Eksodo 40 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 40:1-38

Adzutsa Chihema

1Kenaka Yehova anati kwa Mose, 2“Imika chihema, tenti ya msonkhano, tsiku loyamba la mwezi. 3Uyikemo bokosi la umboni ndipo uphimbe bokosilo ndi katani. 4Ulowetsemo tebulo ndi kuyika zimene zimakhala pamenepo. Kenaka ulowetse choyikapo nyale ndipo uyikepo nyale zake. 5Uyike guwa lofukiza la golide patsogolo pa bokosi la umboni ndipo uyike katani ya pa chipata cha chihema.

6“Uyike guwa lansembe yopsereza patsogolo pa chipata cha chihema, tenti ya msonkhano. 7Uyike beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uyikemo madzi. 8Upange bwalo lozungulira chihemacho ndipo uyike katani ya pa chipata cha bwalolo.

9“Utenge mafuta wodzozera ndipo udzoze chihema ndi chilichonse chili mʼmenemo ndipo zidzakhala zoyeretsedwa. 10Kenaka udzoze guwa lansembe lopsereza ndi ziwiya zake zonse. Ulipatule guwalo ndipo lidzakhala loyera kwambiri. 11Udzoze beseni ndi miyendo yake ndipo uzipatule.

12“Ubwere ndi Aaroni ndi ana ake pa chipata cha tenti ya msonkhano ndipo uwasambitse ndi madzi. 13Kenaka umuveke Aaroni zovala zopatulika, umudzoze ndi kumupatula kotero kuti athe kunditumikira monga wansembe. 14Ubweretse ana ake ndipo uwaveke minjiro. 15Uwadzoze monga momwe unadzozera abambo awo, kotero kuti anditumikire monga ansembe. Kudzozedwako kudzakhala unsembe wawo pa mibado ndi mibado” 16Mose anachita zonse monga Yehova anamulamulira.

17Kotero anayimika chihema tsiku loyamba la mwezi woyamba mʼchaka chachiwiri. 18Nthawi imene Mose anayimika chihema, anayika matsinde mʼmalo ake, kuyimitsa maferemu, kulowetsa mitanda ndi kuyika nsichi. 19Kenaka anayika tenti pamwamba pa chihema ndipo anayika chophimba pa tenti monga momwe Yehova analamulira Mose.

20Iye anatenga miyala ya umboni nayika mʼbokosi lija ndi kuyika chivundikiro pamwamba pake. 21Kenaka analowetsa bokosilo mʼchihema ndipo anapachika katani ndi kubisa bokosi la umboni monga momwe Yehova analamulira iye.

22Mose anayika tebulo mu tenti ya msonkhano kumpoto kwa chihema, kunja kwa katani, 23ndipo anayikapo buledi pamaso pa Yehova, monga momwe Yehova analamulira Mose.

24Iye anayikanso choyikapo nyale mu tenti ya msonkhano moyangʼanana ndi tebulo mbali yakummwera kwa chihema. 25Ndipo anayikapo nyale zija pamaso pa Yehova, monga Yehova analamulira Mose.

26Mose anayika guwa la golide mu tenti ya msonkhano patsogolo pa katani 27ndipo anapserezapo lubani wonunkhira monga Yehova anamulamulira. 28Kenaka anayika katani ya pa chipata cha chihema.

29Iye anayika guwa lansembe yopsereza pafupi ndi chipata cha chihema, tenti ya msonkhano, ndipo anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya ufa monga Yehova anamulamulira.

30Iye anayika beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo anathiramo madzi wosamba, 31ndipo Mose, Aaroni ndi ana ake amasamba manja ndi mapazi awo. 32Iwo amasamba nthawi zonse akamalowa mu tenti ya msonkhano kapena kuyandikira guwa lansembe monga Yehova analamulira Mose.

33Kenaka Mose anamanga bwalo kuzungulira chihema ndi guwa lansembe ndipo anayika katani ya pa chipata cha bwalo. Kotero Mose anamaliza ntchito.

Ulemerero wa Yehova

34Kenaka mtambo unaphimba tenti ya msonkhano, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho. 35Mose sanathe kulowa mu tenti ya msonkhano chifukwa mtambo unali utakhazikika pa chihemacho, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho.

36Pa maulendo awo onse, mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso pamene analipo. 37Koma ngati mtambo sunachoke, iwo sankasamukanso mpaka tsiku limene udzachoke. 38Kotero mtambo wa Yehova unkakhala pamwamba pa chihema usana, ndi mtambo wamoto umakhala usiku, pamaso pa nyumba yonse ya Israeli pa masiku onse aulendo wawo.

Священное Писание

Исход 40:1-38

Установление священного шатра

1Вечный сказал Мусе:

2– Ты возведёшь священный шатёр – шатёр встречи – в первый день первого месяца. 3Поставь в нём сундук соглашения и закрой его завесой. 4Внеси стол и расставь на нём всю его утварь. Потом внеси светильник и поставь на нём лампады. 5Поставь золотой жертвенник для возжигания благовоний перед сундуком соглашения и повесь завесу у входа в священный шатёр.

6Поставь жертвенник для всесожжений перед входом в священный шатёр – шатёр встречи; 7поставь умывальник между шатром встречи и жертвенником и налей в него воды. 8Поставь вокруг него двор и у входа повесь завесу.

9Возьми масло для помазания и помажь священный шатёр и всё, что в нём. Освяти его и всю утварь, и он будет свят. 10Помажь жертвенник для всесожжений и всю утварь. Освяти жертвенник, и он будет великой святыней. 11Помажь умывальник и его основание и освяти их.

12Приведи Харуна и его сыновей к входу в шатёр встречи и омой их водой. 13Надень на Харуна священные одеяния, помажь его и освяти, чтобы он мог быть Моим священнослужителем. 14Приведи его сыновей и одень их в рубашки. 15Помажь их точно так же, как их отца, чтобы они могли быть Моими священнослужителями. Это будет помазание на священство навеки, в грядущих поколениях.

16Муса сделал всё точно так, как повелел ему Вечный.

17В первый день первого месяца второго года40:17 То есть через один год после выхода из Египта. священный шатёр был возведён. 18Муса поставил священный шатёр, положил его основания, поднял брусья, вставил перекладины и поставил столбы. 19Затем он раскинул покров над священным шатром и растянул над ним укрытие, как повелел ему Вечный.

20Он взял плитки священного соглашения и положил их в сундук. Он прикрепил к сундуку шесты и положил на него крышку искупления. 21Затем он внёс сундук в священный шатёр, повесил закрывающую завесу и закрыл сундук соглашения, как повелел ему Вечный.

22Муса поставил стол в шатре встречи, на северной его стороне, за завесой, 23и разложил на нём священный хлеб, как повелел ему Вечный.

24Он поставил светильник в шатре встречи напротив стола, на южной стороне священного шатра, 25и зажёг перед Вечным лампады, как повелел ему Вечный.

26Муса поставил золотой жертвенник в шатре встречи перед завесой 27и зажёг на нём благовония, как повелел ему Вечный. 28Он повесил завесу у входа в священный шатёр.

29Он поставил жертвенник для всесожжений рядом со входом в священный шатёр – шатёр встречи – и принёс на нём всесожжения и хлебные приношения, как повелел ему Вечный.

30Он поставил умывальник между шатром встречи и жертвенником, налил в него воду для омовений; 31Муса, Харун и его сыновья мыли в нём руки и ноги. 32Они омывались всякий раз, когда входили в шатёр встречи или приближались к жертвеннику, как повелел Мусе Вечный.

33Муса сделал двор вокруг священного шатра и жертвенника и повесил у входа завесу. Так Муса завершил работу.

Слава Вечного

34Облако покрыло шатёр встречи, и слава Вечного наполнила священный шатёр. 35Муса не мог войти в шатёр встречи, потому что на шатёр опустилось облако, и слава Вечного наполнила священный шатёр.

36Во всех странствиях исраильтян, когда облако поднималось от священного шатра, они отправлялись в путь; 37но если облако не поднималось, они не отправлялись в путь до тех пор, пока оно не поднималось. 38Облако Вечного было над священным шатром днём, а ночью в этом облаке горел огонь на глазах у всего Исраила во все дни их странствий.