Estere 2 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 2:1-23

Mfumu Ikwatira Estere

1Pambuyo pake mtima wa Ahasiwero utatsika, Ahasiwero anakumbukira Vasiti ndi zimene anachita Vasitiyo. Anakumbukiranso lamulo lomukhudza limene anasindikiza. 2Tsono anyamata a mfumu amene ankamutumikira anati, “Mfumu, akufunireni anamwali okongola. 3Mfumu isankhe oyangʼanira pa chigawo chilichonse cha ufumu wake kuti abwere nawo pamodzi anamwali onse okongola ku nyumba yosungira akazi ku Susa. Hegai, mdindo wofulidwa wa mfumu, amene amayangʼanira amayi, akhale wosamalira anamwaliwa ndipo aziwapatsa mafuta odzola. 4Ndipo namwali amene mfumu yakondwera naye akhale mfumukazi mʼmalo mwa Vasiti.” Mfumu inakondwera ndi uphunguwu, ndipo inachita momwemo.

5Myuda wina wa fuko la Benjamini, dzina lake Mordekai, mwana wa Yairi, mwana wa Simei, mwana wa Kisi, anali mu mzinda wa Susa. 6Iyeyu anali mmodzi mwa anthu amene anatengedwa ukapolo ndi Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu pamodzi ndi Yekoniya mfumu ya Yuda. 7Mordekai nʼkuti atalera Hadasa, amene ankatchedwanso Estere, mwana wamkazi wa amalume ake chifukwa analibe abambo kapena amayi. Mtsikanayu anali wokongola ndi wooneka bwino ndipo Mordekai ankamutenga ngati mwana wake weniweni pamene abambo ndi amayi ake anamwalira.

8Lamulo la mfumu atalilengeza ndi kubwera nawo pamodzi anamwali ambiri ku mzinda wa Susa kuti akasamalidwe ndi Hegai, Estere nayenso anatengedwa kupita naye ku nyumba ya mfumu kuti akasamalidwe ndi Hegai woyangʼanira nyumba yosungiramo akazi uja. 9Hegai anasangalatsidwa naye namwaliyo ndipo anamukomera mtima. Mosataya nthawi anamupatsa mafuta ake odzola ndi chakudya chapadera. Anamusankhiranso anamwali asanu ndi awiri a ku nyumba ya mfumu kuti azimutumikira, ndipo iye pamodzi ndi anamwali omutumikira aja anawapatsa malo abwino koposa mʼnyumba yosungira akazi.

10Estere sanawulule mtundu wake ndi abale ake chifukwa Mordekai anamuletsa kutero. 11Tsiku ndi tsiku Mordekai ankayendayenda pafupi ndi bwalo la nyumba yosungiramo akazi ija kuti adziwe za moyo wa Estere ndi kuti zinthu zikumuyendera bwanji.

12Tsono nthawi inkafika kuti namwali aliyense akaonekere kwa mfumu Ahasiwero, pakutha pa miyezi khumi ndi iwiri yomwe inakhazikitsidwa kuti amayi azidzikongoletsa. Pa miyezi isanu ndi umodzi ankadzola mafuta a mure ndipo pa miyezi isanu ndi umodzi inayo ankadzola zonunkhira ndi zokongoletsa. 13Ndipo namwali ankapita kwa mfumu motere: Ankaloledwa kutenga chilichonse angafune mʼnyumba yosungiramo akazi kupita nacho ku nyumba ya mfumu. 14Ankalowa madzulo kwa mfumu ndi kutuluka mmawa kupita ku nyumba ina yosungira akazi yomwe ankayangʼanira ndi Saasigazi, mdindo wofulidwa wa mfumu amene amayangʼanira akazi a mfumu. Namwali sankabwerera kwa mfumu pokhapokha amukomere mtima ndi kumuyitana potchula dzina lake.

15Tsono inafika nthawi kuti Estere, mwana wamkazi wa Abihaili amenenso analeredwa ndi Mordekai amalume ake, alowe kwa mfumu. Iye sanapemphe kanthu kalikonse, koma anatenga zokhazo zimene ananena Hegai mdindo wofulidwa wa mfumu woyangʼanira nyumba yosungiramo akazi. Ndipo aliyense amene anamuona Estere, anasangalatsidwa naye. 16Anapita naye kwa mfumu Ahasiwero ku nyumba ya ufumu pa mwezi wa khumi, mwezi wa Tebete, chaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wake.

17Ndipo mfumu inamukonda Estere koposa wina aliyense wa akazi aja, kotero inamukonda ndi kumukomera mtima koposa wina aliyense wa anamwali aja. Choncho anamumveka chipewa chaufumu pa mutu pake nakhala mfumukazi mʼmalo mwa Vasiti. 18Ndipo mfumu inakonza phwando lalikulu, phwando la Estere, kukonzera anthu olemekezeka ndi nduna zake zonse. Analamuliranso kuti anthu mʼzigawo zonse asapereke msonkho ndipo anapereka mphatso monga mwakukoma mtima kwa mfumu.

Mordekai Awulula Chiwembu

19Anamwali atasonkhanitsidwa pamodzi, Mordekai anakhala pansi pa chipata cha mfumu. 20Koma Estere anali asanawululebe za mtundu wake ndi anthu a pa banja lake monga momwe analamulira Mordekai, chifukwa anapitirira kutsata malangizo a Mordekai monga ankachitira pamene ankamulera.

21Pa nthawi imene Mordekai ankalondera pa chipata cha mfumu, Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa amfumu, olondera pa khomo la nyumba yake, anayipidwa mtima ndipo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero. 22Koma Mordekai atazindikira za chiwembuchi anawuza mfumukazi Estere ndipo iye anakawuza mfumu mʼmalo mwa Mordekai. 23Ndipo pamene anafufuza za chiwembuchi kuti zinali zoona, adindo awiriwa anaphedwa monyongedwa. Zinthu izi zinalembedwa mʼbuku la Mbiri ndi kusungidwa ndi Mfumu.

New Russian Translation

Есфирь 2:1-23

Есфирь становится царицей

1Спустя некоторое время, когда гнев царя Ксеркса остыл, он вспомнил Астинь, то, что она сделала, и то, что он приказал сделать по отношению к ней. 2Тогда царские слуги, которые прислуживали ему, предложили:

– Пусть для царя поищут красивых молодых девушек. 3Пусть царь назначит особых людей в каждую из провинций своего царства. И пусть они соберут всех красивых молодых девушек в гарем крепости Сузы, под надзор царского евнуха Гегая, который смотрит за женщинами, и пусть им выдают косметические масла для ухода за телом. 4Пусть девушка, которая понравится царю, станет царицей вместо Астинь.

Этот совет понравился царю, и он воспользовался им. 5В крепости Сузы был иудей из рода Вениамина по имени Мардохей, сын Иаира, сына Шимея, сына Киша, 6который был уведен в плен из Иерусалима царем Вавилона Навуходоносором2:6 Навуходоносор II, самый великий царь Нововавилонской империи, правил с 605 по 562 гг. до н. э. вместе с теми, кто был пленен с царем Иудеи Иехонией. 7Мардохей вырастил Гадассу, она же Есфирь, – свою двоюродную сестру, потому что у нее не было ни отца, ни матери. Девушка была пригожа и красива, и когда ее отец и мать умерли, Мардохей взял ее к себе вместо дочери.

8После того как царская воля и указ были объявлены во всеуслышание, в крепость Сузы привели и отдали под надзор Гегая множество девушек. Есфирь тоже была взята в царский дворец и отдана под надзор Гегая, смотрителя гарема. 9Девушка понравилась ему и приобрела его расположение. Он сразу же выдал ей пропитание и косметические масла для ухода за телом. Он приставил к ней семь служанок, выбранных для нее из царского дворца, и переселил ее вместе со служанками в лучшее помещение гарема.

10Есфирь не рассказывала ни о своем народе, ни о сородичах, потому что Мардохей запретил ей. 11Мардохей каждый день прогуливался перед двором гарема, чтобы узнать, как поживает Есфирь и что делается с ней.

12Прежде чем в свой черед войти к царю Ксерксу, каждая девушка должна была двенадцать месяцев ухаживать за собой, как было предписано женщинам: шесть месяцев притираний мирровым маслом и шесть месяцев благовониями и другими средствами. 13Когда девушка входила к царю, ей давали все, чего бы она ни захотела взять с собой из гарема в царский дворец. 14Вечером она уходила туда, а на утро возвращалась в другую часть гарема под надзор Шаашгаза, царского евнуха, который смотрел за наложницами. Она уже не возвращалась к царю, если он не оставался ею доволен и не призывал ее по имени. 15Когда пришел черед Есфири, дочери Авихаила, дяди Мардохея, который взял ее к себе вместо дочери, она не попросила ничего, кроме того, что посоветовал царский евнух, смотритель гарема Гегай. А Есфирь приобрела расположение у всех, кто ее видел. 16Ее отвели к царю Ксерксу в его дворец в десятом месяце, в месяце тевете, в седьмой год его царствования2:16 В начале зимы 479 г. до н. э..

17Есфирь понравилась царю больше всех прочих женщин, она приобрела его расположение и привязанность больше, чем все остальные девушки. Он возложил ей на голову царский венец и сделал ее царицей вместо Астинь. 18Царь устроил великий пир в честь Есфири для всех своих сановников и знати. Он объявил по всем провинциям праздник2:18 Или: «освобождение от налогов». и с царской щедростью раздал дары.

Мардохей раскрывает заговор

19Когда девушек собирали во второй раз, Мардохей сидел у царских ворот. 20А Есфирь ничего не говорила о своих родственниках и о народе, как сказал ей Мардохей, потому что она слушалась наставлений Мардохея, как в те времена, когда он ее растил.

21В то время как Мардохей сидел у царских ворот, Бигтан и Тереш, двое царских евнухов, охранявших порог, разгневались и составили заговор, чтобы убить царя Ксеркса. 22Но Мардохей узнал о заговоре и рассказал царице Есфири, а она рассказала об этом царю от имени Мардохея. 23Дело было расследовано и доказано, и обоих евнухов повесили на виселице2:23 Или: «посадили на кол»; также 5:14; 6:4; 7:9; 8:7; 9:13, 14, 25.. Обо всем этом было записано в летописи в присутствии царя.