Eksodo 28 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 28:1-43

Zovala za Ansembe

1“Aaroni mʼbale wako ndi ana ake aamuna, Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara uwapatule pakati pa Aisraeli. Abwere kwa iwe kuti anditumikire monga ansembe. 2Umusokere mʼbale wako, Aaroni, zovala zopatulika kuti azioneka mwaulemerero ndi molemekezeka. 3Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe. 4Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe. 5Iwo agwiritse ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira ndi yosalala yofewa.

Efodi

6“Apange efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yolukidwa mwaluso. 7Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga. 8Lamba womangira efodi akhale wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Akhale wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala.

9“Utenge miyala iwiri ya onikisi ndipo uzokotepo mayina a ana a Israeli. 10Mayina asanu ndi limodzi akhale pa mwala umodzi, ndipo mayina asanu ndi limodzi pa mwala winawo motsata mabadwidwe awo. 11Mayina a ana a Israeli uwazokote pa miyala iwiriyo, monga momwe amachitira mmisiri wozokota miyala. Ndipo uyike miyalayo mu zoyikamo zake zagolide. 12Umangirire miyala iwiriyi pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli. Aaroni azinyamula mayinawo mʼmapewa ake kuti akhale chikumbutso pamaso pa Yehova. 13Upange zoyikamo za maluwa agolide, 14ndiponso maunyolo awiri a golide wabwino kwambiri, wopetedwa ngati zingwe ndipo uwalumikize ku zoyikamozo.

Chovala Chapachifuwa

15“Upange chovala chapachifuwa chogwiritsa ntchito poweruza mlandu ndipo uchipange mwaluso kwambiri. Uchipange ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino. 16Kutalika kwake kukhale kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, ndipo chikhale chopinda pawiri. 17Uyikepo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba ukhale ndi miyala ya rubi, topazi ndi berili. 18Mzere wachiwiri pakhale miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi; 19mzere wachitatu pakhale miyala ya opera, agate ndi ametisiti. 20Mzere wachinayi pakhale miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi uyiike mu zoyikamo zagolide. 21Miyalayo ikhalepo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse uzokotedwe ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.

22“Upange timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe. 23Upangenso mphete ziwiri zagolide ndipo uzimangirire pa ngodya ziwiri za pa chovala chapachifuwa. 24Umangirire timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho. 25Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi. 26Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija. 27Upangenso mphete zina ziwiri zagolide ndipo uzilumikize kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi. 28Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.

29“Pamene Aaroni akulowa kumalo opatulika azivala chovala chapachifuwa cha zoweruzira chija chimene chalembedwa mayina a ana a Israeli kuti Yehova awakumbukire nthawi zonse. 30Ndiponso uyike Urimu ndi Tumimu mu chovala chapachifuwa cha zoweruziracho, kuti zikhale pamtima pa Aaroni. Choncho Aaroniyo adzakhala akutenga nthawi zonse zida zomuthandizira kuweruza ana a Israeli pamene adzafika pamaso pa Yehova.

Zovala Zina za Ansembe

31“Uyipangire efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo. 32Mkanjowo ukhala ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo pakhale chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike. 33Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, upange mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira zokhala ndi maberu agolide pakati pake. 34Choncho pazikhala mphonje imodzi kenaka belu limodzi, kuzungulira mpendero wa mkanjo wonse. 35Aaroni azivala mkanjowo pamene akutumikira ngati wansembe. Kulira kwa maberu kuzimveka pamene akulowa mʼmalo opatulika pamaso pa Yehova ndiponso pamene akutuluka, kuti asafe.

36“Upange duwa lagolide wabwino kwambiri kukhala ngati chidindo ndipo uzokotepo mawu akuti, choperekedwa kwa Yehova. 37Ulimange ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira ya Aaroni, ndipo duwalo likhale kutsogolo kwa nduwirayo. 38Lidzakhala pa mphumi ya Aaroni, motero iye adzasenza cholakwa chilichonse cha pa zopereka zilizonse zimene Aisraeli amazipatulira Yehova. Aaroni azivala chikwangwanichi pa mphumi pake nthawi zonse kuti Yehova alandire zopereka za anthu ake.

39“Uluke mwinjiro wa nsalu yofewa yosalala ndiponso upange nduwira ya nsalu yofewa yosalala. Lamba wake akhale wolukidwa bwino ndi munthu waluso. 40Upangirenso ana a Aaroni mwinjiro, malamba ndi nduwira kuti azioneka mwaulemu ndi molemekezeka. 41Zovala zimenezi umuveke Aaroni, mʼbale wako ndi ana ake. Kenaka uwadzoze, uwapatse udindo ndi kuwapatula kuti anditumikire ngati ansembe anga.

42“Uwapangire akabudula a nsalu yofewa oyambira mʼchiwuno kulekeza mʼntchafu kuti asamaonetse maliseche. 43Aaroni ndi ana ake ayenera kuvala akabudulawo pamene akulowa mu tenti ya msonkhano kapena pamene akupita ku guwa lansembe kukatumikira malo oyera kuopa kuti angachimwe ndi kufa.

“Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aaroni ndi zidzukulu zake.”

New Russian Translation

Исход 28:1-43

Одеяния для первосвященника

(Исх. 39:1)

1– Позови своего брата Аарона с его сыновьями Надавом и Авиудом, Элеазаром и Итамаром. Отдели их от остальных израильтян, чтобы они служили Мне как священники. 2Сделай своему брату Аарону священные одеяния для славы и величия. 3Вели мастерам, которым Я дал мудрость в таких делах, сделать одеяния для посвящения Аарона, чтобы он мог служить Мне как священник. 4Вот одежды, которые они должны сделать: нагрудник, эфод, ризу, тканую рубашку, тюрбан и пояс. Делая эти священные одеяния, в которых твой брат Аарон и его сыновья будут служить Мне как священники, 5пусть они берут золотые нити, голубую, пурпурную и алую пряжу и крученый лен.

Эфод

(Исх. 39:2-7)

6– Пусть они сделают эфод искусной работы из золотой нити, из голубой, пурпурной и алой пряжи и крученого льна. 7У эфода должно быть два наплечника, прикрепленных по двум углам, чтобы он застегивался. 8Искусно сотканный пояс эфода должен быть подобен ему: из одного с ним куска и сделан из золота, из голубой, пурпурной и алой пряжи и из крученого льна.

9Возьми два оникса и вырежь на них имена сыновей Израиля 10в порядке их рождения: шесть имен на одном камне и шесть других на другом. 11Вырежь имена сыновей Израиля на двух камнях, как камнерез вырезает печать. Вставь камни в золотые филигранные оправы 12и прикрепи их к наплечникам эфода как памятные камни для сыновей Израиля. Аарон будет носить их имена на плечах как памятный знак перед Господом. 13Сделай золотые филигранные оправы 14и две цепочки из чистого золота, свитые подобно веревке. Прикрепи цепочки к оправам.

Нагрудник

(Исх. 39:8-21)

15– Сделай нагрудник решений искусной работы, подобно эфоду, из золотой нити, из голубой, пурпурной и алой пряжи и из крученого льна. 16Пусть он будет квадратным, когда сложен вдвое: пядь28:16 Около 23 см. в длину и пядь в ширину. 17Вставь в него четыре ряда драгоценных камней. В первом ряду пусть будут рубин, топаз и берилл; 18во втором ряду – бирюза, сапфир28:18 Или: «лазурит». и изумруд; 19в третьем ряду – гиацинт, агат и аметист; 20в четвертом ряду – хризолит, оникс и яшма28:20 В некоторых случаях невозможно точно установить, какой камень имеется в виду под тем или иным еврейским названием.. Вставь их в золотые филигранные оправы. 21Камней должно быть двенадцать – по одному на каждое из имен сыновей Израиля; на каждом камне, как на печати, должно быть вырезано имя одного из двенадцати родов.

22Для нагрудника сделай цепочки из чистого золота, свитые подобно веревке. 23Сделай для него два золотых кольца и прикрепи их к двум углам нагрудника. 24Прикрепи две золотые цепочки к кольцам на углах нагрудника, 25а другие концы цепочек – к двум оправам, присоединяя их к наплечникам эфода спереди. 26Сделай еще два золотых кольца и прикрепи их к двум другим углам нагрудника с внутренней стороны эфода. 27Сделай еще два золотых кольца и прикрепи их снизу к наплечникам эфода спереди, рядом со швом прямо над поясом эфода. 28Кольца нагрудника пусть будут привязаны к кольцам эфода голубым шнуром, соединяющим нагрудник с поясом, так, чтобы нагрудник не спадал с эфода.

29Входя в Святое место, Аарон будет носить имена сыновей Израиля у сердца, на нагруднике решений, как постоянное напоминание перед Господом. 30Еще помести на нагрудник Урим и Туммим28:30 Урим и Туммим – «урим (свет) и туммим (совершенство)» – по-видимому, средства для определения Божьей воли, способ использования которых неизвестен., чтобы они были у сердца Аарона каждый раз, когда он будет входить к Господу. Так Аарон всегда будет носить у сердца орудие суда для израильтян перед Господом.

Другие одеяния первосвященника

(Исх. 39:22-26, 30-31)

31– Сделай ризу под эфод голубой, 32с вырезом для головы в середине, подшитым тканой тесьмой, как для воротника28:32 Значение этого еврейского слова неясно., чтобы он не рвался. 33Нашей гранатовые плоды из голубой, пурпурной и алой пряжи по нижнему краю ризы, с золотыми колокольчиками между ними. 34Пусть золотые колокольчики и гранатовые плоды чередуются по нижнему краю ризы. 35Аарон будет носить ее, когда служит. Звук колокольчиков будет раздаваться, когда он будет входить в святилище пред лицо Господа и когда он будет выходить, чтобы ему не умереть.

36Сделай пластинку из чистого золота и вырежь на ней, как на печати: Святыня Господня. 37Прикрепи ее к тюрбану голубым шнуром. Пусть она будет спереди тюрбана. 38Она будет на лбу Аарона, и он примет на себя вину за любую оплошность при принесении священных даров, которые израильтяне отделяют для пожертвований. Она будет на лбу Аарона постоянно, чтобы дары были угодны Господу.

39Сотки рубашку из тонкого льна и сделай к нему тюрбан из тонкого льна. Пусть пояс будет украшен шитьем.

Одежда для остальных священников

(Исх. 39:27-29)

40Сотки рубашки, пояса и головные повязки и сыновьям Аарона для славы и величия. 41Когда ты наденешь эти одежды на своего брата Аарона и его сыновей, помажь и посвяти их в сан. Освяти их, чтобы они могли служить Мне как священники.

42Сделай им льняное нижнее белье, чтобы прикрывать их от пояса до бедер. 43Аарон и его сыновья должны одевать его всегда, когда входят в шатер собрания или приближаются к жертвеннику, чтобы служить в святилище, тогда они не провинятся и не умрут. Это установление для Аарона и его потомков будет вечным.