Eksodo 30 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 30:1-38

Guwa Lansembe Yofukiza

1Upange guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. 2Likhale lofanana mbali zonse. Mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91. Nyanga zake zipangidwe kumodzi ndi guwalo. 3Ukute guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse zinayi, pamodzi ndi nyanga zake. Ndipo upange mkombero wagolide kuzungulira guwalo. 4Upange mphete ziwiri zagolide ndipo uzilumikize ku guwa mʼmunsi mwa mkombero, mphete ziwiri ku mbali zonse ziwiri zoyangʼanana. Mphetozo zizigwira nsichi zonyamulira guwalo. 5Upange mizati yamtengo wa mkesha ndipo uyikute ndi golide. 6Uyike guwalo patsogolo pa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano. Apa ndi pamene ndizidzakumana nawe.

7“Aaroni ayenera kumafukiza lubani wonunkhira pa guwalo mmawa uliwonse. Pamene akukonza nyale zija afukizenso lubani. 8Aaroni ayenera kufukizanso lubani pamene ayatsa nyale madzulo kuti lubani akhale akuyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova kwa mibado imene ikubwera. 9Pa guwapo usafukize lubani wachilendo kapena kuperekapo nsembe yopsereza kapena nsembe yaufa. Usathire pa guwapo ngakhale nsembe yachakumwa. 10Aaroni azidzapereka nsembe yopepesera machimo pa nyanga za guwalo kamodzi pa chaka. Mwambowu uzidzachitika pogwiritsa ntchito magazi a nsembe yopepesera machimo, ndipo zizidzachitika mʼmibado yanu yonse. Choncho guwa lansembelo lidzakhala loyera ndi loperekedwa kwa Yehova.”

Za Chopereka Chowombolera Moyo

11Ndipo Yehova anati kwa Mose, 12“Pamene ukuchita kalembera wa Aisraeli, munthu aliyense ayenera kupereka kwa Yehova chowombolera moyo wake pamene akuwerengedwa. Motero mliri sudzabwera pa iwo pamene ukuwawerenga. 13Izi ndi zimene aliyense wolembedwa mu kawundula ayenera kupereka: theka la sekeli, kutanthauza ndalama zolemera magalamu asanu ndi limodzi malingana ndi kawerengedwe ka ndalama za ku Nyumba ya Mulungu. Paja sekeli imodzi ikulingana ndi magera makumi awiri. Theka la sekeli chidzakhala chopereka cha kwa Yehova. 14Aliyense wolembedwa mu kawundula amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira ayenera kupereka chopereka kwa Yehova. 15Anthu olemera asapereke koposa theka la sekeli ndipo osauka asapereke kuchepera theka la sekeli pamene mukupereka nsembe kwa Yehova yowombolera miyoyo yanu. 16Ulandire ndalama zopepeserazo kuchokera kwa Aisraeli ndipo zigwiritsidwe ntchito ya ku tenti ya msonkhano. Zoperekazi zidzakhala chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova, ndiponso zowombolera miyoyo yanu.”

Za Beseni Losambira

17Ndipo Yehova anati kwa Mose, 18“Upange beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso. Uliyike pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uthiremo madzi. 19Aaroni ndi ana ake azisamba mʼmanja ndi kutsuka mapazi awo ndi madzi amenewo. 20Pamene akulowa mu tenti ya msonkhano, iwo asambe madziwa kuti asafe. Ndiponso pamene akupita kukatumikira ku guwa lansembe ndi kupereka nsembe yopsereza kwa Yehova, 21azisamba mʼmanja mwawo ndi kutsuka mapazi kuti asadzafe. Limeneli ndi lamulo limene Aaroni, pamodzi ndi ana ndi zidzukulu zake mʼtsogolomo ayenera kumadzalitsatira mpaka muyaya.”

Mafuta Wodzozera

22Ndipo Yehova anati kwa Mose, 23“Utenge zonunkhira bwino kwambiri izi: makilogalamu asanu ndi limodzi a mure wamadzi, makilogalamu atatu a zonunkhira bwino za mtundu wa sinamoni, makilogalamu atatu a nzimbe yonunkhira bwino kwambiri, 24makilogalamu asanu ndi limodzi a mkesha. Zonsezi zikhale malingana ndi muyeso wa ku Nyumba ya Mulungu. Pakhalenso malita anayi a mafuta a olivi. 25Ugwiritse ntchito zinthu zimenezi kupanga mafuta opatulika odzozera, mafuta onunkhira, apangidwe ndi mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa. Awa adzakhala mafuta opatulika odzozera. 26Tsono uwagwiritse ntchito podzoza tenti ya msonkhano, Bokosi la Chipangano, 27tebulo, ndi ziwiya zake zonse, choyikapo nyale ndi zipangizo zake, guwa lofukizirapo lubani, 28guwa lansembe yopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso beseni pamodzi ndi nsichi yake. 29Zonsezi uzipatule kuti zidzakhale zopatulika, ndipo chilichonse chimene chidzakhudza zimenezi chidzakhala chopatulika.

30“Udzoze Aaroni ndi ana ake aamuna ndi kuwapatula kuti akhale ansembe onditumikira. 31Tsono awuze a Israeli kuti, mafuta wodzozera awa adzakhala wopatulika mpaka muyaya. 32Musadzadzozere munthu wamba mafuta amenewa, ndipo musadzapange mafuta wofanana ndi amenewa. Mafutawa ndi wopatulika ndipo akhale woyera kwa inu. 33Wina aliyense amene adzapanga mafuta wonunkhira wofanana nawo kapena kudzozera mafutawa munthu wamba osati wansembe ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.”

Za Zofukiza

34Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tenga muyeso wofanana wa zinthu zonunkhira izi: sitakate, onika, galibanumu pamodzi ndi lubani weniweni. 35Uziphatikize pamodzi zonsezi ndi kupanga lubani monga amachitira mmisiri wopanga zonunkhira. Athire mchere ndipo akhale woyera ndi wopatulika. 36Upere gawo lina mosalala kwambiri ndipo utapepo pangʼono ndi kuyika patsogolo pa Bokosi la Chipangano mu tenti ya msonkhano, kumene ine ndidzakumane nawe. Lubani ameneyu kwa inu adzakhala wopatulika kwambiri. 37Musapange lubani wanu potsatira njira iyi. Lubani yense wopangidwa mwa njira iyi akhale wopatulika, woperekedwa kwa Yehova. 38Aliyense amene adzapanga wofanana naye kuti asangalale ndi fungo lake ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.”

Korean Living Bible

출애굽기 30:1-38

향단

1“너는 아카시아나무로 분향할 단을 만들어라.

2그것은 가로 세로를 각각 45센티미터로 하여 네모 반듯하게 하고 높이는 90센티미터로 하며 단 네 모퉁이에는 뿔이 나오도록 만들어야 한다.

3그리고 너는 그 단의 윗면과 전후 좌우 면과 뿔을 순금으로 싸고 30:3 또는 ‘주위에’윗 가장자리에 금테를 둘러라.

4금테 아래 양쪽에는 운반채를 꿸 금고리 두 개씩을 만들어 달고

5아카시아나무로 운반채를 만들어 금으로 싸라.

6그러고서 너는 십계명을 넣어 둔 30:6 또는 ‘언약궤’법궤 위, 곧 내가 너를 만날 속죄소를 가리는 바로 그 휘장 밖에 이 향단을 갖다 놓아라.

7아론은 매일 아침 등을 손질할 때 이 단에 향기로운 향을 피워야 하며

8또 저녁에 등불을 켤 때도 이 향을 피워야 한다. 이와 같이 너희는 나 여호와 앞에서 향을 피우는 일을 대대로 계속하라.

9그리고 이 향단에는 내가 지정하지 않은 다른 향을 피워서는 안 되며 그 위에 동물이나 곡식이나 포도주를 제물로 바쳐서도 안 된다.

10아론은 일 년에 한 번씩 속죄제물의 피를 향단 네 뿔에 발라 이 단을 정결하게 해야 한다. 이 향단은 나 여호와에게 아주 거룩한 것이다. 향단을 정결하게 하는 일을 대대로 계속하여라.”

생명의 값

11여호와께서 모세에게 말씀하셨다.

12“너는 이스라엘 백성의 인구를 조사할 때 각자 자기 생명의 값을 나 여호와에게 바치게 하라. 그러면 네가 인구 조사를 할 때 그들에게 재앙이 미치지 않을 것이다.

13인구 조사를 받는 사람은 은 30:13 히 ‘성소의 세겔대로 반 세겔’약 6그램을 나 여호와에게 바치게 하라.

1420세 이상 인구 조사를 받는 사람은 모두 이 돈을 바쳐야 한다.

15너희가 이 생명의 값을 나 여호와에게 바칠 때에는 부자라고 해서 더 많이 내거나 가난한 사람이라고 해서 덜 내는 일이 없도록 하라.

16너는 이스라엘 백성에게서 이 돈을 받아 성막 비용으로 사용하여라. 나 여호와가 이것을 너희 생명의 값으로 여기고 너희를 기억하여 지켜 주겠다.”

놋으로 만든 물통

17여호와께서 모세에게 말씀하셨다.

18“너는 놋으로 넓적한 물통과 그 받침을 만들어 성막과 단 사이에 두고 거기에 물을 채워라.

19-20아론과 그의 아들들은 성막에 들어갈 때나 단에 가까이 가서 나 여호와에게 불로 제물을 태워 바치기 전에 이 물로 반드시 손발을 씻어야 한다.

21이와 같이 그들이 손발을 씻어야 죽지 않을 것이다. 이것은 그들과 그 후손들이 대대로 지켜야 할 규정이다.”

거룩한 기름

22여호와께서 다시 이렇게 말씀하셨다.

23“너는 제일 좋은 향품, 곧 순수한 몰약 30:23 히 ‘500세겔’ 약 6킬로그램, 향기로운 육계 30:23 히 ‘250세겔’약 3킬로그램, 향기로운 창포 약 3킬로그램,

24계피 약 6킬로그램, 그리고 감람기름 30:24 히 ‘한 힌’약 4리터를 구하여

25향을 만드는 방법으로 이 모든 것을 섞어 향기로운 거룩한 기름을 만들어라.

26그런 다음 너는 이 기름을 성막, 법궤,

27상과 그 모든 기구, 등대와 그 모든 기구, 향단,

28번제단과 그 모든 기구, 그리고 넓적한 물통과 그 받침에 발라

29그 모든 것을 아주 거룩한 것으로 구별하여라. 이것에 접촉하는 사람이나 물건이 다 거룩해질 것이다.

30그리고 아론과 그의 아들들에게 이 기름을 발라 그들을 거룩하게 하여 제사장으로서 나를 섬기게 하라.

31너는 또 이스라엘 백성에게 나 여호와의 말을 이렇게 전하여라. ‘이것은 너희가 나를 섬기는 데 대대로 사용해야 할 거룩한 기름이다.

32너희는 이것을 제사장이 아닌 다른 사람의 몸에 부어서는 안 되며 또 이 기름의 제조법대로 이와 같은 것을 만들어서도 안 된다. 이것은 거룩한 것이니 너희가 거룩하게 여겨라.

33이와 같은 것을 만들거나 이 기름을 제사장이 아닌 다른 사람에게 붓는 자는 누구든지 자기 백성 가운데서 제거될 것이다.’ ”

34그런 다음 여호와께서 모세에게 또 말씀하셨다. “너는 30:34 또는 ‘소합향과 나감향과 풍자향’몰약과 섭조개 가루와 페르시아 수지와 순수한 유향을 똑같은 중량으로 섞어

35향수를 만드는 방법으로 향을 만들고 거기에 소금을 쳐서 깨끗하고 거룩하게 하여라.

36그리고 너는 그 향 얼마를 빻아 곱게 가루를 만들어 내가 너와 만날 성막 안 법궤 앞에 두어라. 이것은 너희에게 아주 거룩한 것이다.

37너희는 이런 제조법으로 너희를 위해 향을 만들지 말고 그것을 나에게 바쳐진 거룩한 것으로 여겨라.

38이 향의 냄새를 맡으려고 이와 같은 것을 만드는 자는 누구든지 자기 백성 가운데서 제거될 것이다.”