Eksodo 3 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 3:1-22

Kuyitanidwa kwa Mose pa Chitsamba Choyaka Moto

1Tsono Mose amaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina iye anazitsogolera kupita ku chipululu ndipo anafika ku phiri la Mulungu lotchedwa Horebu. 2Kumeneko mngelo wa Yehova anaonekera kwa iye mʼmalawi amoto mʼchitsamba. Mose anaona kuti ngakhale chitsambacho chimayaka koma sichimanyeka. 3Tsono Mose anati mu mtima mwake, “Ine ndipita komweko ndikaone zodabwitsazi, chitsamba sichikunyeka chifukwa chiyani?”

4Yehova ataona kuti Mose anapatuka kuti adzaonetsetse, Mulungu anamuyitana Mose kuchokera mʼchitsambamo nati, “Mose! Mose!”

Ndipo anayankha, “Wawa.”

5Mulungu anati, “Usayandikire kuno. Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.” 6Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.” Atamva zimenezi, Mose anaphimba nkhope yake chifukwa anaopa kuona Mulungu.

7Yehova anati, “Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo chifukwa cha anthu amene akuwapsinja, ndipo ndakhudzidwa ndi masautso awo. 8Choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse mʼdzanja la Aigupto, kuwatulutsa mʼdzikolo ndi kukawalowetsa mʼdziko labwino ndi lalikulu, dziko loyenda mkaka ndi uchi, kwawo kwa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. 9Ine ndamva ndithu kulira kwa Aisraeli, ndipo ndaona mmene Aigupto akuwazunzira. 10Kotero tsopano, pita. Ine ndikukutuma kwa Farao kuti ukatulutse anthu anga, Aisraeli mʼdziko la Igupto.”

11Koma Mose anafunsa Mulungu, “Ine ndine yani kuti ndipite kwa Farao ndi kukatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto?”

12Ndipo Mulungu anati, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe kuti ndine amene ndakutuma; Ukadzatulutsa anthu anga mʼdziko la Igupto, udzapembedza Mulungu pa phiri lino.”

13Mose anati kwa Mulungu, “Ngati ndipita kwa Aisraeli ndi kukawawuza kuti, ‘Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu,’ ndipo iwo nʼkukandifunsa kuti ‘Dzina lake ndi ndani?’ Tsono ine ndikawawuze chiyani?”

14Mulungu anati kwa Mose, “NDINE AMENE NDILI. Izi ndi zimene ukanene kwa Aisraeli: ‘NDINE wandituma kwa inu.’ ”

15Mulungu anatinso kwa Mose, “Ukanene kwa Aisraeli kuti ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo, wandituma kwa inu.’ Ili ndilo dzina langa mpaka muyaya, ndipo mibado ya mʼtsogolomo izidzanditchula ndi dzina limeneli.

16“Pita, ukawasonkhanitse akuluakulu a Israeli ndipo ukati kwa iwo, ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, anandionekera ndipo akuti Iye wadzakuyenderani ndipo waona mmene Aigupto akukuzunzirani. 17Choncho wanenetsa kuti adzakutulutsani mʼdziko la Igupto, dziko la masautsoli kupita ku dziko la Akanaani, Ahiti, Aamori Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’

18“Akuluakulu a Israeli akakumvera. Kenaka iwe ndi akuluakuluwo mukapite kwa mfumu ya Igupto ndipo mukanene kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri, wakumana nafe. Tsono tikukupemphani kuti mutilole tipite pa ulendo wa masiku atatu mʼchipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu.’ 19Koma Ine ndikudziwa kuti mfumu ya Igupto sikakulolani kuti mupite pokhapokha Ine nditayikakamiza. 20Tsono Ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kukantha Aigupto ndi zodabwitsa zanga zimene ndidzazichita pakati pawo. Zikadzatha izi, Iye adzakulolani kuti mupite.

21“Ndipo ine ndidzafewetsa mtima wa Aigupto pa anthu anga, kotero kuti mukadzatuluka simudzapita wopanda kanthu. 22Mkazi aliyense adzapemphe Mwigupto woyandikana naye ndiponso mkazi amene akukhala mʼnyumba yake, kuti amupatse ziwiya za siliva ndi golide ndiponso zovala zimene mudzaveka ana anu aamuna ndi aakazi. Ndipo potero mudzawalanda zonse Aiguptowo.”

La Bible du Semeur

Exode 3:1-22

L’appel et l’envoi de Moïse

1Moïse faisait paître les brebis de son beau-père Jéthro, prêtre de Madian. Il mena son troupeau au-delà du désert et parvint jusqu’à Horeb, la montagne de Dieu3.1 Aussi appelé Sinaï dans la suite du récit. C’est la montagne où Dieu va se révéler (chap. 19).. 2L’ange de l’Eternel3.2 D’après la suite du récit, l’ange de l’Eternel est l’Eternel lui-même. lui apparut dans une flamme au milieu d’un buisson : Moïse aperçut un buisson qui était tout embrasé et qui, pourtant, ne se consumait pas. 3Il se dit alors : Je vais faire un détour pour aller regarder ce phénomène extraordinaire et voir pourquoi le buisson ne se consume pas.

4L’Eternel vit que Moïse faisait un détour pour aller voir et il l’appela du milieu du buisson :

Moïse, Moïse !

– Je suis là, répondit Moïse.

5Dieu lui dit : N’approche pas d’ici, ôte tes sandales, car le lieu où tu te tiens est un lieu saint. 6Puis il ajouta : Je suis le Dieu de tes ancêtres, le Dieu d’Abraham, le Dieu d’Isaac et le Dieu de Jacob3.6 Cité en Mt 22.32 ; Mc 12.26 ; Lc 20.37 ; Ac 3.13 ; 7.32..

Alors Moïse se couvrit le visage car il craignait de regarder Dieu.

7L’Eternel reprit : J’ai vu la détresse de mon peuple en Egypte et j’ai entendu les cris que lui font pousser ses oppresseurs. Oui, je sais ce qu’il souffre. 8C’est pourquoi je suis descendu pour le délivrer des Egyptiens, pour le faire sortir d’Egypte et le conduire vers un bon et vaste pays, un pays ruisselant de lait et de miel ; celui qu’habitent les Cananéens, les Hittites, les Amoréens, les Phéréziens, les Héviens et les Yebousiens3.8 Noms de diverses peuplades habitant ce qui deviendra le pays d’Israël.. 9A présent, les cris des Israélites sont parvenus jusqu’à moi et j’ai vu à quel point les Egyptiens les oppriment. 10Va donc maintenant : je t’envoie vers le pharaon3.10 Soit Aménotep II, fils de Thoutmosis III, soit Ramsès II, pharaon de la XIXe dynastie, qui entreprit de grands travaux de construction (1290​1279–1224​1212 av. J.-C.)., pour que tu fasses sortir d’Egypte les Israélites, mon peuple.

11Moïse dit à Dieu :

Qui suis-je, moi, pour aller trouver le pharaon et pour faire sortir les Israélites d’Egypte ?

12– Sache que je serai avec toi, lui répondit Dieu. Et voici le signe auquel on reconnaîtra que c’est moi qui t’ai envoyé : quand tu auras fait sortir le peuple hors d’Egypte, vous m’adorerez sur cette montagne-ci.

13Moïse reprit : J’irai donc trouver les Israélites et je leur dirai : « Le Dieu de vos ancêtres m’a envoyé vers vous. » Mais s’ils me demandent : « Quel est son nom ? » que leur répondrai-je ?

14Alors Dieu dit à Moïse : Je suis celui qui est3.14 Autre traduction : Je suis : Je suis. D’autres comprennent : Je suis qui je suis ; je suis celui que je serai ; Je suis celui qui donne l’existence. Voir Ap 1.4, 8.. Puis il ajouta : Voici ce que tu diras aux Israélites : Je suis m’a envoyé vers vous.

15Puis tu leur diras : « L’Eternel3.15 Le nom Eternel rend le nom hébreu Yahvé qui est proche du nom Je suis que se donne Dieu., le Dieu de vos ancêtres, le Dieu d’Abraham, d’Isaac et de Jacob m’a envoyé vers vous. C’est là mon nom pour l’éternité, c’est sous ce nom que l’on se souviendra de moi pour tous les temps3.15 Cité en Mt 22.32 ; Mc 12.26 ; Ac 3.13.. 16Va donc, réunis les responsables d’Israël et dis-leur : L’Eternel, le Dieu de vos ancêtres, le Dieu d’Abraham, d’Isaac et de Jacob m’est apparu et m’a dit : J’ai résolu d’intervenir en votre faveur au regard du traitement qu’on vous inflige en Egypte. 17Aussi ai-je décidé de vous faire sortir d’Egypte, où vous êtes en proie à l’oppression, pour vous conduire dans le pays des Cananéens, des Hittites, des Amoréens, des Phéréziens, des Héviens et des Yebousiens, dans un pays ruisselant de lait et de miel. » 18Les responsables d’Israël t’écouteront et tu iras trouver le pharaon avec eux pour lui dire : « L’Eternel, le Dieu des Hébreux, est venu nous trouver. Maintenant, veuille donc nous accorder la permission de faire trois journées de marche dans le désert pour aller offrir un sacrifice à l’Eternel notre Dieu. » 19Moi, je sais que le pharaon ne vous permettra pas de partir s’il n’y est pas contraint avec puissance3.19 D’après l’ancienne version grecque. Le texte hébreu traditionnel a : même pas s’il y est contraint avec puissance.. 20C’est pourquoi j’interviendrai et je frapperai l’Egypte de toutes sortes de prodiges que j’accomplirai au milieu d’elle. Après cela, il vous renverra. 21Je ferai gagner à ce peuple la faveur des Egyptiens, de sorte qu’à votre départ, vous ne vous en irez pas les mains vides. 22Chaque femme demandera à sa voisine et à celle qui habite chez elle des ustensiles d’argent et d’or ainsi que des vêtements. Vous les donnerez à porter à vos fils et vos filles. Ainsi vous dépouillerez les Egyptiens.