Ezekieli 1 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 1:1-28

Zolengedwa za Moyo ndi Ulemerero wa Yehova

1Tsiku lachisanu la mwezi wachinayi, chaka cha makumi atatu, ine ndinali pakati pa amʼndende mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara. Tsono kumwamba kunatsekuka ndipo ndinaona maonekedwe a Mulungu mʼmasomphenya.

2Pa tsiku lachisanu la mwezi, chaka chachisanu Yehoyakini ali mʼndende, 3Yehova anayankhula ndi wansembe Ezekieli, mwana wa Buzi, mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara mʼdziko la Ababuloni. Dzanja la Yehova linali pa iye kumeneko.

4Ndinayangʼana ndipo ndinangoona mphepo yamkuntho ikubwera kuchokera kumpoto. Panali mtambo waukulu wozunguliridwa ndi kuwala ndipo moto unali lawilawi kuchokera mu mtambowo. Pakati pa motowo pankaoneka ngati mkuwa wonyezimira. 5Mʼkatikati mwa motowo munali zinthu zinayi zamaonekedwe a nyama. Thupi lawo limaoneka ngati la munthu 6koma chilichonse chinali ndi nkhope zinayi ndiponso mapiko anayi. 7Miyendo yake inali yowongoka; mapazi ake anali a ziboda ngati phazi la mwana wangʼombe. Ndipo zibodazo zinkawala ngati mkuwa wonyezimira. 8Mʼmunsi mwa mapiko awo kumbali zonse zinayi, nyamazo zinali ndi manja a munthu. Zonse zinayi zinali ndi nkhope ndi mapiko, 9ndipo mapiko awowo anakhudzana. Chilichonse chimapita molunjika kutsogolo; sizimatembenuka pamene zimayenda.

10Nkhope zawo zimaoneka motere: Chilichonse chinali ndi nkhope ya munthu, ndipo mbali ya kumanja chilichonse chinali ndi nkhope zinayi zosiyana motere: nkhope ya munthu, nkhope ya mkango ku dzanja lamanja, nkhope ya ngʼombe ku dzanja lamanzere, ndipo kumbuyo kwake nkhope ya chiwombankhanga. 11Ndi mʼmene zinalili nkhope zawo. Mapiko awo anali otambasukira mmwamba. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko awiri okhudzana ndi mapiko a chinzake. Chinalinso ndi mapiko ena awiri ophimbira thupi lake. 12Zamoyozo zinkayenda molunjika kutsogolo. Kulikonse kumene mzimu umazitsogolera kupita, nazonso zimapita kumeneko, osatembenuka pamene zikupita. 13Pakati pa zamayozo panali chinthu chooneka ngati makala oyaka kapena miyuni yoyaka. Moto umayendayenda pakati pa zamayozo; wowala kwambiri, ndipo mphenzi zimatuluka pakati pawo. 14Zamoyozo zinkathamanga uku ndi uko ngati kungʼanima kwa mphenzi.

15Pamene ndinali kuyangʼana zamoyozo, ndinangoona mikombero ndipo pansi pambali pa chamoyo chilichonse panali mkombero umodzi. 16Maonekedwe a mikomberoyo anali ngati mwala wonyezimira. Mikombero yonse inali yofanana ndipo mapangidwe awo anali ngati wongolowanalowana. 17Mikombero ija poyenda inkatha kupita mbali iliyonse yomwe zamoyozo zinayangʼana popanda kutembenuka. 18Marimu a mikomberoyo anali aatali ndi ochititsa mantha ndipo marimu onse anayi anali ndi maso ponseponse.

19Zamoyozo zinkati zikamayenda, mikomberoyo imayendanso mʼmbali mwake; ndipo zamoyozo zinkati zikamakwera mmwamba, mikomberoyo imakweranso. 20Kulikonse kumene mzimu wake unkazitsogolera, zamoyozo zinkapita komweko. Ndipo mikombero ija inkapita nawo pamodzi popeza kuti mzimu wa zamoyozo ndiwo umayendetsa mikombero ija. 21Zamoyo zija zinkati zikamayenda mikombero imayendanso. Zamoyozo zimati zikayima, nayonso mikombero inkayima. Zamoyozo zinkati zikawuluka, mikomberonso imawuluka nazo pamodzi chifukwa mzimu wa zamoyo zija ndiwo umayendetsa mikombero ija.

22Pamwamba pa mitu ya zamoyozo panali chinthu chonga thambo, lowala ndipo kunyezimira kwake ngati galasi loyangʼanitsa ku dzuwa, loyalidwa pamwamba pa mitu yake. 23Zamoyozo zinatambalitsa mapiko ake mʼmunsi mwa thambo lija, mapiko ake ena kumakhudzana, mapiko awiri kumaphimba thupi lake. 24Pamene zamoyo zimayenda ndimamva phokoso la mapiko ake, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati liwu la Wamphamvuzonse, ngati phokoso la gulu lankhondo. Zimati zikayima zinkagwetsa mapiko ake.

25Ndipo panamveka mawu kuchokera pamwamba pa thambo la pa mitu ya zamoyo zija. Nthawi iyi nʼkuti zamoyozo zitayima ndi kugwetsa pansi mapiko ake. 26Pamwamba pa thambo la pa mitu yake panali chinthu chimene chimaoneka ngati mpando waufumu wopangidwa ndi mwala wa safiro, ndipo pamwamba pa mpando waufumuwo panali chinthu chooneka ngati munthu. 27Ndinaona kuti mmwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo chowala konsekonse ngati moto. Mʼmunsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokha. Kuwala kwa mphamvu kunamuzungulira munthuyo. 28Kuwalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza mʼmitambo tsiku limene kwagwa mvula.

Umu ndi mmene ulemerero wa Yehova umaonekera. Pamene ndinawuona ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akundiyankhula.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Езекиил 1:1-28

Видение славы Вечного

1На тридцатом году моей жизни, в пятый день четвёртого месяца, когда я жил среди пленников у реки Кевар в Вавилоне, небеса раскрылись, и мне было видение от Аллаха. 2В тот день (шёл пятый год плена царя Иехонии)1:2 Иехония правил Иудеей всего лишь три месяца и был уведён в плен в Вавилонию в 597 г. до н. э. (см. 4 Цар. 24:8-17; 2 Лет. 36:9-10). (31 июля 593 г. до н. э.) 3слово Вечного1:3 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь. было ко мне, священнослужителю Езекиилу, сыну Бузи1:3 Или: «ко мне, Езекиилу, сыну священнослужителя Бузи»., у реки Кевар в стране вавилонян, и там на мне была рука Вечного.

4Я смотрел и видел смерч, который надвигался с севера: огромное облако со сверкающими молниями, окружённое сиянием. Посреди огня было нечто, подобное сияющему металлу. 5В огне были подобия четырёх живых существ. Обличием они походили на людей, 6но у каждого из них было по четыре лица и четыре крыла. 7Ноги у них были прямыми, а ступни ног походили на копыта телёнка и сверкали, как блестящая латунь. 8Под крыльями на четырёх их сторонах у них были человеческие руки. 9Все они имели лица и крылья, и крылья их соприкасались одно с другим. Каждое из них двигалось лицом вперёд; при движении они не оборачивались. 10Лица у них были такими: у каждого из четырёх спереди было человеческое лицо, с правой стороны у каждого было лицо льва, с левой стороны – лицо вола, а сзади у каждого из них было лицо орла. 11Такими были их лица. Крылья у них были простёрты вверх; у каждого существа было по две пары крыльев: одна пара касалась крыльев других существ по обеим сторонам, а другая пара закрывала тело. 12Каждое из них шло лицом вперёд. Куда бы ни шёл Дух, шли и они, не оборачиваясь на ходу. 13Облик живых существ был подобен горящим углям, подобен факелам. Огонь непрестанно перемещался посреди существ; он пламенел, и из него вырывалась молния. 14Существа быстро передвигались вперёд и назад, подобно тому, как сверкает молния.

15Я смотрел на живых существ и видел на земле возле них колёса, по одному на каждого из четырёх. 16Колёса выглядели следующим образом: они искрились, подобно хризолиту, и все четыре колеса были одинаковыми на вид. Они выглядели так, словно колесо находилось в колесе. 17Двигаясь, они могли направляться в любую из четырёх сторон, куда были обращены существа; когда существа передвигались, колёса не поворачивались. 18Их ободья были высокими и устрашающими; по всему кругу ободьев всех четырёх колёс располагались глаза.

19Когда живые существа двигались, двигались и колёса, располагавшиеся возле них; когда существа поднимались с земли, поднимались и колёса. 20Куда бы ни шёл дух, шли и они; колёса поднимались с ними, потому что дух живых существ был в колёсах. 21Когда существа двигались, они тоже двигались; когда существа стояли, они тоже стояли, а когда существа поднимались с земли, колёса поднимались вместе с ними, потому что дух живых существ был в колёсах.

22Над головами живых существ было нечто, подобное своду, оно изумительно искрилось, подобно кристаллу; и этот свод был распростёрт над их головами. 23Под сводом крылья существ были простёрты одно к другому, и каждый из них имел по два крыла, закрывавших тело. 24Когда существа двигались, я слышал шум от их крыльев, который был подобен рёву могучих вод, подобен голосу Всемогущего или боевому кличу в воинском стане. Останавливаясь, существа опускали крылья.

25И из-за свода над их головами раздавался голос; останавливаясь, они опускали крылья. 26Над сводом, который был над их головами, было нечто, подобное престолу из сапфира, а над подобием престола, сверху, восседал Некто, похожий на человека. 27Я видел, что от пояса и выше Он был похож на сияющий металл, словно бы исполненный пламени, а ниже пояса Он был похож на огонь; Его окружало сияние. 28Сияние вокруг Него было подобно радуге в облаках в дождливый день.