Estere 5 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 5:1-14

Pempho la Estere kwa Mfumu

1Tsiku lachitatu Estere anavala zovala zake zaufumu ndipo anayima mʼbwalo la mʼkati la nyumba yaufumu choyangʼana ku chipinda chachikulu cha mfumu. Mfumu inakhala pa mpando waufumu mʼchipinda chachikulu moyangʼana ku chipata cholowera mʼnyumba yaufumu. 2Mfumu itaona Estere atayima mʼbwalomo inakondwera naye ndipo anamuloza ndi ndodo yagolide imene inali mʼdzanja lake. Choncho Estere anayandikira ndi kukhudza msonga ya ndodoyo.

3Kenaka mfumu inati kwa iye, “Kodi mukufuna chiyani, inu mfumukazi Estere? Nanga pempho lanu ndi chiyani? Ngakhale mutapempha theka la ufumu, ndidzakupatsani.”

4Ndipo Estere anayankha kuti, “Ngati chingakukomereni, mfumu, mubwere lero pamodzi ndi Hamani kuphwando limene ndakonzera inu mfumu.”

5Mfumu inati, “Muwuzeni abwere Hamani msanga, kotero kuti tichite monga Estere wapempha.”

Choncho mfumu ndi Hamani anafika kuphwando limene Estere anakonza. 6Akumwa vinyo, mfumu inamufunsano Estere kuti, “Kodi ukupempha chiyani tsopano? Chimene uti upemphe ndikupatsa. Chopempha chako ndi chiti? Ngakhale utafuna mpaka theka la ufumu, ndidzakupatsa.”

7Estere anayankha kuti, “Pempho langa ndi chofuna changa ndi ichi: 8Ngati mwandikomera mtima mfumu ndiponso ngati chingakukondweretseni mfumu kundipatsa chimene ndapempha ndi kuchita zimene ndifuna, mubwere mawa inu mfumu ndi Hamani ku phwando limene ndidzakukonzerani. Ndipo ndidzakuyankhani mfumu funso lanu.”

Mkwiyo wa Hamani Ukulabe pa Mordekai

9Tsiku limenelo Hamani anatuluka wokondwa ndi wosangalala kwambiri. Koma ataona Mordekai pa chipata cha mfumu ndi kuti sanayimirire kapena kumupatsa ulemu pamene iye amadutsa, Hamani anamukwiyira kwambiri, 10komabe Hamani anadziletsa ndipo anapita ku nyumba kwake.

Anayitana abwenzi ake pamodzi ndi mkazi wake Zeresi. 11Hamani anawawuza za kuchuluka kwa chuma chake ndi kuti anali ndi ana aamuna ambiri. Anawawuzanso za mmene mfumu inamukwezera ndi kumuyika kukhala woposa nduna ndi olemekezeka onse. 12Hamani anawonjeza kuti, “Ndipotu si zokhazi. Ndine ndekha amene ndayitanidwa pamodzi ndi mfumu kuphwando limene mfumukazi Estere anatikonzera. Ndipo mawa wandiyitananso pamodzi ndi mfumu. 13Koma zonsezi sindikhutira nazo ndikamaona nthawi zonse Myuda uja Mordekai atakhala pa chipata cha mfumu.”

14Mkazi wake Zeresi ndi abwenzi ake onse aja anamuwuza kuti, “Anthu apange mtanda wotalika mamita 23 ndipo mmawa upemphe mfumu kuti anthu akhomerepo Mordekai. Kenaka upite ndi mfumu kuphwando mokondwa.” Hamani anakondwera ndi uphungu umenewu ndipo mtanda unapangidwa.

Bibelen på hverdagsdansk

Esters Bog 5:1-14

Ester finder nåde hos kongen

1To dage senere5,1 På hebraisk: „på den tredje dag”, hvilket svarer til „to dage senere” på dansk. iførte Ester sig sin dronningekåbe og gik ind i den inderste gård og stillede sig foran indgangen til tronsalen. Derinde sad kongen på tronen, og han kunne se dem, der opholdt sig udenfor. 2Da han fik øje på Ester, rakte han guldscepteret frem imod hende, og hun gik frem mod ham og rørte ved spidsen af scepteret.

3„Hvad har du på hjerte, dronning Ester?” spurgte han. „Fortæl mig, hvad du ønsker. Jeg vil give dig hvad som helst, du beder om—om det så er det halve kongerige!”

4Ester svarede: „Hvis det behager kongen, vil jeg bede kongen og Haman om i aften at komme til en lille festmiddag, som jeg har forberedt i dag.”

5Da sagde kongen til sine tjenere: „Skynd jer at få fat i Haman!”

Samme aften indfandt kongen og Haman sig til Esters festmiddag. 6Mens de sad og drak vin, sagde kongen til Ester: „Sig mig nu, hvad det er, du ønsker! Jeg giver dig det, om det så er det halve kongerige!”

7-8Hun svarede: „Hvis det behager kongen at opfylde mit ønske, vil jeg bede kongen om at komme igen i morgen aften sammen med Haman til endnu en lille festmiddag, som jeg vil gøre klar til jer. Så skal jeg nok fortælle, hvad jeg har på hjerte.”

Hamans plan om at dræbe Mordokaj

9Haman var glad og fornøjet, da han gik hjem efter den fine middag. Men da han gik ud af paladsets port, fik han øje på Mordokaj, der hverken rejste sig for ham eller viste det mindste tegn på ærbødighed. Det gjorde ham rasende, 10men han beherskede sig og skyndte sig hjem. Da han var kommet hjem, tilkaldte han sine nærmeste venner og sin kone Zeresh. 11Med selvtilfreds mine pralede han af sin store rigdom, sine mange sønner og den ære, kongen havde vist ham ved at forfremme ham til den næstøverste i hele perserriget.

12„Nu skal I høre!” sagde han. „I dag inviterede dronning Ester mig til en privat festmiddag sammen med hende og kongen. Hun havde selv forberedt det hele til os to! Og i morgen har hun inviteret os igen!” 13Så tilføjede han: „Men jeg kan ikke rigtig glæde mig over det, så længe den ubehøvlede jøde, Mordokaj, sidder i paladsets portrum.”

14Hans kone og venner kom straks med et godt forslag: „Du skal få lavet en 22,5 meter5,14 Mere ordret: „50 alen høj”. høj galge, og i morgen kan du så bede kongen om at få Mordokaj hængt i den! Derefter kan intet forstyrre din glæde ved den kongelige festmiddag.”

Det forslag syntes Haman godt om, og han sørgede straks for at få galgen rejst.