Ezara 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezara 3:1-13

Kumangidwanso kwa Guwa la Nsembe

1Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi. 2Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja. 3Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo. 4Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa. 5Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova. 6Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.

Kumangidwanso kwa Nyumba ya Mulungu

7Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.

8Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova. 9Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.

10Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli. 11Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi:

“Yehova ndi wabwino;

chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.”

Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa. 12Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala. 13Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.

New Russian Translation

Ездра 3:1-13

Восстановление жертвенника

1Когда наступил седьмой месяц и израильтяне уже поселились в своих городах, народ, как один человек, собрался в Иерусалиме. 2Иисус, сын Иоседека, вместе со своими собратьями священниками, Зоровавелем, сыном Шеалтиила, и его собратьями начал строить жертвенник Бога Израиля, чтобы приносить на нем всесожжения, как предписано в Законе Божьего человека Моисея. 3Несмотря на то что3:3 Несмотря на то, что – или: «Так как». они боялись народов, которые были вокруг них, они построили жертвенник на прежнем основании и приносили на нем всесожжения Господу – и утренние, и вечерние жертвы. 4Затем они отпраздновали, как предписано, праздник Шалашей3:4 Праздник Шалашей – иудейский праздник в память о попечении Бога во время скитаний в пустыне (см. Лев. 23:33-43; Чис. 29:12-39; Втор. 16:13-17). с указанным количеством всесожжений, установленных для каждого дня. 5После этого они принесли постоянные всесожжения, жертвы на Новолуние3:5 Праздник появления каждой новой луны, означавшей (в системе времяисчисления, построенной на лунном календаре) начало нового месяца., и жертвы на все праздники, посвященные Господу, и добровольные пожертвования от каждого, кто добровольно жертвовал Господу. 6В первый день седьмого месяца они начали приносить Господу всесожжения, хотя основание Господнего храма еще не было заложено.

Закладка основания для храма

7Они начали давать деньги каменщикам и плотникам и еду, питье и масло жителям Сидона и Тира, чтобы те привозили морем кедровые бревна с Ливана в Яффу с разрешения Кира, царя Персии.

8Во второй месяц второго года после того, как они пришли к Божьему дому в Иерусалиме3:8 В середине весны 536 г. до н. э., Зоровавель, сын Шеалтиила, Иисус, сын Иоседека, и все остальные их соплеменники (священники, левиты и все, кто вернулся в Иерусалим из плена) приступили к работе, назначив левитов от двадцати лет и старше следить за строительством дома Господа. 9Иисус со своими сыновьями и братьями, и Кадмиил со своими сыновьями (потомками Годавии3:9 Букв.: «Иуды». Иуда – вариант имени Годавия (см. 2:40; Неем. 7:43).), и сыновья Хенадада со своими сыновьями и братьями – все левиты – вместе начали следить за строительством Божьего дома.

10Когда строители заложили основание дома Господа, священники в своих облачениях и с трубами и левиты (сыновья Асафа) с тарелками заняли свои места, чтобы восславить Господа по наставлениям Давида, царя Израиля. 11Они пели попеременно, возвеличивая и благодаря Господа:

– Он благ;

милость Его к Израилю – навеки!

А весь народ отвечал громким криком хвалы Господу, потому что основание дома Господа было заложено. 12Но многие из старых священников, левитов и глав семейств, видевших прежний дом, громко плакали, глядя, как закладывается основание этого дома, а многие кричали от радости. 13Крики радости нельзя было отличить от плача – так шумел народ. И шум был слышен далеко.