Estere 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 1:1-22

Vasiti Mkazi wa Mfumu Achotsedwa

1Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi. 2Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa, 3ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.

4Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake. 5Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu. 6Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira. 7Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu. 8Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.

9Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.

10Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi 11kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri. 12Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.

13Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama. 14Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.

15Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”

16Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero. 17Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’ 18Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”

19“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye. 20Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”

21Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani. 22Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.

New Serbian Translation

Књига о Јестири 1:1-22

Царица Астина свргнута

1Било је то у време Артаксеркса, када је Артаксеркс царевао од Индије па све до Куша у стотину двадесет седам области. 2У то време, док је цар Артаксеркс седео на престолу свог царства, у двору који је био у Сусану, 3треће године своје владавине је приредио гозбу за све своје главаре и све његове слуге. А заповедници војске Персије и Мидије, племићи и главари области су били пред њим.

4Он им је много дана показивао богатство сјаја свог царства и раскош славе свога величанства, чак стотину осамдесет дана. 5Када су се ти дани завршили, цар је приредио за све људе који су се затекли на двору у Сусану – од највећих до најмањих – седмодневну гозбу у дворишту врта царског двора. 6Беле и љубичасте завесе су висиле на врпцама од финог платна и од скерлета на сребрним алкама и мермерним стубовима. Златни и сребрени лежајеви били су на поду од порфира, седефа, црног и белог мермера. 7Пило се из златних чаша и других различитих посуда. Било је обиља царског вина, онако како доликује царској дарежљивости. 8Ипак, пило се према указу да нико на то није био примораван. Наиме, цар је наредио сваком надгледнику свог двора да поступа по жељи сваког понаособ.

9Такође је и царица Астина приредила гозбу за жене у Артаксерксовом царском двору.

10А седмог дана, када је вино разгалило царево срце, заповедио је Меуману, Висати, Арвони, Викти, Авакти, Зетару и Харкасу – седморици евнуха који су служили пред царем Артаксерксом – 11да доведу царицу Астину пред цара, са царском круном, да народу и главарима покаже њену лепоту. Наиме, она је била веома лепа. 12Али царица Астина је одбила да дође на цареву заповест коју су јој пренели евнуси. На то се цар јако разгневио и у себи разбуктао од беса.

13Тада је цар упитао мудраце, који су умели да разумеју времена – јер, цар је тако поступао. Изложио би ствар свима који су познавали закон и право; 14онима који су му били блиски: Карсени, Сетару, Адмати, Тарсису, Мересу, Марсени и Мемукану, седморици персијских и мидијских главара који су гледали царево лице и били најузвишенији у царству:

15„Шта закон налаже да се уради са царицом Астином зато што није послушала заповест цара Артаксеркса коју су јој пренели евнуси?“

16Тада је пред царем и главарима одговорио Мемукан: „Царица Астина није погрешила само против цара већ и против свих главара и против свег народа у свим областима цара Артаксеркса. 17Наиме, царичин случај ће доћи до свих жена и изазвати их да презриво гледају своје мужеве када разгласе: ’Цар Артаксеркс је наредио да му пред њега доведу царицу Астину, а она није дошла!’ 18И колико данас ће кнегиње Персије и Мидије, које буду чуле за царичин случај, рећи тако свим царевим главарима. Биће много презира и гнева.

19Ако је цару по вољи, нека се од њега пошаље царски указ и нека се за стално запише у законе Персије и Мидије: царица Астина више неће долазити у присуство цара Артаксеркса, а царичино достојанство цар даје другој која је боља од ње. 20Царев ће се указ – који ће он да донесе – чути по свем његовом царству, које је велико. И све ће жене да поштују своје мужеве, од највећег до најмањег.“

21Овај савет се допао цару и главарима, па је цар поступио према Мемукановој речи. 22Послао је писма по свим царским областима, и то свакој области на њеном писму и сваком народу на његовом језику – да сваки човек буде домаћин свог дома и говори језиком свог народа.