Eksodo 20 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 20:1-26

Malamulo Khumi

1Ndipo Mulungu anayankhula mawu onse awa nati:

2“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.

3“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.”

4“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko. 5Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane. 6Koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda, ndi kusunga malamulo anga.

7“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.

8“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika. 9Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi. 10Koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi, wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu, ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu. 11Pakuti Yehova anapanga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo mʼmasiku asanu ndi limodzi. Iye anapuma pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Kotero Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale loyera.

12“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako kuti ukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.

13“Usaphe.

14“Usachite chigololo.

15“Usabe.

16“Usapereke umboni womunamizira mnzako.

17“Usasirire nyumba ya mnzako. Usasirire mkazi wa mnzako kapena wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”

18Pamene anthu ankamva mabingu ndi kuona ziphaliwali ndi kumvanso lipenga ndi kuona utsi umene umafuka mʼphiri, ananjenjemera ndi mantha. Ndipo iwo anayima patali. 19Ndipo anati kwa Mose, “Iwe utiyankhule ndipo tidzamvera. Koma usalole kuti Mulungu atiyankhule, tingafe.”

20Koma Mose anati kwa anthuwo, “Musachite mantha. Mulungu wabwera kudzakuyesani kuti mukhale ndi mtima woopa Mulungu kuti musamuchimwire.”

21Anthu aja anayima patali koma Mose anayandikira mtambo wakuda kumene kunali Mulungu.

Za Mafano ndi Maguwa Ansembe

22Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Awuze izi Aisraeli: ‘Inu mwaona nokha kuti Ine ndakuyankhulani kuchokera kumwamba. 23Choncho musadzipangire milungu yasiliva kapena yagolide kuti muziyipembedza pamodzi ndi Ine.’ ”

24Mundimangire guwa ladothi ndipo muziperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe zanu. Pamalo paliponse pamene Ine ndidzakonza kuti muzinditamandirapo, ndidzabwera ndi kukudalitsani. 25Ngati mudzandimangira guwa lansembe lamiyala, musagwiritse ntchito miyala yosema, pakuti mudzalidetsa mukadzagwiritsa ntchito zida. 26Musamakwere pa makwerero popita pa guwa langa lansembe kuti mungaonetse maliseche anu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Исход 20:1-26

Десять повелений

(Втор. 5:5-33)

1Всевышний сказал такие слова:

2– Я Вечный, твой Бог, Который вывел тебя из Египта, земли рабства.

3Пусть не будет у тебя других богов, кроме Меня.

4Не делай себе идола – никакого изображения того, что на небе вверху, или на земле внизу, или в водах ниже земли. 5Не поклоняйся им и не служи им, ведь Я, Вечный, твой Бог – ревнивый Бог, наказывающий детей за грехи отцов до третьего и четвёртого поколения тех, кто ненавидит Меня. 6Но Я дарую любовь тысячам поколений тех, кто20:6 Или: «тысячам тех, кто…» любит Меня и соблюдает Мои повеления.

7Не произноси имени Вечного, твоего Бога, напрасно, потому что Вечный не оставит безнаказанным никого, кто произносит Его имя напрасно.

8Помни субботний день и храни его святым. 9Шесть дней трудись и делай всю свою работу, 10но седьмой день – это суббота, она принадлежит Вечному, твоему Богу. Не делай в этот день никакой работы – ни ты, ни твой сын или дочь, ни слуга или служанка, ни твой скот, ни чужеземец в твоих городах. 11За шесть дней Вечный сотворил небеса и землю, море и всё, что в них, а на седьмой – отдыхал. Поэтому Вечный благословил субботний день и освятил его.

12Почитай отца и мать, чтобы тебе долго жить на земле, которую даёт тебе Вечный, твой Бог.

13Не убивай.

14Не нарушай супружескую верность.

15Не кради.

16Не лжесвидетельствуй.

17Не желай дома ближнего твоего. Не желай жены ближнего твоего, его слуги или служанки, его вола или осла: ничего из того, что принадлежит ближнему твоему.

18Когда люди увидели гром и молнию, услышали трубный звук и увидели гору в дыму, они задрожали от страха. Они встали поодаль 19и сказали Мусо:

– Говори с нами ты сам, а мы будем слушать. Пусть Всевышний не говорит с нами, иначе мы умрём.

20Мусо сказал народу:

– Не бойтесь. Всевышний пришёл испытать вас, чтобы вы исполнились страха перед Ним и не грешили.

21Народ остался стоять поодаль, а Мусо приблизился к тёмному облаку, где был Всевышний.

Закон о жертвеннике

22Вечный сказал Мусо:

– Скажи исроильтянам: «Вы сами видели, что Я говорил с вами с небес: 23не делайте себе серебряных или золотых богов и не поклоняйтесь им вместо Меня».

24Сделайте Мне жертвенник из земли и приносите на нём овец и волов в жертву всесожжения и в жертву примирения. На всяком месте, где Я повелю вам чтить Меня, Я приду к вам и благословлю вас. 25Если вы захотите сделать Мне каменный жертвенник, не стройте его из тёсаных камней. Вы оскверните камень, прикоснувшись к нему резцом. 26Не поднимайтесь к Моему жертвеннику по ступеням, чтобы не открылась перед ним ваша нагота.