Estere 5 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 5:1-14

Pempho la Estere kwa Mfumu

1Tsiku lachitatu Estere anavala zovala zake zaufumu ndipo anayima mʼbwalo la mʼkati la nyumba yaufumu choyangʼana ku chipinda chachikulu cha mfumu. Mfumu inakhala pa mpando waufumu mʼchipinda chachikulu moyangʼana ku chipata cholowera mʼnyumba yaufumu. 2Mfumu itaona Estere atayima mʼbwalomo inakondwera naye ndipo anamuloza ndi ndodo yagolide imene inali mʼdzanja lake. Choncho Estere anayandikira ndi kukhudza msonga ya ndodoyo.

3Kenaka mfumu inati kwa iye, “Kodi mukufuna chiyani, inu mfumukazi Estere? Nanga pempho lanu ndi chiyani? Ngakhale mutapempha theka la ufumu, ndidzakupatsani.”

4Ndipo Estere anayankha kuti, “Ngati chingakukomereni, mfumu, mubwere lero pamodzi ndi Hamani kuphwando limene ndakonzera inu mfumu.”

5Mfumu inati, “Muwuzeni abwere Hamani msanga, kotero kuti tichite monga Estere wapempha.”

Choncho mfumu ndi Hamani anafika kuphwando limene Estere anakonza. 6Akumwa vinyo, mfumu inamufunsano Estere kuti, “Kodi ukupempha chiyani tsopano? Chimene uti upemphe ndikupatsa. Chopempha chako ndi chiti? Ngakhale utafuna mpaka theka la ufumu, ndidzakupatsa.”

7Estere anayankha kuti, “Pempho langa ndi chofuna changa ndi ichi: 8Ngati mwandikomera mtima mfumu ndiponso ngati chingakukondweretseni mfumu kundipatsa chimene ndapempha ndi kuchita zimene ndifuna, mubwere mawa inu mfumu ndi Hamani ku phwando limene ndidzakukonzerani. Ndipo ndidzakuyankhani mfumu funso lanu.”

Mkwiyo wa Hamani Ukulabe pa Mordekai

9Tsiku limenelo Hamani anatuluka wokondwa ndi wosangalala kwambiri. Koma ataona Mordekai pa chipata cha mfumu ndi kuti sanayimirire kapena kumupatsa ulemu pamene iye amadutsa, Hamani anamukwiyira kwambiri, 10komabe Hamani anadziletsa ndipo anapita ku nyumba kwake.

Anayitana abwenzi ake pamodzi ndi mkazi wake Zeresi. 11Hamani anawawuza za kuchuluka kwa chuma chake ndi kuti anali ndi ana aamuna ambiri. Anawawuzanso za mmene mfumu inamukwezera ndi kumuyika kukhala woposa nduna ndi olemekezeka onse. 12Hamani anawonjeza kuti, “Ndipotu si zokhazi. Ndine ndekha amene ndayitanidwa pamodzi ndi mfumu kuphwando limene mfumukazi Estere anatikonzera. Ndipo mawa wandiyitananso pamodzi ndi mfumu. 13Koma zonsezi sindikhutira nazo ndikamaona nthawi zonse Myuda uja Mordekai atakhala pa chipata cha mfumu.”

14Mkazi wake Zeresi ndi abwenzi ake onse aja anamuwuza kuti, “Anthu apange mtanda wotalika mamita 23 ndipo mmawa upemphe mfumu kuti anthu akhomerepo Mordekai. Kenaka upite ndi mfumu kuphwando mokondwa.” Hamani anakondwera ndi uphungu umenewu ndipo mtanda unapangidwa.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以斯帖記 5:1-14

以斯帖為王和哈曼設宴

1第三天,以斯帖身穿朝服進入王宮內院,面對大殿站立,王在殿裡正面朝宮門坐在寶座上。 2王見以斯帖王后站在院內,就施恩給她,向她伸出手中的金杖,以斯帖便上前摸杖頭。 3王問道:「以斯帖王后啊,你有什麼事?你有何要求?就是半壁江山,也必賜給你!」 4以斯帖回答說:「王若願意,就請王今天帶哈曼來赴我預備的宴席。」 5王說:「快召哈曼來,我們好照以斯帖的話做。」於是王帶著哈曼以斯帖預備的宴席。 6席間,王對以斯帖說:「你要什麼?我必賜給你。你有何要求?就是半壁江山,也必為你成就。」 7以斯帖回答說:「王啊,我所要、我所求的就是, 8我若得到王的恩寵,王若願意賜我所要所求的,就請王明天帶哈曼再來赴我預備的宴席,到時我一定向王稟明。」

哈曼圖謀殺末底改

9那天哈曼出來,心中歡喜快樂。但他看見末底改在宮門前既不起身,也不對他表示畏懼,心中十分惱火。 10哈曼忍怒回到家中,把朋友和妻子細利斯叫來, 11向他們誇耀自己的榮華富貴和兒孫滿堂,以及王怎樣擢升他,使他位極人臣。 12哈曼又說:「還有,以斯帖王后只請了我隨王赴她預備的宴席。她還請我明天隨王赴宴。 13但只要我看見猶太末底改坐在宮門口,這一切對我都毫無意義。」 14他妻子細利斯和他所有的朋友對他說:「你可以叫人做一個二十三米高的木架,明天早上求王將末底改吊在上面,然後你可以快樂地隨王去赴宴。」哈曼喜歡這個提議,就叫人做了木架。