Eksodo 24 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 24:1-18

Kutsimikizira kwa Pangano

1Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali. 2Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”

3Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.” 4Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena.

Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli. 5Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano. 6Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe. 7Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”

8Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”

9Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri, 10ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo. 11Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.

12Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”

13Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa. 14Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”

15Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo. 16Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo. 17Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo. 18Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.

La Bible du Semeur

Exode 24:1-18

Conclusion de l’alliance avec Israël

1Dieu dit à Moïse : Monte vers l’Eternel, et prends avec toi Aaron, Nadab, Abihou24.1 Les deux fils aînés d’Aaron qui auraient dû lui succéder dans l’office de grand-prêtre, mais ils ont offert un feu profane sur l’autel et ont été frappés par Dieu (Lv 10.1-2 ; Nb 3.4). et soixante-dix des responsables d’Israël24.1 Il ne s’agit donc pas de tous les responsables du peuple. Le nombre soixante-dix renvoie peut-être au nombre des personnes composant la famille d’Israël lors de sa venue en Egypte (1.5) à moins qu’il ne symbolise la plénitude (sept) multipliée par dix (grand nombre).. Vous vous prosternerez de loin. 2Toi, Moïse, tu t’approcheras seul de moi ; les autres ne s’approcheront pas, et l’ensemble du peuple ne montera pas avec toi.

3Moïse alla rapporter au peuple toutes les paroles de l’Eternel et toutes ses lois. Et tout le peuple s’écria d’une seule voix : Nous ferons tout ce que l’Eternel a dit.

4Moïse mit par écrit toutes les paroles de l’Eternel. Le lendemain, de bonne heure, il bâtit un autel au pied de la montagne et dressa douze stèles pour les douze tribus d’Israël. 5Puis il chargea les jeunes gens d’Israël d’offrir à l’Eternel des holocaustes et des taureaux en sacrifices de communion. 6Il recueillit la moitié du sang versé dans des récipients et répandit l’autre moitié sur l’autel. 7Puis il prit le livre de l’alliance24.7 Le livre qui vient d’être écrit (v. 4). et le lut à haute voix au peuple. Les Israélites déclarèrent : Nous ferons tout ce que l’Eternel a dit, nous obéirons à toutes ses paroles.

8Alors Moïse prit le sang et en aspergea le peuple en disant : C’est le sang de l’alliance que l’Eternel a conclue avec vous, sur la base de toutes ces paroles24.8 Jésus semble avoir fait allusion à ces paroles en instituant la cène (Mt 26.28 ; Mc 14.24 ; Lc 22.20 ; 1 Co 11.25) ; voir Hé 9.19-20 ; 10.29..

9Ensuite Moïse gravit la montagne avec Aaron, Nadab, Abihou et soixante-dix responsables d’Israël. 10Ils virent le Dieu d’Israël. Sous ses pieds s’étendait comme une plateforme de saphirs aussi purs que le fond du ciel24.10 Voir Ap 4.6.. 11L’Eternel n’étendit pas la main sur ces notables des Israélites ; ils contemplèrent Dieu et puis ils mangèrent et burent.

Moïse entre dans la présence de l’Eternel

12L’Eternel dit à Moïse : Monte vers moi sur la montagne et tiens-toi là. Je te donnerai les tables de pierre sur lesquelles j’ai transcrit la Loi et les commandements pour que tu les enseignes au peuple.

13Moïse se mit en route avec Josué, son assistant, et gravit la montagne de Dieu 14après avoir dit aux responsables d’Israël : Attendez-nous ici jusqu’à notre retour. Aaron et Hour resteront avec vous. Si quelqu’un a un problème à régler, qu’il s’adresse à eux.

15Moïse monta sur la montagne et la nuée la recouvrit. 16La gloire de l’Eternel demeura sur le mont Sinaï et la nuée le recouvrit pendant six jours. Le septième jour, l’Eternel appela Moïse du milieu de la nuée. 17La gloire de l’Eternel apparaissait aux Israélites comme un feu au sommet de la montagne. 18Moïse pénétra dans la nuée et monta plus haut sur la montagne. Il y demeura quarante jours et quarante nuits.