Eksodo 8 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 8:1-32

1Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze. 2Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule. 3Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo. 4Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”

5Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’ ”

6Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto. 7Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.

8Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”

9Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”

10Farao anati, “Mawa.”

Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu. 11Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”

12Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao. 13Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa 14Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha. 15Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.

Mliri wa Nsabwe

16Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.” 17Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe. 18Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.

19Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.

Mliri wa Ntchentche Zoluma

20Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze. 21Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’ ”

22“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino. 23Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”

24Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.

25Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”

26Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife. 27Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”

28Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”

29Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”

30Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova. 31Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala. 32Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.

La Bible du Semeur

Exode 8:1-28

1L’Eternel dit encore à Moïse : Ordonne à Aaron d’étendre la main avec son bâton vers les fleuves, les canaux et les étangs, pour faire venir les grenouilles sur l’Egypte.

2Aaron étendit la main vers les cours d’eau d’Egypte, et les grenouilles en sortirent et envahirent le pays. 3Mais les magiciens en firent autant par leurs sortilèges : ils firent aussi venir les grenouilles sur l’Egypte.

4Le pharaon convoqua Moïse et Aaron et leur dit : Priez l’Eternel pour qu’il nous débarrasse des grenouilles, moi et mon peuple ; alors je laisserai aller votre peuple pour qu’il lui offre des sacrifices.

5Moïse répondit au pharaon : Fixe toi-même le moment où je dois prier en ta faveur, en faveur de tes hauts fonctionnaires et de tes sujets, pour que l’Eternel te débarrasse des grenouilles, les fasse disparaître de tes maisons, et il n’en restera plus que dans le Nil.

6Le pharaon répondit : Que ce soit pour demain.

Moïse dit : Il sera fait comme tu le demandes, pour que tu saches que l’Eternel notre Dieu n’a pas d’égal. 7Les grenouilles te laisseront ainsi que tes hauts fonctionnaires et tes sujets, et elles quitteront tes maisons ; il n’en restera que dans le Nil.

8Moïse et Aaron quittèrent le pharaon, et Moïse pria l’Eternel de faire partir les grenouilles qu’il avait envoyées contre le pharaon. 9L’Eternel fit ce que Moïse lui demandait : les grenouilles périrent dans les maisons, dans les cours et dans les champs. 10On en fit des tas en quantité considérable et le pays en fut empesté. 11Mais lorsque le pharaon vit que les choses s’arrangeaient, il s’entêta et n’écouta pas Moïse et Aaron, comme l’Eternel l’avait dit.

Troisième fléau : les moustiques

12L’Eternel dit à Moïse : Ordonne à Aaron d’étendre son bâton et d’en frapper la poussière du sol pour qu’elle se change en moustiques8.12 Autres traductions : poux, vermine. dans toute l’Egypte.

13Et ils obéirent : Aaron étendit la main et frappa de son bâton la poussière du sol, et la poussière de tout le pays se transforma en moustiques qui se répandirent sur les hommes et le bétail. 14Les magiciens essayèrent d’accomplir le même miracle par leurs sortilèges et de produire des moustiques, mais ils n’y parvinrent pas. Et les hommes et le bétail restaient couverts de moustiques. 15Alors les magiciens dirent au pharaon : C’est le doigt de Dieu8.15 C’est-à-dire le signe de l’intervention d’un dieu plus puissant que nous. Peut-être les magiciens désignaient-ils aussi le bâton d’Aaron par cette expression-là. !

Pourtant, le pharaon s’obstina et il n’écouta pas Moïse et Aaron, comme l’Eternel l’avait dit.

Quatrième fléau : les mouches venimeuses

16L’Eternel dit à Moïse : Va de bon matin te placer sur le passage du pharaon, lorsqu’il sortira pour aller au bord de l’eau et dis-lui : « Voici ce que l’Eternel t’ordonne : Laisse aller mon peuple, pour qu’il me rende un culte. 17Si tu refuses, je vais lâcher les mouches venimeuses contre toi, contre tes hauts fonctionnaires, contre tes sujets, et elles envahiront tes maisons, celles des Egyptiens en seront remplies et le sol en sera couvert. 18Mais, en ce jour-là, j’épargnerai la région de Goshen8.18 A l’est du delta du Nil. où demeure mon peuple : les mouches ne l’infesteront pas afin que tu saches que moi, l’Eternel, je suis présent dans ce pays. 19Ainsi je ferai une distinction entre mon peuple et le tien en épargnant le mien. C’est demain que ce signe miraculeux aura lieu. »

20L’Eternel fit comme il l’avait annoncé. Un formidable essaim de mouches venimeuses pénétra dans le palais du pharaon, dans la demeure de ses hauts fonctionnaires, et toute l’Egypte fut ravagée par les mouches. 21Le pharaon convoqua Moïse et Aaron et leur dit : Allez faire des sacrifices à votre Dieu, dans le pays.

22Moïse répliqua : Il n’est pas convenable d’agir ainsi car nos sacrifices à l’Eternel notre Dieu seraient considérés comme abominables par les Egyptiens. Si nous les offrons sous leurs yeux, ils nous lapideront8.22 Parce que les Egyptiens vénéraient certains de ces animaux comme des dieux (le taureau, le bœuf et la vache).. 23Nous irons à trois jours de marche dans le désert et nous offrirons des sacrifices à l’Eternel notre Dieu, comme il nous l’a ordonné.

24Le pharaon reprit : Eh bien ! Je vous laisse aller offrir des sacrifices à l’Eternel votre Dieu dans le désert ; seulement, ne vous éloignez surtout pas trop. Et priez pour moi !

25Moïse répondit : Dès que je serai sorti de chez toi, je prierai l’Eternel, et demain, le pharaon, ses hauts fonctionnaires et ses sujets seront débarrassés des insectes malfaisants. Seulement, que le pharaon ne recommence pas à nous tromper en refusant de laisser notre peuple aller offrir des sacrifices à l’Eternel.

26Moïse sortit de chez le pharaon et pria l’Eternel. 27Et l’Eternel exauça Moïse : les mouches venimeuses laissèrent le pharaon, ses hauts fonctionnaires et ses sujets ; il n’en resta pas une seule. 28Mais cette fois-ci encore, le pharaon s’entêta et ne laissa pas partir le peuple.