Eksodo 16 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 16:1-36

Mana ndi Zinziri

1Pambuyo pake gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Elimu, ndipo pa tsiku la khumi ndi chisanu mwezi wachiwiri chichokere mʼdziko la Igupto, anafika ku chipululu cha Sini chimene chinali pakati pa Elimu ndi Sinai. 2Mʼchipululumo gulu lonse linadandaulira Mose ndi Aaroni 3kuti, “Kukanakhala bwino Yehova akanatiphera mʼdziko la Igupto! Kumeneko timadya nyama ndi buledi mpaka kukhuta, koma inu mwabwera nafe ku chipululu kudzapha mpingo wonsewu ndi njala!”

4Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzakupatsani buledi wogwa kuchokera kumwamba ngati mvula. Anthu azituluka tsiku lililonse kukatola buledi wokwanira tsiku limenelo. Ine ndidzawayesa mʼnjira imeneyi kuti ndione ngati adzatsatira malangizo anga. 5Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, pamene azidzakonza buledi amene abwera naye, adzapeza kuti ndi wokwanira masiku awiri.”

6Kotero Mose ndi Aaroni anati kwa Aisraeli onse, “Nthawi yamadzulo inu mudzadziwa kuti ndi Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto. 7Ndipo mmawa mudzaona ulemerero wa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu. Kodi ife ndi yani kuti muzitidandaulira?” 8Mose anati, “Yehova adzakupatsani nyama madzulo aliwonse ndi buledi mmawa uliwonse kuti mukhute chifukwa Iye wamva madandawulo anu. Nanga ife ndi yani? Kudandaula kwanu simudandaulira ife, koma Yehova.”

9Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Bwerani pamaso pa Yehova pakuti wamva kudandaula kwanu.’ ”

10Pamene Aaroni amayankhula ndi gulu lonse la Aisraeli, iwo anayangʼana ku chipululu, ndipo ulemerero wa Yehova umaoneka mu mtambo.

11Yehova anati kwa Mose, 12“Ine ndamva kudandaula kwa Aisraeli. Awuze kuti, ‘Madzulo mudzadya nyama ndipo mmawa mudzakhuta buledi. Pamenepo mudzadziwa kuti ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

13Madzulo amenewo panatuluka zinziri zimene zinali ponseponse pa misasa yawo, ndipo mmawa panali mame kuzungulira misasa yawo. 14Mamewo atachoka, pa nthaka mʼchipululumo panaoneka tinthu tina topyapyala komanso totuwa ngati chipale. 15Aisraeli atationa anafunsana wina ndi mnzake nati, “Kodi timeneti nʼchiyani?” Popeza sanatidziwe.

Mose anawawuza kuti, “Uyu ndi buledi amene Yehova wakupatsani kuti mudye. 16Yehova walamula kuti, ‘Aliyense atole zomukwanira kudya, malita awiri pa munthu mmodzi molingana ndi chiwerengero cha anthu amene ali mu tenti yanu.’ ”

17Aisraeli anachita zonse anawawuza. Ena anatola zambiri ena zochepa. 18Ndipo iwo atayeza ndi muyeso wa malita awiri, iye amene anatola zambiri sizinamutsalireko ndipo amene anatola pangʼono sizinamuchepere. Aliyense anatola zomukwanira kudya.

19Ndipo Mose anawawuza kuti, “Wina aliyense asasunge mpaka mmawa.”

20Komabe ena sanamvere Mose, anasungako mpaka mmawa. Koma mmawa mwake tonse tinali mphutsi zokhazokha. Kotero Mose anawapsera mtima.

21Mmawa uliwonse aliyense amatola zimene amazifuna, ndipo dzuwa likatentha zimasungunuka. 22Tsiku lachisanu ndi chimodzi anatuta malita anayi munthu aliyense, ndipo atsogoleri a mpingo wonse anabwera kudzawuza Mose za zimenezi. 23Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova analamula, ‘Mawa ndi tsiku lopumula, Sabata Loyera la Yehova, choncho wotchani ndi kuphika zimene mukufuna. Sungani zotsala mpaka mmawa.’ ”

24Choncho anasunga mpaka mmawa monga Mose anawalamulira, ndipo sananunkhe kapena kuchita mphutsi. 25Mose anati, “Idyani lero chifukwa lero ndi Sabata la Yehova. Lero simukapeza chilichonse kunjaku. 26Muzitola chakudya masiku asanu ndi limodzi koma tsiku la chisanu ndi chiwiri ndi la Sabata, simukapeza chilichonse kunjaku.”

27Komabe anthu ena anapita kuti akatole chakudya tsiku lachisanu ndi chiwiri, koma sanapeze kanthu. 28Ndipo Yehova anafunsa Mose nati, “Kodi inu muzipitirira kukana kusunga malamulo ndi malangizo anga mpaka liti? 29Taonani, popeza Yehova wakupatsani Sabata nʼchifukwa chake tsiku lachisanu ndi chimodzi amakupatsani chakudya cha masiku awiri. Aliyense azikhala pamene ali pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, pasapezeke wotuluka kunja.” 30Kotero anthu anapuma tsiku lachisanu ndi chiwiri.

31Aisraeli anatchula chakudyacho Mana. Chakudyacho chinkaoneka ngati mbewu zamapira, zoyera. Ndipo chinkakoma ngati chothira uchi. 32Mose anati, “Chimene Yehova walamula ndi ichi: ‘Tengani muyeso wa malita awiri a mana ndi kusungira mibado imene ikubwera, kuti iwo adzaone chakudya chimene Ine ndinakupatsani kuti mudye mʼchipululu pamene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.’ ”

33Choncho Mose anati kwa Aaroni, “Tenga mtsuko ndipo uyikemo malita awiri a mana. Ndipo uyike manawo pamaso pa Yehova kusungira mibado imene ikubwera.”

34Monga momwe Yehova analamulira Mose, Aaroni anayika mtsuko uja pafupi ndi bokosi la Chipangano kuti manawo asungike. 35Aisraeli anadya mana zaka 40, mpaka pamene anafika ku dziko kumene amati akakhazikeko. Iwo anadya mana mpaka pamene anafika mʼmalire a Kanaani.

36(Malita awiri amafanana ndi gawo lakhumi la efa).

New Russian Translation

Исход 16:1-36

Манна и перепела

1Народ Израиля тронулся в путь из Елима и на пятнадцатый день второго месяца после ухода из Египта пришел в пустыню Син, что между Елимом и Синаем. 2В пустыне народ стал роптать на Моисея и Аарона. 3Израильтяне говорили им:

– Лучше бы нам было умереть в Египте от руки Господа! Там мы сидели у котлов с мясом и ели хлеб досыта. А вы вывели нас в пустыню, чтобы весь народ уморить голодом.

4Господь сказал Моисею:

– Я осыплю вас хлебом с неба. Пусть народ выходит каждый день и собирает, сколько нужно на день. Так Я испытаю их, будут ли они следовать Моим наставлениям. 5На шестой день пусть они соберут вдвое больше, чем в прочие дни, и заготовят это впрок.

6Моисей и Аарон сказали израильтянам:

– Вечером вы узнаете, что из Египта вас вывел Господь, 7а утром увидите славу Господа, потому что Он услышал ваш ропот на Него. Кто мы такие, чтобы вам роптать на нас?

8Еще Моисей сказал:

– Вот как вы узнаете, что это был Господь: этим вечером Он накормит вас мясом, а утром даст вам вдоволь хлеба. Он услышал ваш ропот на Него. Кто мы такие? Вы ропщете не на нас, а на Господа.

9Моисей сказал Аарону:

– Скажи обществу израильскому: «Предстаньте пред Господом, потому что Он услышал ваш ропот».

10Когда Аарон говорил с народом израильским, они повернулись к пустыне и увидели, как слава Господа явилась в облаке.

11Господь сказал Моисею:

12– Я услышал ропот израильтян. Скажи им: «К сумеркам вы будете есть мясо, а утром наедитесь хлеба. Тогда вы узнаете, что Я – Господь, ваш Бог».

13В тот же вечер налетели перепела и накрыли лагерь, а утром вокруг лагеря легла роса. 14Когда роса сошла, на поверхности пустыни показались тонкие хлопья, похожие на иней. 15Увидев их, израильтяне говорили друг другу:

– Что это?

Они не знали, что это такое. Моисей сказал им:

– Это хлеб, который Господь дал вам в пищу. 16Господь повелел: «Пусть каждый собирает, сколько ему нужно. Берите по омеру16:16 Возможно, около 2 л; также в ст. 18, 32, 33 и 36. на каждого члена семьи».

17Израильтяне сделали так, как им сказали. Одни собрали больше, другие – меньше. 18Но когда они измерили омером, то у того, кто собрал много, не было излишка, и у того, кто собрал мало, не было недостатка. Каждый собрал столько, сколько ему было нужно.

19Моисей сказал им:

– Пусть никто ничего не оставляет до утра.

20Но некоторые не послушали Моисея и оставили часть до утра. В пище завелись черви, и она стала зловонной. Моисей разгневался на них.

21Утром каждый собирал, сколько ему было нужно, а когда пригревало солнце, оно таяло. 22На шестой день они собрали в два раза больше – по два омера16:22 Возможно, около 4 л. на человека – и вожди народа пришли и доложили об этом Моисею.

23Он сказал им:

– Господь повелел: «Завтра – день покоя, святая суббота Господа. Испеките сейчас то, что хотите испечь, и сварите то, что хотите сварить. То, что останется, нужно отложить и сохранить до утра».

24Они сохранили это до утра, как повелел Моисей, и оно не начало портиться, и черви в нем не завелись.

25– Ешьте это сегодня, – сказал Моисей, – потому что сегодня суббота Господня. Сегодня вы ничего не найдете на земле. 26Вы будете собирать хлопья шесть дней, но на седьмой день, в субботу, ничего не будет.

27Некоторые из народа вышли собирать в седьмой день, но ничего не нашли. 28Господь сказал Моисею:

– Сколько еще вы будете нарушать Мои повеления и наставления? 29Запомните: Господь дал вам субботу, и поэтому в шестой день дает вам хлеб на два дня. Пусть в седьмой день каждый остается там, где он есть. Пусть никто не выходит из дома.

30И в седьмой день народ пребывал в покое.

31Народ Израиля назвал эту пищу манной16:31 Манна – переводится как: «Что это?» (см. 16:15).. Она была белой, как кориандровое семя, а на вкус – как медовое печенье. 32Моисей сказал:

– Так повелел Господь: «Возьмите омер манны и храните для грядущих поколений, чтобы они могли видеть хлеб, которым Я кормил вас в пустыне, когда вывел из Египта».

33Моисей сказал Аарону:

– Возьми кувшин и наполни его омером манны. Поставь его перед Господом, чтобы сохранить для грядущих поколений.

34Как Господь повелел Моисею, Аарон поставил кувшин с манной перед ковчегом свидетельства, чтобы хранить. 35Израильтяне ели манну сорок лет, пока не пришли в заселенную землю. Они ели манну, пока не достигли рубежей Ханаана.

36(Мера омер составляет одну десятую часть ефы16:36 Ефа – это мера объема, равная 22 л.).