Estere 6 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 6:1-14

Mordekai Apatsidwa Ulemu

1Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere. 2Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.

3Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?”

Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”

4Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.

5Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.”

“Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.

6Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?”

Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?” 7Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi: 8Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake. 9Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’ ”

10Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”

11Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”

12Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake. 13Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira.

Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.” 14Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.

Bibelen på hverdagsdansk

Esters Bog 6:1-14

Hamans plan går i vasken

1Den nat kunne kongen ikke falde i søvn. Derfor sendte han bud efter rigets krønikebog og bad om at få læst op af bogen. 2Det stykke, der blev læst, indeholdt beretningen om, hvordan Mordokaj havde angivet de to kongelige portvagter Bigtana og Teresh, der i sin tid havde lavet en sammensværgelse i den hensigt at myrde kongen.

3„Hvilken belønning fik Mordokaj i den anledning?” spurgte kongen.

„Ingen,” svarede kammertjenerne.

4-5„Er der nogle af mine embedsmænd i paladset?” spurgte kongen. Haman var netop ankommet tidligt til paladset den morgen for at anmode kongen om tilladelse til at få Mordokaj hængt i den galge, han havde rejst. Tjenerne meldte nu kongen: „Haman står her udenfor.” „Før ham ind!” befalede kongen. 6Da Haman var kommet ind, spurgte kongen: „Sig mig, Haman: Jeg har i sinde at hædre en af mine mænd. Hvordan mener du, jeg bedst kan gøre det?” Haman tænkte straks: „Mon ikke det er mig, kongen gerne vil hædre?” 7Derfor svarede han: „Hvis kongen ønsker at hædre en mand, 8skal man iføre ham en dragt, som kongen selv har haft på, og sætte ham på en hest, som kongen selv har redet på, og som bærer det kongelige diadem på hovedet. 9Så skal en af kongens øverste mænd føre ham rundt i byen, mens han råber: ‚Sådan belønner kongen den mand, han ønsker at hædre!’ ”

10„Udmærket!” svarede kongen. „Tag min kongekåbe og min hest og gør, som du har foreslået, med jøden Mordokaj, der sidder blandt dommerne i portrummet. Alt, hvad du har foreslået, skal du gøre!”

11Haman var nødt til at parere ordre. Han fik overdraget kongens dragt og hest, gav Mordokaj dragten på, hjalp ham op på hesten og førte ham gennem byens gader, mens han råbte: „Sådan belønner kongen den mand, han ønsker at hædre!”

12Bagefter vendte Mordokaj tilbage til sit arbejde i portrummet, mens Haman skyndte sig hjem med tilhyllet ansigt, fuldstændig knust. 13Da han fortalte sin kone og vennerne, hvad der var sket, sagde de: „Hvis Mordokaj er jøde, har du ikke blot trukket det korteste strå. Du kan ikke stille noget op imod ham. Du er færdig!”

14Mens de endnu talte sammen, ankom kongens tjenere for at hente Haman til den festmiddag, Ester havde forberedt.