Eksodo 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 3:1-22

Kuyitanidwa kwa Mose pa Chitsamba Choyaka Moto

1Tsono Mose amaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina iye anazitsogolera kupita ku chipululu ndipo anafika ku phiri la Mulungu lotchedwa Horebu. 2Kumeneko mngelo wa Yehova anaonekera kwa iye mʼmalawi amoto mʼchitsamba. Mose anaona kuti ngakhale chitsambacho chimayaka koma sichimanyeka. 3Tsono Mose anati mu mtima mwake, “Ine ndipita komweko ndikaone zodabwitsazi, chitsamba sichikunyeka chifukwa chiyani?”

4Yehova ataona kuti Mose anapatuka kuti adzaonetsetse, Mulungu anamuyitana Mose kuchokera mʼchitsambamo nati, “Mose! Mose!”

Ndipo anayankha, “Wawa.”

5Mulungu anati, “Usayandikire kuno. Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.” 6Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.” Atamva zimenezi, Mose anaphimba nkhope yake chifukwa anaopa kuona Mulungu.

7Yehova anati, “Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo chifukwa cha anthu amene akuwapsinja, ndipo ndakhudzidwa ndi masautso awo. 8Choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse mʼdzanja la Aigupto, kuwatulutsa mʼdzikolo ndi kukawalowetsa mʼdziko labwino ndi lalikulu, dziko loyenda mkaka ndi uchi, kwawo kwa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. 9Ine ndamva ndithu kulira kwa Aisraeli, ndipo ndaona mmene Aigupto akuwazunzira. 10Kotero tsopano, pita. Ine ndikukutuma kwa Farao kuti ukatulutse anthu anga, Aisraeli mʼdziko la Igupto.”

11Koma Mose anafunsa Mulungu, “Ine ndine yani kuti ndipite kwa Farao ndi kukatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto?”

12Ndipo Mulungu anati, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe kuti ndine amene ndakutuma; Ukadzatulutsa anthu anga mʼdziko la Igupto, udzapembedza Mulungu pa phiri lino.”

13Mose anati kwa Mulungu, “Ngati ndipita kwa Aisraeli ndi kukawawuza kuti, ‘Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu,’ ndipo iwo nʼkukandifunsa kuti ‘Dzina lake ndi ndani?’ Tsono ine ndikawawuze chiyani?”

14Mulungu anati kwa Mose, “NDINE AMENE NDILI. Izi ndi zimene ukanene kwa Aisraeli: ‘NDINE wandituma kwa inu.’ ”

15Mulungu anatinso kwa Mose, “Ukanene kwa Aisraeli kuti ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo, wandituma kwa inu.’ Ili ndilo dzina langa mpaka muyaya, ndipo mibado ya mʼtsogolomo izidzanditchula ndi dzina limeneli.

16“Pita, ukawasonkhanitse akuluakulu a Israeli ndipo ukati kwa iwo, ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, anandionekera ndipo akuti Iye wadzakuyenderani ndipo waona mmene Aigupto akukuzunzirani. 17Choncho wanenetsa kuti adzakutulutsani mʼdziko la Igupto, dziko la masautsoli kupita ku dziko la Akanaani, Ahiti, Aamori Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’

18“Akuluakulu a Israeli akakumvera. Kenaka iwe ndi akuluakuluwo mukapite kwa mfumu ya Igupto ndipo mukanene kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri, wakumana nafe. Tsono tikukupemphani kuti mutilole tipite pa ulendo wa masiku atatu mʼchipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu.’ 19Koma Ine ndikudziwa kuti mfumu ya Igupto sikakulolani kuti mupite pokhapokha Ine nditayikakamiza. 20Tsono Ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kukantha Aigupto ndi zodabwitsa zanga zimene ndidzazichita pakati pawo. Zikadzatha izi, Iye adzakulolani kuti mupite.

21“Ndipo ine ndidzafewetsa mtima wa Aigupto pa anthu anga, kotero kuti mukadzatuluka simudzapita wopanda kanthu. 22Mkazi aliyense adzapemphe Mwigupto woyandikana naye ndiponso mkazi amene akukhala mʼnyumba yake, kuti amupatse ziwiya za siliva ndi golide ndiponso zovala zimene mudzaveka ana anu aamuna ndi aakazi. Ndipo potero mudzawalanda zonse Aiguptowo.”

New Russian Translation

Исход 3:1-22

Моисей и горящий куст

1Моисей пас отару своего тестя Иофора, мадианского жреца. Он повел ее далеко в пустыню и пришел к Хориву, Божьей горе. 2Там ему явился Ангел Господень3:2 Ангел Господень – этот особенный Ангел отождествляется с Самим Господом. Многие толкователи видят в Нем явления Иисуса Христа до Его воплощения. То же в 14:19. в пламени3:2 Или: «как пламя». из среды горящего тернового куста. Моисей увидел, что объятый огнем куст не сгорал, 3и подумал: «Пойду и посмотрю на это великое чудо – почему куст не сгорает».

4Когда Господь увидел, что Моисей подошел посмотреть, Он позвал его из куста:

– Моисей! Моисей!

Моисей ответил:

– Вот я.

5– Не подходи ближе, – сказал Бог. – Сними свою обувь, потому что место, на котором ты стоишь, – святая земля.

6Он сказал:

– Я – Бог твоего отца, Бог Авраама, Бог Исаака и Бог Иакова.

Услышав это, Моисей закрыл лицо, потому что боялся смотреть на Бога.

7Господь сказал:

– Я увидел угнетение Моего народа в Египте и услышал, как стонут они под властью надсмотрщиков, и узнал об их муках. 8Я сошел, чтобы освободить их от ига египтян и вывести их из этой земли в добрую, просторную землю, где течет молоко и мед, – в край хананеев, хеттов, аморреев, ферезеев, хиввеев и иевусеев. 9И вот, вопль израильтян дошел до Меня. Я увидел, как угнетают их египтяне. 10А теперь иди, Я посылаю тебя к фараону, чтобы ты вывел Мой народ, израильтян, из Египта.

11Но Моисей сказал Богу:

– Кто я такой, чтобы пойти к фараону и вывести израильтян из Египта?

12Бог ответил:

– Я буду3:12 На языке оригинала здесь стоит то же слово, что и в ст. 14, где оно переведено как «Я есть». с тобой. Вот тебе знак, что Я послал тебя: когда ты выведешь народ из Египта, вы будете служить Богу на этой горе.

13Моисей сказал Богу:

– Вот, я пойду к израильтянам и скажу им: «Бог ваших отцов послал меня к вам», а они спросят: «Как Его имя?» Что мне ответить им?

14Бог ответил Моисею:

– Я Тот, Кто Я Есть. Скажи израильтянам: «„Я Есть“ послал меня к вам».

15Еще Бог сказал Моисею:

– Скажи израильтянам: «Господь3:15 Евр.: «ЙГВГ». Это имя вероятно означает «Он Есть». Здесь Бог постепенно открывает Моисею Свое имя. Бог, говоря о Себе, использует форму «Я Есть» (см. ст. 14), мы же называем Его «Он Есть». Это имя указывает на Его активное участие в жизни Своего народа и всего творения (см. ст. 12), говорит о Его вечном существовании и показывает неизменность Его природы и характера. В данном переводе это имя везде переводится как «Господь». Это имя также переводится как «Сущий»., Бог ваших отцов – Бог Авраама, Бог Исаака и Бог Иакова, послал меня к вам».

Вот Мое имя навеки.

Так Меня будут называть

из поколения в поколение.

16Иди, собери старейшин Израиля и скажи им: «Господь, Бог ваших отцов – Бог Авраама, Бог Исаака и Бог Иакова, явился мне и сказал: „Я наблюдал за вами и увидел, как с вами обращаются в Египте. 17Я обещаю вывести вас из Египта, где вы бедствуете, в землю хананеев, хеттов, аморреев, ферезеев, иевусеев и хиввеев – в землю, где течет молоко и мед“». 18Старейшины Израиля послушают тебя. Тогда ты и старейшины пойдете к царю Египта и скажете ему: «Господь, Бог евреев, явился нам. Отпусти нас на три дня в пустыню принести жертвы Господу, нашему Богу». 19Я знаю, царь Египта не отпустит вас, если не принудить его могучей рукой3:19 Так в некоторых древних переводах; букв.: «даже под крепкой рукой».. 20Поэтому Я протяну руку и поражу Египет чудесами, которые Я в нем совершу. После этого он отпустит вас. 21Я сделаю так, что египтяне хорошо отнесутся к вам и вы не уйдете с пустыми руками. 22Пусть каждая женщина попросит у соседки-египтянки и у любой другой женщины, живущей в соседнем доме, серебряных и золотых вещей и одежды. Вы наденете это на своих сыновей и дочерей. Так вы оберете египтян.