Eksodo 36 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 36:1-38

1Choncho Bezaleli, Oholiabu pamodzi ndi anthu aluso onse amene Yehova anawapatsa luso ndi nzeru zodziwira kupanga zofunika zonse zomangira malo opatulika, adzapanga zonse iwowo, monga momwe Yehova analamulira.”

2Ndipo Mose anayitana Bezaleli ndi Oholiabu ndiponso munthu aliyense waluso amene Yehova anamupatsa luso ndiponso amene anali ndi mtima wofuna kugwira ntchito. 3Iwo analandira kuchokera kwa Mose zopereka zonse Aisraeli anabweretsa kuti agwirire ntchito yomanga malo wopatulika. Ndipo anthu anapitirira kupereka zopereka zaufulu mmawa uliwonse. 4Kotero amisiri onse amene amagwira ntchito yonse ya malo wopatulika anasiya ntchitoyo 5ndipo anati kwa Mose, “Anthu akubweretsa kuposa zimene zikufunika kugwirira ntchito imene Yehova analamulira kuti ichitike.”

6Choncho Mose analamulira ndipo analengeza mu msasa onse, “Mwamuna kapena mayi aliyense asaperekenso chopereka chilichonse cha ku malo wopatulika.” Choncho anthu analetsedwa kubweretsa zambiri, 7chifukwa zimene anali nazo zinali zoposera zimene zimafunika kugwirira ntchito yonse.

Chihema

8Anthu onse aluso pakati pa anthu ogwira ntchitoyo anapanga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso anapeta pa nsaluzo Akerubi. 9Nsalu zonse zinali zofanana. Mulitali mwake zinali mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri. 10Iwo analumikiza nsalu zisanu, kuti ikhale nsalu imodzi ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo. 11Kenaka anapanga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo. 12Iwo anasokerera zokolowekamo makumi asanu pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Anapanga kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana. 13Kenaka anapanga ngowe zagolide 50 zolumikizira nsalu ziwirizo kotero kuti zinapanga chihema chimodzi.

14Iwo anapanga nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zinalipo khumi ndi imodzi. 15Nsalu zonse khumi ndi imodzi zinali zofanana. Mulitali mwake munali mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake munali mamita awiri. 16Iwo analumikiza nsalu zisanu kukhala nsalu imodzi ndipo nsalu zinazo zisanu ndi imodzi, analumikizanso kukhala nsalu imodzinso. 17Kenaka anasokerera zokolowekamo makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija ndiponso anapanga zokolowekamo zina makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija. 18Iwo anapanga ngowe 50 zamkuwa zolowetsa mu zokolowekazo ndipo anaphatikiza nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi. 19Ndipo anapanga chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake anapanganso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.

20Iwo anapanga maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho. 21Feremu iliyonse inali yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake munali masentimita 69. 22Thabwa lililonse linali ndi zolumikizira ziwiri. Iwo anapanga maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere. 23Anapanga maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho, 24ndiponso anapanga matsinde 40 asiliva ndipo anawayika pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse anayika matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija. 25Iwo anapanganso maferemu makumi awiri a mbali yakumpoto ya chihemacho, 26ndiponso matsinde makumi anayi asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse. 27Anapanganso maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo, 28ndiponso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti. 29Pa ngodya ziwirizi panali maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba atalumikizidwa pa ngowe imodzi. Maferemu onse anali ofanana. 30Choncho panali maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri anali pansi pa feremu iliyonse.

31Iwo anapanganso mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha. Mitanda isanu inali ya maferemu a mbali imodzi ya chihema, 32mitanda isanu inanso inali ya maferemu a mbali inayo ndipo mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema. 33Anapanga mtanda wapakati omwe umachokera pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso. 34Iwo anakuta maferemuwo ndi golide ndiponso anapanga mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso anayikuta ndi golide.

35Anapanga nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo inali yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso anapetapo zithunzi za Akerubi. 36Iwo anapanga nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide. Anapanganso ngowe zagolide za nsanamirazo ndi matsinde asiliva anayi. 37Anapanga nsalu ya pa chipata cholowera mu chihema, yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira yomwe inali yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso. 38Anapanga nsanamira zisanu ndi ngowe zake. Anakuta pamwamba pa nsanamirazo ndi zomangira zake ndi golide, ndipo anapanganso matsinde asanu amkuwa.

La Bible du Semeur

Exode 36:1-38

Les artisans se mettent au travail

1Betsaléel et Oholiab et tous les hommes habiles que l’Eternel avait doués d’habileté, d’intelligence et de compétence pour exécuter tous les ouvrages à réaliser pour le sanctuaire, exécutèrent tout conformément aux ordres de l’Eternel.

2Moïse fit venir Betsaléel et Oholiab et tous les hommes habiles que l’Eternel avait doués d’habileté, et tous ceux dont le cœur était disposé à exécuter les travaux. 3Ils reçurent de Moïse toutes les contributions que les Israélites avaient apportées pour exécuter les travaux nécessaires à la construction du sanctuaire. Et chaque matin, on continuait à apporter des offrandes volontaires à Moïse. 4Alors tous les artisans habiles qui exécutaient tous les ouvrages du sanctuaire, interrompirent l’un après l’autre leur travail 5et vinrent dire à Moïse : Le peuple en apporte plus qu’il ne faut pour exécuter l’ouvrage que l’Eternel a commandé de faire.

6Là-dessus, Moïse fit passer dans le camp le mot d’ordre suivant : « Que plus personne, ni homme, ni femme, ne prépare d’offrande pour le sanctuaire. » Le peuple cessa donc d’en apporter, 7car les matériaux étaient en quantité suffisante pour l’ensemble des travaux à réaliser. Il y en avait même en surplus.

Les tentures36.8 Pour les v. 8-38, voir 26.1-37. Les mesures, en hébreu, sont en coudées (une coudée = 50 cm).

8Ainsi les artisans habiles qui étaient à l’ouvrage firent le tabernacle avec dix tentures de fin lin retors, de pourpre violette ou écarlate et de rouge éclatant ornées de chérubins, dans les règles de l’art. 9Chaque tenture avait quatorze mètres de long et deux mètres de large. Elles étaient toutes identiques. 10Cinq de ces tentures furent cousues l’une à l’autre, et l’on fit de même avec les cinq autres. 11Sur le bord de la dernière tenture de chaque assemblage, on fixa des cordons de pourpre violette. 12Il y en avait cinquante à l’extrémité de chacun des deux assemblages et les cordons se correspondaient l’un à l’autre. 13On fit aussi cinquante agrafes d’or au moyen desquelles on assembla les deux séries de tentures, de sorte que le tabernacle forma un tout.

14On confectionna aussi onze tentures de poil de chèvre pour recouvrir le tabernacle comme d’une tente. 15Ces tentures avaient quinze mètres de long et deux mètres de large. Elles étaient toutes identiques. 16On les assembla cinq d’une part et six de l’autre. 17On fixa cinquante cordons sur le bord de la dernière tenture de chaque assemblage. 18On fabriqua cinquante agrafes de bronze pour assembler la tente afin qu’elle forme un tout. 19Ensuite, on fit pour la tente une couverture de peaux de béliers teintes en rouge et une couverture de peaux de dauphins par-dessus.

L’armature

20On fit aussi des cadres en bois d’acacia, posés à la verticale, pour le tabernacle. 21Chaque cadre avait cinq mètres de long et soixante-quinze centimètres de large 22et était muni de deux tenons parallèles. On fit ainsi pour tous les cadres du tabernacle. 23On fit vingt cadres pour le côté sud du tabernacle. 24Pour chacun d’eux, on disposa deux socles d’argent, un pour chaque tenon, soit quarante socles pour les vingt cadres. 25On fit de même pour le côté nord du tabernacle : vingt cadres 26et quarante socles d’argent, deux pour chaque cadre. 27Pour l’arrière du tabernacle, tourné vers l’ouest, on fit six cadres, 28plus deux cadres comme contreforts des angles arrières du tabernacle. 29Chacun était jumelé avec l’un des cadres des extrémités, depuis le bas, et bien lié avec lui jusqu’à son sommet par un seul anneau ; c’est ainsi qu’on les fit tous deux pour les deux angles. 30Il y avait donc en tout huit cadres et seize socles d’argent, deux pour chaque cadre.

31On fit cinq traverses de bois d’acacia pour les cadres d’un côté du tabernacle, 32cinq traverses pour l’autre côté, et cinq pour le fond à l’ouest. 33Ils firent la traverse médiane qui passait au milieu des cadres, d’une extrémité à l’autre du tabernacle. 34On plaqua ces cadres d’or et l’on fabriqua des anneaux d’or pour recevoir les traverses que l’on plaqua également d’or.

Le voile et le rideau

35On fit le voile de pourpre violette et écarlate, de rouge éclatant et de fin lin retors, en l’ornant de chérubins, dans les règles de l’art. 36Pour le suspendre, on tailla quatre piliers d’acacia que l’on plaqua d’or ; ils étaient munis de crochets d’or et reposaient sur quatre socles d’argent. 37On confectionna pour l’entrée de la tente un rideau de pourpre violette et écarlate, de rouge éclatant et de fin lin retors, en ouvrage de broderie. 38On fit, pour l’y suspendre, cinq piliers avec leurs crochets ; on plaqua d’or leurs chapiteaux et leurs tringles ; leurs cinq socles étaient en bronze.