Ezara 8 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezara 8:1-36

Mʼndandanda wa Akuluakulu a Mabanja Amene Anabwera ndi Ezara

1Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:

2Geresomu wa fuko la Finehasi;

Danieli wa fuko la Itamara;

Hatusi 3mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide;

Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;

4Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.

5Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.

6Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.

7Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.

8Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.

9Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.

10Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.

11Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.

12Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.

13Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.

14Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.

Kubwerera ku Yerusalemu

15Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi. 16Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani, 17ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu. 18Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18. 19Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri. 20Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.

21Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense. 22Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.” 23Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.

24Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi 25ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka. 26Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide, 27mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.

28Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu. 29Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.” 30Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.

31Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira. 32Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.

33Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi. 34Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.

35Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova. 36Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.

Священное Писание

Узайр 8:1-36

Список глав семей вернувшихся с Узайром

1Вот главы семейств и родословия тех, кто вышел со мной из Вавилона во время правления царя Артаксеркса:

2из потомков Пинхаса – Гершом;

из потомков Итамара – Даниял;

из потомков Давуда – Хаттуш, 3сын Шехании;

из потомков Пароша – Закария, и с ним по родословному списку было 150 мужчин;

4из потомков Пахат-Моава – Элиегоенай, сын Зерахии, и с ним 200 мужчин;

5из потомков Затту – Шехания, сын Иахазиила, и с ним 300 мужчин;

6из потомков Адина – Эвед, сын Ионафана, и с ним 50 мужчин;

7из потомков Елама – Иешая, сын Аталии, и с ним 70 мужчин;

8из потомков Шефатии – Зевадия, сын Микаила, и с ним 80 мужчин;

9из потомков Иоава – Авдий, сын Иехиила, и с ним 218 мужчин;

10из потомков Бани – Шеломит, сын Иосифия, и с ним 160 мужчин;

11из потомков Бевая – Закария, сын Бевая, и с ним 28 мужчин;

12из потомков Азгада – Иоханан, сын Аккатана, и с ним 110 мужчин;

13из потомков Адоникама – последние, чьи имена Элифелет, Иеуил и Шемая, и с ними 60 мужчин;

14из потомков Бигвая – Утай и Заккур, и с ними 70 мужчин.

Узайр призывает левитов и храмовых слуг к возвращению

15Я собрал их у реки, которая течёт в сторону Ахавы, где мы разбили лагерь и провели там три дня. Когда я осмотрел народ и священнослужителей, то не нашёл среди них ни одного левита. 16Тогда я позвал Элиезера, Ариила, Шемаю, Элнафана, Иарива, Элнафана, Нафана, Закарию и Мешуллама, которые были вождями, и учёных – Иоярива и Элнафана, 17и отправил их к Иддо, вождю в Касифии. Я велел им передать Иддо и его родственникам, храмовым слугам в Касифии, чтобы они привели к нам служителей для дома нашего Бога. 18Так как милостивая рука нашего Бога была над нами, они привели к нам Шеревию, способного человека из потомков Махли, сына Леви, сына Исраила, и сыновей и братьев Шеревии – восемнадцать мужчин; 19и Хашавию вместе с Иешаей из потомков Мерари, и его братьев и племянников – двадцать мужчин. 20Они также привели двести двадцать храмовых слуг – группу служителей, которых Давуд и чиновники отдали в помощь левитам. Все они были записаны поимённо.

Подготовка к пути

21Там, у реки Ахавы, я объявил пост, чтобы мы могли смирить себя перед нашим Богом и попросить Его о безопасном путешествии для нас и наших детей со всем нашим имуществом. 22Мне было стыдно просить у царя войска и всадников для нашей защиты от врагов в пути, потому что мы уже сказали царю: «Милостивая рука нашего Бога на каждом, кто ищет Его, но Его великий гнев на всех, кто покидает Его». 23Итак, мы постились и просили нашего Бога об этом, и Он ответил на нашу молитву.

24Затем я отделил двенадцать главных священнослужителей: Шеревию вместе с Хашавией и десять других из их братьев, 25и, взвесив, я отдал им пожертвованное серебро, и золото, и предметы, которые царь, его советники, его чиновники и все находившиеся там исраильтяне отдали для дома нашего Бога. 26Взвесив, я отдал им 23 400 килограммов серебра, серебряных предметов весом в 3 600 килограммов, золота – 3 600 килограммов8:26 Букв.: «650… 100… 100 талантов»., 2720 золотых чаш стоимостью в 1 000 золотых монет8:27 Букв.: «1 000 дариков». Золотые чаши весили 8,5 кг. и два сосуда из лучшей блестящей латуни, ценимой как золото.

28И я сказал им:

– Вы, так же как и все эти предметы, посвящены Вечному. Серебро и золото – добровольные пожертвования Вечному, Богу ваших предков. 29Бережно храните всё это до тех пор, пока не передадите в хранилище дома Вечного в Иерусалиме, взвесив всё на глазах у главных священнослужителей, левитов и глав семейств Исраила.

30Затем священнослужители и левиты приняли серебро, золото и священные предметы, которые были отданы для того, чтобы их отвезли в дом нашего Бога в Иерусалиме.

Возвращение в Иерусалим

31В двенадцатый день первого месяца (19 апреля 458 г. до н. э.) мы отправились в путь от реки Ахавы, чтобы дойти до Иерусалима. Рука нашего Бога была над нами, и Он защитил нас от врагов и разбойников в пути. 32Итак, мы пришли в Иерусалим, где отдыхали три дня.

33На четвёртый день в доме нашего Бога мы, взвесив серебро, золото и священные предметы, передали их в руки священнослужителя Меремота, сына Урии. С ним был Элеазар, сын Пинхаса, а также левиты – Иозавад, сын Иешуа, и Ноадия, сын Биннуи. 34Всё было сосчитано по количеству и весу, и в то же время был записан общий вес.

35Затем пришедшие из плена переселенцы принесли жертвы всесожжения Богу Исраила – двенадцать быков за весь Исраил, девяносто шесть баранов, семьдесят семь ягнят мужского пола и двенадцать козлов в жертву за грех. Всё это было принесено в жертву всесожжения Вечному. 36Они также отдали царские приказы царским сатрапам8:36 Персидская империя была поделена на административные области (сатрапии), которыми управляли сатрапы – самый высокий ранг чиновников в империи. Сатрапии, в свою очередь, состояли из отдельных провинций. и наместникам провинции за Евфратом, которые потом оказали поддержку народу и дому Всевышнего.