Eksodo 26 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 26:1-37

Chihema cha Mapemphero

1“Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi. 2Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri. 3Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo. 4Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo. 5Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana. 6Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.

7“Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi. 8Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri. 9Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri. 10Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija. 11Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi. 12Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho. 13Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo. 14Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.

15“Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho. 16Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69. 17Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere. 18Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho. 19Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija. 20Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri. 21Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse. 22Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo. 23Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti. 24Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana. 25Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.

26“Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema, 27mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema. 28Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso. 29Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.

30“Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.

31“Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi. 32Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi. 33Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri. 34Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri. 35Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.

36“Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso. 37Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”

La Bible du Semeur

Exode 26:1-37

Les tentures du tabernacle

1Tu feras le tabernacle avec dix tentures de fin lin retors26.1 Tissé de fils de lin formés de plusieurs fils tordus ensemble, ce qui le rendait particulièrement résistant., de pourpre violette et écarlate, de rouge éclatant, ornées de chérubins dans les règles de l’art. 2Chaque tenture aura quatorze mètres de long et deux mètres de large26.2 Dans les chapitres 26 et 27, l’hébreu donne les mesures en coudées. Une coudée correspond à 50 centimètres. Certains n’attribuent que 44 ou 46 cm à la coudée, d’où les différences entre les versions modernes.. Elles seront toutes identiques. 3On coudra d’abord cinq de ces tentures l’une à l’autre, puis on fera de même pour les cinq autres26.3 La couverture du tabernacle était composée de dix bandes parallèles de deux mètres de large. Elles étaient cousues cinq par cinq, bord à bord, dans le sens de leur longueur formant ainsi deux grands tapis de quatorze mètres sur dix mètres, l’un pour recouvrir le lieu saint, l’autre le lieu très saint.. 4Sur le bord de la dernière tenture de chacun de ces assemblages, tu fixeras des cordons de pourpre violette. 5Il y en aura cinquante à l’extrémité de chacun des deux assemblages et les cordons se correspondront l’un à l’autre. 6Tu feras cinquante agrafes d’or au moyen desquelles tu assembleras les tentures, de sorte que le tabernacle forme un tout.

7Ensuite tu feras onze tentures de poil de chèvre, pour recouvrir le tabernacle comme d’une tente26.7 Au-dessus de ce tissu précieux venait une tenture faite en poil de chèvre comme en utilisent encore les Bédouins pour leurs tentes. Ces tentures avaient un mètre de plus que le tissu précédent, il y avait une bande de plus, donc elles débordaient de cinquante centimètres de chaque côté et d’un mètre sur l’arrière (voir v. 12-13).. 8Chacune d’elles aura quinze mètres de long et deux mètres de large. Elles seront toutes identiques. 9Tu les assembleras, cinq d’une part, six de l’autre, et tu rabattras la sixième sur le devant de la tente. 10Tu fixeras cinquante cordons sur le bord de la dernière tenture de chaque assemblage 11et tu feras cinquante agrafes de bronze dans lesquelles tu introduiras les cordons pour assembler la tente, afin qu’elle forme un tout. 12Le pan supplémentaire des tentures de la tente – c’est-à-dire la moitié de l’assemblage des tentures qui sera en surplus – retombera librement sur l’arrière du tabernacle. 13De même, le demi-mètre en surplus sur la longueur des tentures de la tente pendra librement de chaque côté du tabernacle pour bien le couvrir. 14Tu mettras sur la tente une couverture de peaux de béliers teintes en rouge et une couverture de peaux de dauphins par-dessus.

L’armature du tabernacle

15Tu feras pour le tabernacle des cadres en bois d’acacia qui seront posés debout. 16Chaque cadre aura cinq mètres de long et soixante-quinze centimètres de large, 17et sera muni de deux tenons parallèles. Tu feras ainsi pour tous les cadres du tabernacle. 18Tu feras vingt cadres pour le côté sud du tabernacle. 19Pour chacun d’eux, tu disposeras deux socles d’argent, un pour chaque tenon, soit quarante socles d’argent pour les vingt cadres. 20Tu feras de même pour le second côté du tabernacle, le côté nord : vingt cadres, 21supportés par quarante socles d’argent, à raison de deux par cadre. 22Pour l’arrière du tabernacle, tourné vers l’ouest, tu prépareras six cadres. 23Tu ajouteras deux cadres comme contreforts des angles arrières du tabernacle : 24chacun sera jumelé avec l’un des cadres des extrémités, depuis le bas, et bien lié avec lui jusqu’à son sommet par un seul anneau ; les deux contreforts d’angles seront identiques. 25Il y aura donc en tout huit cadres avec leurs seize socles d’argent, deux sous chaque cadre.

26Tu feras cinq traverses de bois d’acacia pour les cadres d’un des côtés du tabernacle, 27cinq pour l’autre côté et cinq pour le fond à l’ouest. 28La traverse médiane, au milieu des cadres, courra d’une extrémité à l’autre du tabernacle. 29Tu plaqueras d’or tous les cadres et tu fabriqueras des anneaux d’or pour recevoir les traverses que tu plaqueras également d’or. 30Tu dresseras le tabernacle selon la manière qui t’est montrée sur la montagne.

Le voile

31Tu feras un voile de pourpre violette et écarlate, de rouge éclatant et de fin lin retors, orné de chérubins, dans les règles de l’art. 32Tu le suspendras à quatre piliers d’acacia plaqués d’or, munis de crochets d’or et posés sur quatre socles d’argent. 33Tu fixeras le voile sous les agrafes.

C’est là, derrière le voile, que tu déposeras le coffre contenant l’acte de l’alliance. Ce voile vous servira de séparation entre le lieu saint et le lieu très saint26.33 Seul le grand-prêtre avait le droit de franchir ce voile, une fois par an, le jour des Expiations (Lv 16 ; Hé 9.2-14). Au moment de la mort de Christ, c’est probablement ce voile qui s’est déchiré dans le Temple, indiquant qu’à présent tout croyant avait directement accès auprès de Dieu (Mt 27.51 ; Mc 15.38 ; voir Hé 6.19-20 ; 9.3-5 ; 10.19-22).. 34Tu poseras le propitiatoire sur le coffre de l’acte de l’alliance dans le lieu très saint. 35Tu disposeras la table à l’extérieur26.35 C’est-à-dire la table sur laquelle étaient déposés les pains exposés devant l’Eternel (25.23-30). Dans le lieu très saint, il n’y avait que le coffre de l’alliance ; dans le lieu saint, cette table, le chandelier d’or et l’autel d’encens., devant le voile, du côté nord du tabernacle, et le chandelier face à la table, du côté sud. 36Tu confectionneras pour l’entrée de la tente un rideau de pourpre violette et écarlate, de rouge éclatant et de fin lin retors, en ouvrage de broderie. 37Tu feras pour le rideau cinq piliers en acacia et tu les plaqueras d’or, tu les muniras de crochets en or, puis tu couleras pour ces piliers cinq socles de bronze.