Ezara 10 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezara 10:1-44

Anthu Avomereza Tchimo Lawo

1Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri. 2Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli. 3Tsopano tiyeni tichite naye pangano Mulungu wathu, kuti tichotse akazi onsewa ndi ana awo, potsata malangizo a inu mbuye wanga ndi wa anthu amene amaopa malamulo a Mulungu wathu. Lolani kuti zichitike motsatira malamulo. 4Tsono dzukani, imeneyi ndi ntchito yanu. Ife tikuthandizani. Limbani mtima ndipo gwirani ntchitoyi.”

5Choncho Ezara anayimirira ndipo analumbiritsa akulu a ansembe, Alevi ndi Aisraeli onse, kuti adzachitedi monga Sekaniya ananenera. Tsono onse analumbira. 6Ezara anachoka ku Nyumba ya Mulungu napita ku chipinda cha Yehohanani, mwana wa Eliyasibu. Anatandala kumeneko usiku wonse ndipo sanadye chakudya kapena kumwa madzi popeza ankalira chifukwa cha kusankhulupirika kwa anthu obwera ku ukapolo.

7Tsono anthu analengeza mʼdziko lonse la Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Yerusalemu kwa onse ochokera ku ukapolo aja kuti asonkhane ku Yerusalemu. 8Ananena kuti wina aliyense amene saonekera pakutha pa masiku atatu, adzalandidwa katundu wake, potsata malangizo a nduna ndi akuluakulu, ndipo adzachotsedwa mʼgulu la anthu obwerako ku ukapolo.

9Choncho anthu onse a mʼdziko la Yuda ndi a mʼdziko la Benjamini anasonkhana ku Yerusalemu asanathe masiku atatu. Limeneli linali tsiku la 20 la mwezi wa 9. Anthu onse anakhala pansi pa bwalo la Nyumba ya Mulungu akunjenjemera chifukwa cha mvula yambiri imene inagwa. 10Ndipo wansembe Ezara anayimirira nawuza anthuwo kuti, “Inu mwachimwa pomakwatira akazi achikunja ndi kumawonjezera pa tchimo la Aisraeli. 11Tsopano lapani kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu ndi kuchita zimene akufuna. Dzipatuleni kwa anthu a mayiko enawa ndi kwa akazi achikunjawa.”

12Gulu lonse la anthu linayankha ndi mawu ofuwula kuti, “Nʼzoona! Tichita monga mwaneneramu. 13Koma pano pali anthu ambiri ndiponso mvula ikugwa kwambiri, choncho sitingakayime panja. Ndiponso ntchitoyi si ya tsiku limodzi kapena awiri, chifukwa tachimwa kwambiri pa zimene tachitazi. 14Tsono mulole kuti atsogoleri athu ayimirire mʼmalo mwa anthu onse. Aliyense wa mʼmizinda yathu amene anakwatira mkazi wachikunja abwere pa nthawi imene inu munene, ndipo abwere pamodzi ndi akuluakulu ndi oweruza a mzindawo. Choncho mkwiyo wa Mulungu wathu udzatichoka.” 15Koma Yonatani yekha mwana wa Asaheli ndi Yahazieli mwana wa Tikiva ndiwo anatsutsapo pa zimenezi. Tsono Mesulamu ndi Mlevi Sebetai anawayikira kumbuyo.

16Choncho anthu obwerako ku ukapolo aja anachita zimene zimafunika. Ndipo wansembe Ezara anasankha amuna amene anali atsogoleri a mabanja potsata mafuko awo ndipo onsewo analembedwa mayina awo. Tsiku loyamba la mwezi wa khumi anayambapo kuyifufuza nkhani imeneyi. 17Ndipo pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba anali atathana nawo anthu amene anakwatira akazi achilendo aja.

Okwatira Akazi Achilendo

18Nawu mʼndandanda wa ansembe amene anakwatira akazi achikunja:

Pa banja la Yesuwa ndi abale ake, ana a Yozadaki, panali awa: Maaseiya, Eliezara, Yaribu ndi Gedaliya. 19Iwo anatsimikiza zochotsa akazi awo ndipo chifukwa cha kulakwa kwawo aliyense anapereka nkhosa yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.

20Pa banja la Imeri panali awa:

Hanani ndi Zebadiya.

21Pa banja la Harimu panali awa:

Maseya, Eliya, Semaya, Yehieli ndi Uziya.

22Pa banja la Pasuri panali awa:

Eliyoenai, Maseya, Ismaeli, Netaneli, Yozabadi ndi Eleasa.

23Pakati pa Alevi panali:

Yozabadi, Simei, Kelaya (ndiye kuti, Kelita). Petaya, Yuda ndi Eliezara.

24Pakati pa oyimba nyimbo panali

Eliyasibu.

Ochokera kwa alonda a zipata:

Salumu, Telemu ndi Uri.

25Ochokera pakati pa Aisraeli ena:

a fuko la Parosi anali

Ramiya, Iziya, Malikiya, Miyamini, Eliezara, ndi Benaya.

26A fuko la Elamu anali

Mataniya, Zekariya, Yehieli, Abidi, Yeremoti ndi Eliya.

27A fuko la Zatu anali

Eliyoenai, Eliyasibu, Mataniya, Yeremoti, Zabadi ndi Aziza.

28A fuko la Bebai anali

Yehohanani, Hananiya, Zabayi ndi Atilayi.

29A fuko la Bani anali

Mesulamu, Maluki, Adaya, Yasubu, Seali ndi Yeremoti.

30A fuko la Pahati-Mowabu anali

Adina, Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, Binuyi ndi Manase.

31A fuko la Harimu anali

Eliezara, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni, 32Benjamini, Maluki ndi Semariya.

33A fuko la Hasumu anali

Mataneyi, Matata, Zabadi, Elifeleti, Yeremayi, Manase ndi Simei.

34A fuko la Bani anali

Madai, Amramu, Uweli, 35Benaya, Bediya, Keluhi, 36Vaniya, Meremoti, Eliyasibu, 37Mataniya, Matenayi ndi Yasu.

38A fuko la Binuyi anali

Simei, 39Selemiya, Natani, Adaya, 40Makinadebayi, Sasai, Sarai, 41Azaleli, Selemiya, Semariya, 42Salumu, Amariya ndi Yosefe.

43A fuko la Nebo anali

Yeiyeli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Yadai, Yoweli ndi Benaya.

44Onsewa anakwatira akazi achilendo. Tsono anawasudzula akaziwo ndi kuwatumiza kwawo pamodzi ndi ana awo.