Eksodo 2 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 2:1-25

Kubadwa kwa Mose

1Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo. 2Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu. 3Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo. 4Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.

5Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge. 6Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”

7Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”

8Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo. 9Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera. 10Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”

Mose Athawira ku Midiyani

11Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake. 12Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga. 13Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”

14Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”

15Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime. 16Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo. 17Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.

18Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”

19Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”

20Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”

21Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake. 22Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”

23Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu. 24Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 25Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Исход 2:1-25

Рождение пророка Мусо

1Один человек из рода Леви взял себе жену из того же рода. 2Она забеременела и родила сына. Увидев, какой это красивый ребёнок, она прятала его три месяца, 3а когда не смогла больше прятать, взяла тростниковую корзину и покрыла её смолой и дёгтем. Она положила в неё младенца и поставила её среди тростника на берегу Нила. 4Сестра младенца встала поодаль, чтобы увидеть, что с ним случится. 5Дочь фараона спустилась к Нилу купаться, а её служанки ходили по берегу. Она увидела корзину среди тростника и послала за ней рабыню. 6Открыв корзину, дочь фараона увидела младенца. Он плакал, и она пожалела его.

– Это один из еврейских детей, – сказала она.

7Тогда сестра младенца подошла и спросила у дочери фараона:

– Может, пойти и привести кормилицу из евреек, чтобы она вскормила для тебя младенца?

8– Да, пойди, – ответила та.

Девочка пошла и привела мать младенца.

9Дочь фараона сказала ей:

– Возьми этого младенца и вскорми его для меня, а я тебе заплачу за это.

Женщина взяла младенца и вскормила его. 10Когда ребёнок подрос, она отвела его к дочери фараона, и та усыновила мальчика. Она назвала его Мусо («вытащить»)2:10 О переводе имён и названий см. приложение VI., говоря: «Я вытащила его из воды».

Бегство Мусо в Мадиан

11Однажды, когда Мусо уже вырос, он пошёл к своим соплеменникам и увидел, какую тяжёлую работу они делают. Он увидел, как египтянин бьёт еврея – его соплеменника. 12Оглянувшись вокруг и увидев, что никого нет, Мусо убил египтянина и спрятал его тело в песке.

13На следующий день он увидел двух дерущихся евреев. Он спросил обидчика:

– Зачем ты бьёшь своего соплеменника?

14Тот ответил:

– Кто поставил тебя начальником и судьёй над нами? Не думаешь ли ты убить и меня, как убил египтянина?

Мусо испугался и подумал: «Должно быть, то, что я сделал, стало известно».

15Услышав об этом, фараон хотел казнить Мусо, но Мусо убежал от него и поселился в стране мадианитян. Однажды, когда он сидел у колодца, 16семь дочерей мадианского жреца пришли начерпать воды, чтобы наполнить поилки и напоить отару отца. 17Но пришли пастухи и отогнали их, тогда Мусо встал, защитил дочерей жреца и напоил их овец.

18Когда девушки вернулись к своему отцу Иофору2:18 Букв.: «Рагуил». Рагуил – второе имя Иофора., тот спросил:

– Почему вы сегодня так рано вернулись?

19Они ответили:

– Какой-то египтянин защитил нас от пастухов. Он даже начерпал нам воды и напоил отару овец.

20– Где же он? – спросил отец у дочерей. – Почему вы оставили его? Пригласите его поесть с нами.

21Мусо решил остаться у этого человека, и тот отдал свою дочь Ципору Мусо в жёны. 22Она родила сына, и Мусо назвал его Гершом («чужестранец там»), говоря: «Я стал поселенцем в чужой земле».

23Спустя долгое время царь Египта умер. Исроильтяне стонали в рабстве и взывали о помощи. Вопль об их рабской доле дошёл до Всевышнего, 24и Всевышний, услышав их стоны, вспомнил Своё соглашение с Иброхимом, Исхоком и Якубом. 25Всевышний посмотрел на исроильтян и пожалел их.