyama. Thupi lawo limaoneka ngati la munthu 6koma chilichonse chinali ndi nkhope zinayi ndiponso mapiko anayi. 7Miyendo yake inali yowongoka; mapazi ake anali a ziboda ngati phazi la mwana wangʼombe. Ndipo zibodazo zinkawala ngati mkuwa wonyezimira. 8Mʼmunsi mwa mapiko awo kumbali zonse zinayi, nyamazo zinali ndi manja a munthu. Zonse zinayi zinali ndi nkhope ndi mapiko, 9ndipo mapiko awowo anakhudzana. Chilichonse chimapita molunjika kutsogolo; sizimatembenuka pamene zimayenda.

10Nkhope zawo zimaoneka motere: Chilichonse chinali ndi nkhope ya munthu, ndipo mbali ya kumanja chilichonse chinali ndi nkhope zinayi zosiyana motere: nkhope ya munthu, nkhope ya mkango ku dzanja lamanja, nkhope ya ngʼombe ku dzanja lamanzere, ndipo kumbuyo kwake nkhope ya chiwombankhanga. 11Ndi mʼmene zinalili nkhope zawo. Mapiko awo anali otambasukira mmwamba. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko awiri okhudzana ndi mapiko a chinzake. Chinalinso ndi mapiko ena awiri ophimbira thupi lake. 12Zamoyozo zinkayenda molunjika kutsogolo. Kulikonse kumene mzimu umazitsogolera kupita, nazonso zimapita kumeneko, osatembenuka pamene zikupita. 13Pakati pa zamayozo panali chinthu chooneka ngati makala oyaka kapena miyuni yoyaka. Moto umayendayenda pakati pa zamayozo; wowala kwambiri, ndipo mphenzi zimatuluka pakati pawo. 14Zamoyozo zinkathamanga uku ndi uko ngati kungʼanima kwa mphenzi.

15Pamene ndinali kuyangʼana zamoyozo, ndinangoona mikombero ndipo pansi pambali pa chamoyo chilichonse panali mkombero umodzi. 16Maonekedwe a mikomberoyo anali ngati mwala wonyezimira. Mikombero yonse inali yofanana ndipo mapangidwe awo anali ngati wongolowanalowana. 17Mikombero ija poyenda inkatha kupita mbali iliyonse yomwe zamoyozo zinayangʼana popanda kutembenuka. 18Marimu a mikomberoyo anali aatali ndi ochititsa mantha ndipo marimu onse anayi anali ndi maso ponseponse.

19Zamoyozo zinkati zikamayenda, mikomberoyo imayendanso mʼmbali mwake; ndipo zamoyozo zinkati zikamakwera mmwamba, mikomberoyo imakweranso. 20Kulikonse kumene mzimu wake unkazitsogolera, zamoyozo zinkapita komweko. Ndipo mikombero ija inkapita nawo pamodzi popeza kuti mzimu wa zamoyozo ndiwo umayendetsa mikombero ija. 21Zamoyo zija zinkati zikamayenda mikombero imayendanso. Zamoyozo zimati zikayima, nayonso mikombero inkayima. Zamoyozo zinkati zikawuluka, mikomberonso imawuluka nazo pamodzi chifukwa mzimu wa zamoyo zija ndiwo umayendetsa mikombero ija.

22Pamwamba pa mitu ya zamoyozo panali chinthu chonga thambo, lowala ndipo kunyezimira kwake ngati galasi loyangʼanitsa ku dzuwa, loyalidwa pamwamba pa mitu yake. 23Zamoyozo zinatambalitsa mapiko ake mʼmunsi mwa thambo lija, mapiko ake ena kumakhudzana, mapiko awiri kumaphimba thupi lake. 24Pamene zamoyo zimayenda ndimamva phokoso la mapiko ake, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati liwu la Wamphamvuzonse, ngati phokoso la gulu lankhondo. Zimati zikayima zinkagwetsa mapiko ake.

25Ndipo panamveka mawu kuchokera pamwamba pa thambo la pa mitu ya zamoyo zija. Nthawi iyi nʼkuti zamoyozo zitayima ndi kugwetsa pansi mapiko ake. 26Pamwamba pa thambo la pa mitu yake panali chinthu chimene chimaoneka ngati mpando waufumu wopangidwa ndi mwala wa safiro, ndipo pamwamba pa mpando waufumuwo panali chinthu chooneka ngati munthu. 27Ndinaona kuti mmwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo chowala konsekonse ngati moto. Mʼmunsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokha. Kuwala kwa mphamvu kunamuzungulira munthuyo. 28Kuwalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza mʼmitambo tsiku limene kwagwa mvula.

Umu ndi mmene ulemerero wa Yehova umaonekera. Pamene ndinawuona ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akundiyankhula.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 1:1-28

以西結的異象

1第三十年四月五日,我正在迦巴魯河畔被擄的人當中,忽然天開了,我看見了上帝的異象。 2那是約雅斤王被擄第五年的四月五日, 3就在迦勒底人境內的迦巴魯河畔,耶和華的話特別傳給了布西的兒子以西結祭司,耶和華的能力1·3 能力」希伯來文是「手」。降在他身上。

4在異象中,我看見一陣狂風從北方颳來,隨後有一大朵雲閃耀著火光,四周環繞著燦爛的光芒,火的中心像發光的金屬。 5火中有四個像人形的活物, 6每個活物有四張不同的面孔和四個翅膀。 7他們的腿是直的,腳如同牛犢的蹄,都亮如磨光的銅。 8四面的翅膀下都有人的手,四個活物都有臉和翅膀, 9翅膀彼此相連。他們移動時不必轉身,各朝前面移動。 10四個活物的面孔是這樣的:正面是人的臉,右面是獅子的臉,左面是牛的臉,後面是鷹的臉。 11他們的翅膀向上展開,每個活物的一對翅膀與其他活物的翅膀相連,另外一對翅膀遮蔽身體。 12耶和華的靈往哪裡去,他們也往哪裡去,移動時不用轉身。 13四個活物的形像如燃燒的火炭,又像火把。活物之間有火上下移動,發出耀眼的閃電。 14這些活物像閃電一樣往來飛馳。

15當我觀看這些活物的時候,發現每個活物旁邊的地上都有一個輪子。 16四個輪子的形狀和結構都一樣,好像輪套輪,如同閃耀的綠寶石。 17他們可以向四面移動,移動時輪子不必轉向。 18輪圈高而可畏,周圍佈滿了眼睛。 19活物行走,輪子也在旁邊行走;活物上升,輪子也上升。 20靈往哪裡去,活物也往哪裡去,輪子也跟著往哪裡去,因為活物的靈在輪子裡。 21活物行走,輪子也行走;活物站立不動,輪子也站立不動;活物上升,輪子也跟著上升,因為活物的靈在輪子裡。

22活物的頭上好像鋪展著茫茫的穹蒼,如同頂著耀眼的水晶。 23穹蒼下四個活物伸展翅膀,彼此相對,各用兩個翅膀遮蔽身體。 24他們移動時,翅膀發出的響聲如洪濤之聲,既像全能者的聲音,又像軍隊的呐喊。活物站住的時候,便將翅膀垂下。 25他們站立垂下翅膀時,有聲音從他們頭頂的穹蒼之上傳來。

26在他們頭頂的穹蒼之上彷彿有藍寶石的寶座,有一位形狀像人的高高坐在寶座上。 27我看到祂的腰部以上好像燒紅發亮的金屬,好像有火四面環繞。腰部以下如同火焰。祂周圍有耀眼的光輝, 28彷彿雨天雲中的彩虹。

這是耶和華榮耀的形像。我一看見,便俯伏在地,隨後聽見有說話的聲音。